Add parallel Print Page Options

Paulo Mlaliki wa Anthu a Mitundu Ina

Nʼchifukwa chake ine Paulo, ndili wamʼndende wa Khristu Yesu chifukwa cha inu anthu a mitundu ina.

Ndithudi, inu munamva za ntchito yachisomo cha Mulungu imene anandipatsa chifukwa cha inu, ndicho chinsinsi chimene chinawululidwa kwa ine mwa vumbulutso, monga ndinakulemberani kale mwachidule. Pamene mukuwerenga izi, inu mudzazindikira za chidziwitso changa pa chinsinsi cha Khristu, chimene sichinawululidwe kwa anthu amibado ina monga momwe tsopano chawululidwa ndi Mzimu wa Mulungu mwa atumwi oyera ndi aneneri. Chinsinsicho nʼchakuti, kudzera mu Uthenga Wabwino anthu a mitundu ina ndi olowamʼmalo pamodzi ndi Aisraeli, ndi ziwalo za thupi limodzi, ndi olandira nawo pamodzi malonjezo a mwa Khristu Yesu.

Mwachisomo cha Mulungu ndi mphamvu zake, ine ndinasanduka mtumiki wa Uthenga Wabwinowu. Ngakhale ndili wamngʼono kwambiri pakati pa anthu onse a Mulungu, anandipatsa chisomo chimenechi cholalikira kwa anthu a mitundu ina chuma chopanda malire cha Khristu. Ndinasankhidwa kuti ndifotokoze momveka bwino kwa munthu aliyense za chinsinsi chimenechi, chinsinsi chimene kuyambira kale chinali chobisika mwa Mulungu amene analenga zinthu zonse. 10 Cholinga chake tsopano nʼchakuti, kudzera mwa mpingo, mafumu ndi a ulamuliro onse a kumwamba adziwe nzeru zochuluka za Mulungu. 11 Chimenechi chinali chikonzero chamuyaya cha Mulungu, chimene chinachitika kudzera mwa Khristu Yesu Ambuye athu. 12 Mwa Khristu ndi mwa chikhulupiriro chathu mwa Iye, timayandikira kwa Mulungu momasuka ndi molimbika mtima. 13 Choncho, ine ndikukupemphani kuti musakhumudwe popeza ndikusautsidwa chifukwa cha inu pakuti masautso angawa ndi ulemerero wanu.

Paulo Apempherera Aefeso

14 Nʼchifukwa chake ine ndikugwada pamaso pa Atate, 15 amene banja lililonse kumwamba ndi pa dziko lapansi limatchulidwa ndi dzina lawo. 16 Ndikupemphera kuti kuchokera mʼchuma cha ulemerero wake alimbikitse moyo wanu wa mʼkati ndi mphamvu za Mzimu wake, 17 kuti Khristu akhazikike mʼmitima mwanu mwachikhulupiriro. Ndipo ndikukupemphererani kuti muzikike ndi kukhazikika mʼchikondi 18 kuti mukhale ndi mphamvu, kuti pamodzi ndi anthu oyera mtima onse muthe kuzindikira kupingasa, kutalika ndi kukwera komanso kuzama kwake kwa chikondi cha Khristu. 19 Ndikukupemphererani kuti mudziwe chikondi chija cha Khristu chopitirira nzeru za anthu, kuti mudzazidwe kwathunthu ndi moyo wa Mulungu mwini.

20 Tsopano kwa Iye amene angathe kuchita zochuluka kuposa zimene tingapemphe, kapena kuganiza molingana ndi mphamvu zake zimene zikugwira ntchito mwa ife, 21 Iyeyo akhale ndi ulemu mu mpingo ndi mwa Khristu Yesu pa mibado yonse mpaka muyaya. Ameni.

God’s Marvelous Plan for the Gentiles

For this reason I, Paul, the prisoner(A) of Christ Jesus for the sake of you Gentiles—

Surely you have heard about the administration of God’s grace that was given to me(B) for you, that is, the mystery(C) made known to me by revelation,(D) as I have already written briefly. In reading this, then, you will be able to understand my insight(E) into the mystery of Christ, which was not made known to people in other generations as it has now been revealed by the Spirit to God’s holy apostles and prophets.(F) This mystery is that through the gospel the Gentiles are heirs(G) together with Israel, members together of one body,(H) and sharers together in the promise in Christ Jesus.(I)

I became a servant of this gospel(J) by the gift of God’s grace given me(K) through the working of his power.(L) Although I am less than the least of all the Lord’s people,(M) this grace was given me: to preach to the Gentiles(N) the boundless riches of Christ,(O) and to make plain to everyone the administration of this mystery,(P) which for ages past was kept hidden in God, who created all things. 10 His intent was that now, through the church, the manifold wisdom of God(Q) should be made known(R) to the rulers and authorities(S) in the heavenly realms,(T) 11 according to his eternal purpose(U) that he accomplished in Christ Jesus our Lord. 12 In him and through faith in him we may approach God(V) with freedom and confidence.(W) 13 I ask you, therefore, not to be discouraged because of my sufferings for you, which are your glory.

A Prayer for the Ephesians

14 For this reason I kneel(X) before the Father, 15 from whom every family[a] in heaven and on earth derives its name. 16 I pray that out of his glorious riches(Y) he may strengthen you with power(Z) through his Spirit in your inner being,(AA) 17 so that Christ may dwell in your hearts(AB) through faith. And I pray that you, being rooted(AC) and established in love, 18 may have power, together with all the Lord’s holy people,(AD) to grasp how wide and long and high and deep(AE) is the love of Christ, 19 and to know this love that surpasses knowledge(AF)—that you may be filled(AG) to the measure of all the fullness of God.(AH)

20 Now to him who is able(AI) to do immeasurably more than all we ask(AJ) or imagine, according to his power(AK) that is at work within us, 21 to him be glory in the church and in Christ Jesus throughout all generations, for ever and ever! Amen.(AL)

Footnotes

  1. Ephesians 3:15 The Greek for family (patria) is derived from the Greek for father (pater).