Add parallel Print Page Options

Nkhondo za Davide ndi Kupambana Kwake

18 Patapita nthawi, Davide anagonjetsa Afilisti ndipo anakhala pansi pa ulamuliro wake. Iye analanda Gati ndi midzi yake yozungulira mʼmanja mwa Afilistiwo.

Davide anagonjetsanso Amowabu, nakhala pansi pa ulamuliro wake ndipo ankapereka msonkho kwa iye.

Komanso Davide anagonjetsa Hadadezeri mfumu ya Zoba, mpaka ku Hamati, pamene anapita kukakhazikitsa ulamuliro wake mʼmbali mwa mtsinje wa Yufurate. Davide analanda magaleta 1,000, anthu okwera magaleta 7,000 pamodzi ndi asilikali oyenda pansi 20,000. Iye anadula mitsempha ya akavalo onse okoka magaleta, koma anasiyapo akavalo 100 okha.

Aramu wa ku Damasiko atabwera kudzathandiza Hadadezeri mfumu ya ku Zoba, Davide anakantha asilikali 22,000. Iye anakhazikitsa maboma mu ufumu wa Aramu wa ku Damasiko, ndipo Aaramu anakhala pansi pa ulamuliro wake ndipo ankapereka msonkho. Yehova ankamupatsa chipambano Davide kulikonse kumene ankapita.

Davide anatenga zishango zagolide zimene ankanyamula akuluakulu ankhondo a Hadadezeri ndi kubwera nazo ku Yerusalemu. Kuchokera ku Teba ndi Kuni, mizinda ya Hadadezeri, Davide anatengako mkuwa wambiri umene Solomoni anapangira chimbiya, zipilala ndi zida zosiyanasiyana zamkuwa.

Tou, mfumu ya Hamati atamva kuti Davide wagonjetsa gulu lonse lankhondo la Hadadezeri mfumu ya Zoba, 10 anatumiza mwana wake Hadoramu kwa mfumu Davide kukamulonjera ndi kukamuyamikira chifukwa cha kupambana kwake pa nkhondo yake ndi Hadadezeriyo, amene analinso pa nkhondo ndi Tou. Hadoramu anabweretsa ziwiya zosiyanasiyana zagolide, zasiliva ndi zamkuwa.

11 Mfumu Davide inapereka zinthu zimenezi kwa Yehova, monga anachitira ndi siliva ndi golide zochokera ku mayiko ena onse monga Edomu ndi Mowabu, Aamoni ndi Afilisti, ndi Aamaleki.

12 Abisai mwana wa Zeruya anakantha Aedomu 18,000 mu Chigwa cha Mchere. 13 Iye anayika maboma ku Edomu, ndipo Aedomu onse anakhala pansi pa Davide. Yehova ankapambanitsa Davide kulikonse kumene ankapita.

Akuluakulu a Davide

14 Davide analamulira dziko lonse la Israeli ndipo ankachita zonse mwachilungamo ndi molondola pamaso pa anthu ake onse. 15 Yowabu, mwana wa Zeruya anali mkulu wa ankhondo; Yehosafati mwana wa Ahiludi anali mlembi wa zochitika; 16 Zadoki, mwana wa Ahitubi ndi Ahimeleki mwana wa Abiatara anali ansembe; Savisa anali mlembi; 17 Benaya mwana wa Yehoyada anali mtsogoleri wa Akereti ndi Apeleti, ndipo ana a Davide anali alangizi a mfumu.

David’s Victories(A)

18 In the course of time, David defeated the Philistines and subdued them, and he took Gath and its surrounding villages from the control of the Philistines.

David also defeated the Moabites,(B) and they became subject to him and brought him tribute.

Moreover, David defeated Hadadezer king of Zobah,(C) in the vicinity of Hamath, when he went to set up his monument at[a] the Euphrates River.(D) David captured a thousand of his chariots, seven thousand charioteers and twenty thousand foot soldiers. He hamstrung(E) all but a hundred of the chariot horses.

When the Arameans of Damascus(F) came to help Hadadezer king of Zobah, David struck down twenty-two thousand of them. He put garrisons in the Aramean kingdom of Damascus, and the Arameans became subject to him and brought him tribute. The Lord gave David victory wherever he went.

David took the gold shields carried by the officers of Hadadezer and brought them to Jerusalem. From Tebah[b] and Kun, towns that belonged to Hadadezer, David took a great quantity of bronze, which Solomon used to make the bronze Sea,(G) the pillars and various bronze articles.

When Tou king of Hamath heard that David had defeated the entire army of Hadadezer king of Zobah, 10 he sent his son Hadoram to King David to greet him and congratulate him on his victory in battle over Hadadezer, who had been at war with Tou. Hadoram brought all kinds of articles of gold, of silver and of bronze.

11 King David dedicated these articles to the Lord, as he had done with the silver and gold he had taken from all these nations: Edom(H) and Moab, the Ammonites and the Philistines, and Amalek.(I)

12 Abishai son of Zeruiah struck down eighteen thousand Edomites(J) in the Valley of Salt. 13 He put garrisons in Edom, and all the Edomites became subject to David. The Lord gave David victory wherever he went.

David’s Officials(K)

14 David reigned(L) over all Israel,(M) doing what was just and right for all his people. 15 Joab(N) son of Zeruiah was over the army; Jehoshaphat son of Ahilud was recorder; 16 Zadok(O) son of Ahitub and Ahimelek[c](P) son of Abiathar were priests; Shavsha was secretary; 17 Benaiah son of Jehoiada was over the Kerethites and Pelethites;(Q) and David’s sons were chief officials at the king’s side.

Footnotes

  1. 1 Chronicles 18:3 Or to restore his control over
  2. 1 Chronicles 18:8 Hebrew Tibhath, a variant of Tebah
  3. 1 Chronicles 18:16 Some Hebrew manuscripts, Vulgate and Syriac (see also 2 Samuel 8:17); most Hebrew manuscripts Abimelek