Add parallel Print Page Options

Davide Adzozedwa Kukhala Mfumu ya Israeli

11 Aisraeli onse anasonkhana pamaso pa Davide ku Hebroni ndipo anati, “Ife ndife abale anu. Kale lija, ngakhale pamene Sauli anali mfumu, inu ndinu amene munkatsogolera Aisraeli pa nkhondo zawo. Ndipo Yehova Mulungu wanu anakuwuzani kuti, ‘Iwe udzaweta anthu anga Aisraeli, ndipo udzakhala mfumu yawo.’ ”

Akuluakulu onse a Israeli atafika kwa Mfumu Davide ku Hebroni, iye anachita nawo pangano pamaso pa Yehova, ndipo anamudzoza Davide kukhala mfumu ya Israeli, monga momwe Yehova analonjezera kudzera mwa Samueli.

Davide Agonjetsa Yerusalemu

Davide ndi Aisraeli onse anapita ku Yerusalemu (ku Yebusi). Ayebusi amene ankakhala kumeneko anamuwuza Davide kuti, “Simulowa muno.” Komabe Davide analanda linga la Ziyoni, limene ndi mzinda wa Davide.

Davide anali atanena kuti “Aliyense amene adzatsogolere kukathira nkhondo Ayebusi adzakhala mkulu wa asilikali.” Yowabu mwana wa Zeruya ndiye anayamba kupita, motero anakhala mkulu wa asilikali.

Tsono Davide anakhazikika mu lingamo, ndipo mzindawu anawutcha Mzinda wa Davide. Iye anamanga malo onse ozungulira, kuyambira ku matsitso ozungulira khoma. Ndipo Yowabu anakonzanso mbali ina ya mzindawu. Ndipo mphamvu za Davide zinkakulirakulira chifukwa anali ndi Yehova Wamphamvuzonse.

Asilikali Otchuka a Davide

10 Awa ndiye anali atsogoleri amphamvu a Davide. Iwo pamodzi ndi Aisraeli onse, anathandiza kulimbikitsa ufumu wake kuti ukwanire madera onse, monga momwe Yehova analonjezera. 11 Nawa mayina a ankhondo amphamvu a Davide:

Yasobeamu Mhakimoni anali mkulu wa atsogoleri. Iye anapha ndi mkondo ankhondo 300 nthawi imodzi.

12 Wotsatana naye anali Eliezara mwana wa Dodo Mwahohi, mmodzi mwa ankhondo atatu amphamvu. 13 Iye anali ndi Davide ku Pasi-Damimu pamene Afilisti anasonkhana kudzachita nkhondo. Ankhondo anathawa Afilistiwo pamalo pamene panali munda wodzaza ndi barele. 14 Koma awiriwo anayima pakati pa mundawo. Iwo anawuteteza, nakantha Afilistiwo ndipo Yehova anawapambanitsa koposa.

15 Atatu mwa atsogoleri makumi atatu aja anabwera kwa Davide ku thanthwe ku phanga la Adulamu pamene gulu la Afilisti linali litamanga misasa mʼchigwa cha Refaimu. 16 Nthawi imeneyo Davide anali mu linga, ndipo boma la Afilisti linali ku Betelehemu. 17 Davide analakalaka madzi ndipo anati, “Haa, pakanapezeka munthu wokanditungira madzi a mʼchitsime chomwe chili pafupi ndi chipata cha ku Betelehemu!” 18 Choncho anthu atatuwa anadutsa mizere ya Afilisti, natunga madzi amene anali mʼchitsime chomwe chinali pafupi ndi chipata cha ku Betelehemu nabwera nawo kwa Davide. Koma iye anakana kumwa. Mʼmalo mwake anathira pansi pamaso pa Yehova. 19 Iye anati, “Inu Mulungu, musalole kuti ine ndichite chinthu ichi! Kodi ndimwe magazi a anthu amene anayika miyoyo yawo pachiswe?” Chifukwa iwo anayika miyoyo yawo pachiswe kuti abweretse madziwo, Davide sanamwe.

Zimenezi ndi zimene anachita anthu amphamvu atatuwo.

20 Abisai mʼbale wa Yowabu ndiye anali mtsogoleri wa anthu atatuwa. Iye anapha ndi mkondo ankhondo 300. Choncho iyeyo anali wotchuka pakati pa anthu atatu aja. 21 Iye analandira ulemu woposa atatuwo. Kotero anakhala mtsogoleri wawo ngakhale kuti iyeyo sanali mʼgulu la anthu atatu aja.

22 Benaya mwana wa Yehoyada wa ku Kabizeeli anali munthu wolimba mtima amene anachita zinthu zamphamvu. Iye anakantha ankhondo awiri otchuka a ku Mowabu. Tsiku lina kukuzizira kwambiri, iye analowa mʼdzenje ndi kuphamo mkango. 23 Ndipo iye anakanthanso Mwigupto amene anali wotalika mamita awiri ndi theka. Ngakhale kuti Mwiguptoyo anali ndi mkondo wofanana ndi ndodo yowombera nsalu mʼdzanja mwake, Benaya anapita kukamenyana naye ali ndi chibonga chokha mʼmanja. Iye analanda mkondo mʼdzanja la Mwiguptoyo ndi kumupha ndi mkondo wake womwe. 24 Izi ndi zamphamvu zimene Benaya mwana wa Yehoyada anachita. Iyeyo analinso wotchuka ngati anthu atatu amphamvu aja. 25 Iye ankalemekezedwa kuposa wina aliyense mwa anthu makumi atatu, koma sanali mʼgulu la anthu atatu aja. Ndipo Davide anamuyika kukhala woyangʼanira asilikali omuteteza.

26 Ankhondo amphamvuwa anali:

Asaheli mʼbale wa Yowabu,

Elihanani mwana wa Dodo wa ku Betelehemu,

27 Samoti Mharori,

Helezi Mpeloni.

28 Ira mwana wa Ikesi wa ku Tekowa,

Abiezeri wa ku Anatoti,

29 Sibekai Mhusati,

Ilai Mwahohi,

30 Maharai Mnetofa,

Heledi mwana wa Baana Mnetofa,

31 Itai mwana wa Ribai wa ku Gibeya ku Benjamini,

Benaya Mpiratoni,

32 Hurai wa ku zigwa za Gaasi,

Abieli Mwaribati,

33 Azimaveti Mbaharumi,

Eliyahiba Msaaliboni,

34 ana a Hasemu Mgizoni,

Yonatani mwana wa Sage Mharari,

35 Ahiamu mwana wa Sakari Mharari,

Elifali mwana wa Uri,

36 Heferi Mmekerati,

Ahiya Mpeloni,

37 Heziro wa ku Karimeli

Naara mwana wa Ezibai,

38 Yoweli mʼbale wa Natani,

Mibihari mwana wa Hagiri,

39 Zeleki Mwamoni,

Naharai wa ku Beeroti, mnyamata wonyamula zida za Yowabu mwana wa Zeruya.

40 Ira Mwitiri,

Garebu Mwitiri,

41 Uriya Mhiti,

Zabadi mwana wa Ahilai,

42 Adina mwana wa Siza Mrubeni, amene anali mtsogoleri wa Arubeni ndi anthu makumi atatu pamodzi naye,

43 Hanani mwana wa Maaka,

Yehosafati Mmitini,

44 Uziya Mwasiterati,

Sama ndi Yeiyeli ana a Hotamu Mwaroeri,

45 Yediaeli mwana wa Simiri,

ndi Yoha Mtizi mʼbale wake,

46 Elieli Mhavati,

Yeribai ndi Yosaviya ana a Elinaamu,

Itima Mmowabu,

47 Elieli, Obedi ndi Yaasieli Mmeobai.

David Becomes King Over Israel(A)

11 All Israel(B) came together to David at Hebron(C) and said, “We are your own flesh and blood. In the past, even while Saul was king, you were the one who led Israel on their military campaigns.(D) And the Lord your God said to you, ‘You will shepherd(E) my people Israel, and you will become their ruler.(F)’”

When all the elders of Israel had come to King David at Hebron, he made a covenant with them at Hebron before the Lord, and they anointed(G) David king over Israel, as the Lord had promised through Samuel.

David Conquers Jerusalem(H)

David and all the Israelites marched to Jerusalem (that is, Jebus). The Jebusites(I) who lived there said to David, “You will not get in here.” Nevertheless, David captured the fortress of Zion—which is the City of David.

David had said, “Whoever leads the attack on the Jebusites will become commander in chief.” Joab(J) son of Zeruiah went up first, and so he received the command.

David then took up residence in the fortress, and so it was called the City of David. He built up the city around it, from the terraces[a](K) to the surrounding wall, while Joab restored the rest of the city. And David became more and more powerful,(L) because the Lord Almighty was with him.

David’s Mighty Warriors(M)

10 These were the chiefs of David’s mighty warriors—they, together with all Israel,(N) gave his kingship strong support to extend it over the whole land, as the Lord had promised(O) 11 this is the list of David’s mighty warriors:(P)

Jashobeam,[b] a Hakmonite, was chief of the officers[c]; he raised his spear against three hundred men, whom he killed in one encounter.

12 Next to him was Eleazar son of Dodai the Ahohite, one of the three mighty warriors. 13 He was with David at Pas Dammim when the Philistines gathered there for battle. At a place where there was a field full of barley, the troops fled from the Philistines. 14 But they took their stand in the middle of the field. They defended it and struck the Philistines down, and the Lord brought about a great victory.(Q)

15 Three of the thirty chiefs came down to David to the rock at the cave of Adullam, while a band of Philistines was encamped in the Valley(R) of Rephaim. 16 At that time David was in the stronghold,(S) and the Philistine garrison was at Bethlehem. 17 David longed for water and said, “Oh, that someone would get me a drink of water from the well near the gate of Bethlehem!” 18 So the Three broke through the Philistine lines, drew water from the well near the gate of Bethlehem and carried it back to David. But he refused to drink it; instead, he poured(T) it out to the Lord. 19 “God forbid that I should do this!” he said. “Should I drink the blood of these men who went at the risk of their lives?” Because they risked their lives to bring it back, David would not drink it.

Such were the exploits of the three mighty warriors.

20 Abishai(U) the brother of Joab was chief of the Three. He raised his spear against three hundred men, whom he killed, and so he became as famous as the Three. 21 He was doubly honored above the Three and became their commander, even though he was not included among them.

22 Benaiah son of Jehoiada, a valiant fighter from Kabzeel,(V) performed great exploits. He struck down Moab’s two mightiest warriors. He also went down into a pit on a snowy day and killed a lion.(W) 23 And he struck down an Egyptian who was five cubits[d] tall. Although the Egyptian had a spear like a weaver’s rod(X) in his hand, Benaiah went against him with a club. He snatched the spear from the Egyptian’s hand and killed him with his own spear. 24 Such were the exploits of Benaiah son of Jehoiada; he too was as famous as the three mighty warriors. 25 He was held in greater honor than any of the Thirty, but he was not included among the Three. And David put him in charge of his bodyguard.

26 The mighty warriors were:

Asahel(Y) the brother of Joab,

Elhanan son of Dodo from Bethlehem,

27 Shammoth(Z) the Harorite,

Helez the Pelonite,

28 Ira son of Ikkesh from Tekoa,

Abiezer(AA) from Anathoth,

29 Sibbekai(AB) the Hushathite,

Ilai the Ahohite,

30 Maharai the Netophathite,

Heled son of Baanah the Netophathite,

31 Ithai son of Ribai from Gibeah in Benjamin,

Benaiah(AC) the Pirathonite,(AD)

32 Hurai from the ravines of Gaash,

Abiel the Arbathite,

33 Azmaveth the Baharumite,

Eliahba the Shaalbonite,

34 the sons of Hashem the Gizonite,

Jonathan son of Shagee the Hararite,

35 Ahiam son of Sakar the Hararite,

Eliphal son of Ur,

36 Hepher the Mekerathite,

Ahijah the Pelonite,

37 Hezro the Carmelite,

Naarai son of Ezbai,

38 Joel the brother of Nathan,

Mibhar son of Hagri,

39 Zelek the Ammonite,

Naharai the Berothite, the armor-bearer of Joab son of Zeruiah,

40 Ira the Ithrite,

Gareb the Ithrite,

41 Uriah(AE) the Hittite,

Zabad(AF) son of Ahlai,

42 Adina son of Shiza the Reubenite, who was chief of the Reubenites, and the thirty with him,

43 Hanan son of Maakah,

Joshaphat the Mithnite,

44 Uzzia the Ashterathite,(AG)

Shama and Jeiel the sons of Hotham the Aroerite,

45 Jediael son of Shimri,

his brother Joha the Tizite,

46 Eliel the Mahavite,

Jeribai and Joshaviah the sons of Elnaam,

Ithmah the Moabite,

47 Eliel, Obed and Jaasiel the Mezobaite.

Footnotes

  1. 1 Chronicles 11:8 Or the Millo
  2. 1 Chronicles 11:11 Possibly a variant of Jashob-Baal
  3. 1 Chronicles 11:11 Or Thirty; some Septuagint manuscripts Three (see also 2 Samuel 23:8)
  4. 1 Chronicles 11:23 That is, about 7 feet 6 inches or about 2.3 meters