Add parallel Print Page Options

Magulu a Ansembe

24 Magulu a ana a Aaroni anali awa:

Ana a Aaroni anali Nadabu, Abihu, Eliezara ndi Itamara. Koma Nadabu ndi Abihu anamwalira abambo awo asanamwalire, ndipo analibe ana aamuna. Kotero Eliezara ndi Itamara ankatumikira monga ansembe. Mothandizidwa ndi Zadoki chidzukulu cha Eliezara ndi Ahimeleki chidzukulu cha Itamara, Davide anawagawa mʼmagulu molingana ndi ntchito yawo yotumikira. Atsogoleri ambiri anapezeka pakati pa zidzukulu za Eliezara kusiyana ndi zidzukulu za Itamara ndipo anagawidwa moyenera: atsogoleri 16 a mabanja ochokera kwa Eliezara, ndipo atsogoleri asanu ndi atatu a mabanja ochokera kwa zidzukulu za Itamara. Anawagawa mosakondera pochita maere, pakuti iwo anali akuluakulu a ku malo opatulika ndi akuluakulu a Mulungu pakati pa zidzukulu za Eliezara ndi Itamara.

Mlembi Semaya mwana wa Netaneli, Mlevi, analemba mayina awo pamaso pa mfumu ndi akuluakulu ake: wansembe Zadoki, Ahimeleki mwana wa Abiatara ndi atsogoleri a mabanja a ansembe ndiponso Alevi, banja limodzi kuchokera kwa Eliezara kenaka limodzi kuchokera kwa Itamara.

Maere woyamba anagwera Yehoyaribu,

achiwiri anagwera Yedaya,

achitatu anagwera Harimu,

achinayi anagwera Seorimu,

achisanu anagwera Malikiya,

achisanu ndi chimodzi anagwera Miyamini,

10 achisanu ndi chiwiri anagwera Hakozi,

achisanu ndi chitatu anagwera Abiya,

11 achisanu ndi chinayi anagwera Yesuwa,

a khumi anagwera Sekaniya,

12 a 11 anagwera Eliyasibu,

a 12 anagwera Yakimu,

13 a 13 anagwera Hupa,

a 14 anagwera Yesebeabu,

14 a 15 anagwera Biliga,

a 16 anagwera Imeri,

15 a 17 anagwera Heziri,

a 18 anagwera Hapizezi,

16 a 19 anagwera Petahiya,

a 20 anagwera Ezekieli,

17 a 21 anagwera Yakini,

a 22 anagwera Gamuli,

18 a 23 anagwera Delaya,

ndipo a 24 anagwera Maaziya.

19 Umu ndi mmene anasankhidwira kuti azigwira ntchito yotumikira pamene alowa mʼNyumba ya Yehova, motsatira dongosolo limene anapatsidwa ndi kholo lawo Aaroni, monga momwe Yehova Mulungu wa Israeli anamulamulira.

Alevi Ena Onse

20 Za zidzukulu zina zonse za Levi:

Kuchokera kwa ana a Amramu: Subaeli;

kuchokera kwa ana a Subaeli: Yehideya.

21 Kwa Rehabiya, kuchokera kwa ana ake:

Mtsogoleri anali Isiya.

22 Kuchokera ku banja la Izihari: Selomoti;

kuchokera kwa ana a Selomoti: Yahati.

23 Ana a Hebroni: woyamba anali Yeriya, wachiwiri anali Amariya, wachitatu anali Yahazieli ndipo Yekameamu anali wachinayi.

24 Mwana wa Uzieli: Mika;

kuchokera kwa ana a Mika: Samiri.

25 Mʼbale wa Mika: Isiya;

kuchokera kwa ana a Isiya: Zekariya.

26 Ana a Merari: Mahili ndi Musi.

Mwana wa Yaaziya: Beno.

27 Ana a Merari:

Kuchokera kwa Yaaziya: Beno, Sohamu, Zakuri ndi Ibiri.

28 Kuchokera kwa Mahili: Eliezara, amene analibe ana aamuna.

29 Kuchokera kwa Kisi:

Mwana wa Kisi: Yerahimeeli.

30 Ndipo ana a Musi: Mahili, Ederi ndi Yerimoti.

Awa anali Alevi potsata mabanja a makolo awo. 31 Iwonso anachita maere, monga anachitira abale awo, zidzukulu za Aaroni, pamaso pa mfumu Davide, ndi Zadoki ndi Ahimeleki, atsogoleri a mabanja a ansembe ndi Alevi. Mabanja a mwana wamkulu anachita nawo mofanana ndi a mwana wamngʼono.

The Divisions of Priests

24 These were the divisions(A) of the descendants of Aaron:(B)

The sons of Aaron were Nadab, Abihu, Eleazar and Ithamar.(C) But Nadab and Abihu died before their father did,(D) and they had no sons; so Eleazar and Ithamar served as the priests. With the help of Zadok(E) a descendant of Eleazar and Ahimelek a descendant of Ithamar, David separated them into divisions for their appointed order of ministering. A larger number of leaders were found among Eleazar’s descendants than among Ithamar’s, and they were divided accordingly: sixteen heads of families from Eleazar’s descendants and eight heads of families from Ithamar’s descendants. They divided them impartially by casting lots,(F) for there were officials of the sanctuary and officials of God among the descendants of both Eleazar and Ithamar.

The scribe Shemaiah son of Nethanel, a Levite, recorded their names in the presence of the king and of the officials: Zadok the priest, Ahimelek(G) son of Abiathar and the heads of families of the priests and of the Levites—one family being taken from Eleazar and then one from Ithamar.

The first lot fell to Jehoiarib,

the second to Jedaiah,(H)

the third to Harim,(I)

the fourth to Seorim,

the fifth to Malkijah,

the sixth to Mijamin,

10 the seventh to Hakkoz,

the eighth to Abijah,(J)

11 the ninth to Jeshua,

the tenth to Shekaniah,

12 the eleventh to Eliashib,

the twelfth to Jakim,

13 the thirteenth to Huppah,

the fourteenth to Jeshebeab,

14 the fifteenth to Bilgah,

the sixteenth to Immer,(K)

15 the seventeenth to Hezir,(L)

the eighteenth to Happizzez,

16 the nineteenth to Pethahiah,

the twentieth to Jehezkel,

17 the twenty-first to Jakin,

the twenty-second to Gamul,

18 the twenty-third to Delaiah

and the twenty-fourth to Maaziah.

19 This was their appointed order of ministering when they entered the temple of the Lord, according to the regulations prescribed for them by their ancestor Aaron, as the Lord, the God of Israel, had commanded him.

The Rest of the Levites

20 As for the rest of the descendants of Levi:(M)

from the sons of Amram: Shubael;

from the sons of Shubael: Jehdeiah.

21 As for Rehabiah,(N) from his sons:

Ishiah was the first.

22 From the Izharites: Shelomoth;

from the sons of Shelomoth: Jahath.

23 The sons of Hebron:(O) Jeriah the first,[a] Amariah the second, Jahaziel the third and Jekameam the fourth.

24 The son of Uzziel: Micah;

from the sons of Micah: Shamir.

25 The brother of Micah: Ishiah;

from the sons of Ishiah: Zechariah.

26 The sons of Merari:(P) Mahli and Mushi.

The son of Jaaziah: Beno.

27 The sons of Merari:

from Jaaziah: Beno, Shoham, Zakkur and Ibri.

28 From Mahli: Eleazar, who had no sons.

29 From Kish: the son of Kish:

Jerahmeel.

30 And the sons of Mushi: Mahli, Eder and Jerimoth.

These were the Levites, according to their families. 31 They also cast lots,(Q) just as their relatives the descendants of Aaron did, in the presence of King David and of Zadok, Ahimelek, and the heads of families of the priests and of the Levites. The families of the oldest brother were treated the same as those of the youngest.

Footnotes

  1. 1 Chronicles 24:23 Two Hebrew manuscripts and some Septuagint manuscripts (see also 23:19); most Hebrew manuscripts The sons of Jeriah: