Add parallel Print Page Options

Davide Amusiya Sauli Wosamupha

24 Sauli atabwera kuchokera kumene amathamangitsa Afilisti anamva kuti, “Davide ali mʼchipululu cha Eni Gedi.” Tsono Sauli anatenga asilikali 3,000 odziwa kumenya bwino nkhondo kuchokera pakati pa Aisraeli onse ndipo anapita kukafunafuna Davide ndi anthu ake ku Matanthwe a Mbalale.

Iye anafika ku makola a nkhosa amene anali mʼmbali mwa njira. Kumeneko kunali phanga, ndipo Sauli analowa mʼphangamo kuti akadzithandize. Davide ndi anthu ake ankabisala mʼkati mwenimweni mwa phangalo. Tsono anthu a Davide anamuwuza kuti, “Tsiku lija lafika limene Yehova anakuwuzani kuti, ‘Ndidzapereka mdani wanu mʼmanja mwanu, ndi kumuchita chimene chidzakukomereni.’ ” Koma Davide anapita mwakachetechete ndi kukadula msonga ya mkanjo wa Sauli.

Atachita izi, Davide anatsutsika mu mtima chifukwa anadula msonga ya mkanjo wa Sauli. Tsono anawuza anthu ake kuti, “Yehova asalole kuti ndimuchite choyipa mbuye wanga, wodzozedwa wa Yehova. Ndisamupweteke pakuti ndi wodzozedwa wa Yehova.” Choncho Davide anabweza mitima ya anthu ake ndi mawu amenewa, ndipo sanawalole kuti aphe Sauli. Pambuyo pake Sauli anatuluka mʼphangamo ndipo anachoka.

Kenaka Davide anatuluka mʼphanga muja ndipo anayitana Sauli, “Mbuye wanga!” Sauli atayangʼana mʼmbuyo, Davide anawerama ndi kugunditsa nkhope yake pansi. Anafunsa Sauli kuti, “Nʼchifukwa chiyani mumamvera mawu a anthu kuti, ‘Davide wakukonzerani chiwembu?’ 10 Lero lino inu mwadzionera nokha kuti Yehova anakuperekani mʼmanja mwanga mʼphanga muja. Ena anandiwuza kuti ndikupheni, koma ndakusiyani. Ndinati, ‘Sindidzapha mbuye wanga pakuti ndiye wodzozedwa wa Yehova.’ 11 Tsono abambo anga, onanitu kansalu ka mkanjo wanu kali mʼdzanja langali! Popeza kuti ndinatha kudula msonga ya mkanjo wanu koma osakuphani, pamenepo mudziwe kuti ine ndilibe maganizo woti ndikuchiteni choyipa kapena kukuwukirani. Sindinakulakwireni ngakhale kuti inu mukufuna moyo wanga kuti mundiphe. 12 Yehova aweruze pakati pa inu ndi ine, akulangeni chifukwa cha zoyipa zimene mukundichitazi, koma dzanja langa silidzakukhudzani. 13 Paja anthu akale anati, ‘Munthu woyipa, ntchito zakenso ndi zoyipa.’ Kotero dzanja langa silidzakukhudzani.

14 “Kodi mfumu ya Israeli yadzalondola yani. Inu mukuthamangitsa yani? Galu wakufa kodi? Nsabwe kodi? 15 Nʼchifukwa chake Yehova agamule, inde aweruze pakati pa inu ndi ine ndi kupeza wolakwa. Yehova anditeteze ndi kundipulumutsa mʼdzanja lanu.”

16 Davide atatsiriza kuyankhula mawu awa, Sauli anafunsa kuti, “Kodi mawu amenewa ndi akodi mwana wanga Davide?” Sauli anayamba kulira mokweza. 17 Anawuza Davide kuti, “Ndiwe wolungama kuposa ine. Iwe wandikomera mtima pamene ine ndakuchitira zoyipa. 18 Iweyo lero lino wandifotokozera zabwino zimene wandichitira. Yehova anandipereka mʼdzanja lako koma iwe sunandiphe. 19 Kodi munthu atapeza mdani wake angamulole kuti apite wosamuvulaza? Motero Yehova akuchitire iwe zabwino chifukwa cha zimene wandichitira lerozi. 20 Ona tsono, Ine ndikudziwa kuti udzakhala mfumu ndithu ndipo ufumu wa Israeli udzakhazikika mʼmanja mwako. 21 Tsopano undilonjeze molumbira lero mʼdzina la Yehova kuti sudzapha zidzukulu zanga ine nditamwalira kapena kufuta dzina langa pa banja la makolo anga.”

22 Choncho Davide analumbira pamaso pa Sauli. Pambuyo pake Sauli anabwerera kwawo, koma Davide ndi anthu ake anapitanso ku phanga kuja.

David Spares Saul’s Life

24 [a]After Saul returned from pursuing the Philistines, he was told, “David is in the Desert of En Gedi.(A) So Saul took three thousand able young men from all Israel and set out to look(B) for David and his men near the Crags of the Wild Goats.

He came to the sheep pens along the way; a cave(C) was there, and Saul went in to relieve(D) himself. David and his men were far back in the cave. The men said, “This is the day the Lord spoke(E) of when he said[b] to you, ‘I will give your enemy into your hands for you to deal with as you wish.’”(F) Then David crept up unnoticed and cut(G) off a corner of Saul’s robe.

Afterward, David was conscience-stricken(H) for having cut off a corner of his robe. He said to his men, “The Lord forbid that I should do such a thing to my master, the Lord’s anointed,(I) or lay my hand on him; for he is the anointed of the Lord.” With these words David sharply rebuked his men and did not allow them to attack Saul. And Saul left the cave and went his way.

Then David went out of the cave and called out to Saul, “My lord the king!” When Saul looked behind him, David bowed down and prostrated himself with his face to the ground.(J) He said to Saul, “Why do you listen(K) when men say, ‘David is bent on harming(L) you’? 10 This day you have seen with your own eyes how the Lord delivered you into my hands in the cave. Some urged me to kill you, but I spared(M) you; I said, ‘I will not lay my hand on my lord, because he is the Lord’s anointed.’ 11 See, my father, look at this piece of your robe in my hand! I cut(N) off the corner of your robe but did not kill you. See that there is nothing in my hand to indicate that I am guilty(O) of wrongdoing(P) or rebellion. I have not wronged(Q) you, but you are hunting(R) me down to take my life.(S) 12 May the Lord judge(T) between you and me. And may the Lord avenge(U) the wrongs you have done to me, but my hand will not touch you. 13 As the old saying goes, ‘From evildoers come evil deeds,(V)’ so my hand will not touch you.

14 “Against whom has the king of Israel come out? Who are you pursuing? A dead dog?(W) A flea?(X) 15 May the Lord be our judge(Y) and decide(Z) between us. May he consider my cause and uphold(AA) it; may he vindicate(AB) me by delivering(AC) me from your hand.”

16 When David finished saying this, Saul asked, “Is that your voice,(AD) David my son?” And he wept aloud. 17 “You are more righteous than I,”(AE) he said. “You have treated me well,(AF) but I have treated you badly.(AG) 18 You have just now told me about the good you did to me; the Lord delivered(AH) me into your hands, but you did not kill me. 19 When a man finds his enemy, does he let him get away unharmed? May the Lord reward(AI) you well for the way you treated me today. 20 I know that you will surely be king(AJ) and that the kingdom(AK) of Israel will be established in your hands. 21 Now swear(AL) to me by the Lord that you will not kill off my descendants or wipe out my name from my father’s family.(AM)

22 So David gave his oath to Saul. Then Saul returned home, but David and his men went up to the stronghold.(AN)

Footnotes

  1. 1 Samuel 24:1 In Hebrew texts 24:1-22 is numbered 24:2-23.
  2. 1 Samuel 24:4 Or “Today the Lord is saying