Add parallel Print Page Options

Davide Alanda Raba

20 Nthawi ya mphukira, nthawi imene mafumu amapita ku nkhondo, Yowabu anatsogolera gulu la ankhondo. Iye anawononga Aamoni, kenaka anapita ku mzinda wa Raba ndipo anawuzungulira, koma Davide anatsala ku Yerusalemu. Yowabu anathira nkhondo mzinda wa Raba ndipo anawuwononga. Davide anachotsa chipewa chaufumu pamutu pa mfumu yawo. Chipewacho chinkalemera makilogalamu asanu agolide ndiponso chinali ndi miyala yokongola. Ndipo Davide anavala chipewacho. Iye anatenga katundu wambiri kuchokera mu mzindawo, ndipo anatulutsa anthu amene anali mʼmenemo, nawayika kuti azigwira ntchito ya macheka, yosula makasu ndi nkhwangwa. Davide anachita izi ndi mizinda yonse ya Aamoni. Kenaka Davide pamodzi ndi gulu lake lonse lankhondo anabwerera ku Yerusalemu.

Davide Achita Nkhondo ndi Afilisti

Patapita nthawi, nkhondo inayambika pakati pa Aisraeli ndi Afilisti ku Gezeri. Nthawi imeneyo Sibekai Mhusati anapha Sipai, mmodzi mwa zidzukulu za Arefai, ndipo Afilisti anagonja.

Pa nkhondo inanso ndi Afilisti, Elihanani mwana wa Yairi anapha Lahimi mʼbale wake wa Goliati Mgiti, amene mkondo wake unali ngati ndodo yowombera nsalu.

Pa nkhondo inanso imene inachitika ku Gati, panali munthu wina wamtali kwambiri, wa zala zisanu ndi chimodzi mʼmanja ndi mʼmapazi ndipo zonse pamodzi zinalipo 24. Iyenso anali chidzukulu cha Rafa. Pamene iye ankanyoza Aisraeli, Yonatani mwana wa Simea, mʼbale wake wa Davide anamupha.

Anthu amenewa anali zidzukulu za Rafa ku Gati, ndipo anaphedwa ndi Davide ndi ankhondo ake.

The Capture of Rabbah(A)

20 In the spring, at the time when kings go off to war, Joab led out the armed forces. He laid waste the land of the Ammonites and went to Rabbah(B) and besieged it, but David remained in Jerusalem. Joab attacked Rabbah and left it in ruins.(C) David took the crown from the head of their king[a]—its weight was found to be a talent[b] of gold, and it was set with precious stones—and it was placed on David’s head. He took a great quantity of plunder from the city and brought out the people who were there, consigning them to labor with saws and with iron picks and axes.(D) David did this to all the Ammonite towns. Then David and his entire army returned to Jerusalem.

War With the Philistines(E)

In the course of time, war broke out with the Philistines, at Gezer.(F) At that time Sibbekai the Hushathite killed Sippai, one of the descendants of the Rephaites,(G) and the Philistines were subjugated.

In another battle with the Philistines, Elhanan son of Jair killed Lahmi the brother of Goliath the Gittite, who had a spear with a shaft like a weaver’s rod.(H)

In still another battle, which took place at Gath, there was a huge man with six fingers on each hand and six toes on each foot—twenty-four in all. He also was descended from Rapha. When he taunted Israel, Jonathan son of Shimea, David’s brother, killed him.

These were descendants of Rapha in Gath, and they fell at the hands of David and his men.

Footnotes

  1. 1 Chronicles 20:2 Or of Milkom, that is, Molek
  2. 1 Chronicles 20:2 That is, about 75 pounds or about 34 kilograms