Add parallel Print Page Options

Tsono abale anga, ndimakukondani ndipo ndikukulakalakani. Ndinu chimwemwe changa ndi chipewa cha ulemerero wanga. Abwenzi okondedwa, chilimikani choncho mwa Ambuye.

Ndikudandaulira Euodiya ndi Suntuke kuti akhale ndi mtima umodzi mwa Ambuye. Inde, ndikupempha iwe mnzanga pa ntchitoyi, thandiza amayiwa amene ndagwira nawo ntchito ya Uthenga Wabwino pamodzi ndi Klementonso ndi ena onse antchito anzanga amene mayina awo ali mʼbuku lamoyo.

Malangizo Otsiriza

Nthawi zonse muzikondwa mwa Ambuye. Ndikubwerezanso; muzikondwa! Kufatsa kwanu kuzioneka pamaso pa anthu onse. Ambuye anu ali pafupi. Musade nkhawa ndi kanthu kalikonse, koma pa china chilichonse, mwa pemphero ndi chidandaulo pamodzi ndi chiyamiko, perekani zopempha zanu kwa Mulungu. Ndipo mtendere wa Mulungu, umene upambana nzeru zonse udzasunga bwino mitima yanu ndi maganizo anu mwa Khristu Yesu.

Potsiriza, abale, muziyika mtima wanu pa zinthu zilizonse zabwino ndi zotamandika monga, zinthu zoona, zinthu zolemekezeka, zinthu zolungama, zinthu zoyera, zinthu zokongola ndi zinthu zosiririka. Muzichita chilichonse chimene mwaphunzira kapena kulandira kapena kumva kuchokera kwa ine kapena mwaona mwa ine. Ndipo Mulungu wamtendere adzakhala nanu.

Kuthokoza Chifukwa cha Mphatso

10 Ndikukondwa kwambiri mwa Ambuye kuti patapita nthawi tsopano mwayambanso kuonetsa kuti mumandiganizira. Zoonadi, mwakhala mukundikumbukira, koma munalibe mpata woti muonetsere zimenezi. 11 Sindikunena izi chifukwa choti ndikusowa thandizo, poti ine ndaphunzira kukhala wokwaniritsidwa ndi zimene ndili nazo. 12 Ndimadziwa kusauka nʼkutani, ndipo ndimadziwa kulemera nʼkutani. Ndaphunzira chinsinsi chokhala wokhutitsidwa mwa njira ina iliyonse, kaya nʼkudya bwino kapena kukhala ndi njala, kaya kukhala ndi chuma kapena umphawi. 13 Ndikhoza kuchita zonse kudzera mwa Iye amene amandipatsa mphamvu.

14 Komatu munachita bwino kundithandiza mʼmavuto anga. 15 Ndipo inu Afilipi mukudziwa kuti masiku oyambirira olalikira Uthenga Wabwino, nditachoka ku Makedoniya, panalibe mpingo ndi umodzi omwe umene unagwirizana nane pa nkhani yopereka ndi kulandira, kupatula inu. 16 Pakuti ngakhale pamene ndinali ku Tesalonika, munanditumizira kangapo zondithandiza pa zosowa zanga. 17 Osati ndikufuna mphatso zanu, koma ndikufuna kuti pa zimene muli nazo pawonjezerekepo phindu. 18 Ndalandira zonse ndipo ndili nazo zokwanira zoposa zosowa zanga popeza ndalandira kwa Epafrodito mphatso zochuluka zimene munatumiza. Ndizo zopereka za fungo labwino, nsembe zolandiridwa zokondweretsa Mulungu. 19 Ndipo Mulungu wanga adzakwaniritsa zosowa zanu monga mwa chuma chake chaulemerero mwa Khristu Yesu.

20 Kwa Mulungu ndi Atate athu, kukhale ulemerero mpaka muyaya. Ameni.

Malonje Otsiriza

21 Perekani moni kwa oyera mtima onse mwa Khristu Yesu. Abale amene ali ndi ine akupereka moni wawo. 22 Oyera mtima onse akupereka moni, makamaka iwo a ku nyumba ya Kaisara.

23 Chisomo cha Ambuye Yesu Khristu chikhale ndi mzimu wanu. Ameni.

Closing Appeal for Steadfastness and Unity

Therefore, my brothers and sisters, you whom I love and long for,(A) my joy and crown, stand firm(B) in the Lord in this way, dear friends!

I plead with Euodia and I plead with Syntyche to be of the same mind(C) in the Lord. Yes, and I ask you, my true companion, help these women since they have contended at my side in the cause of the gospel, along with Clement and the rest of my co-workers,(D) whose names are in the book of life.(E)

Final Exhortations

Rejoice in the Lord always. I will say it again: Rejoice!(F) Let your gentleness be evident to all. The Lord is near.(G) Do not be anxious about anything,(H) but in every situation, by prayer and petition, with thanksgiving, present your requests to God.(I) And the peace of God,(J) which transcends all understanding,(K) will guard your hearts and your minds in Christ Jesus.

Finally, brothers and sisters, whatever is true, whatever is noble, whatever is right, whatever is pure, whatever is lovely, whatever is admirable—if anything is excellent or praiseworthy—think about such things. Whatever you have learned or received or heard from me, or seen in me—put it into practice.(L) And the God of peace(M) will be with you.

Thanks for Their Gifts

10 I rejoiced greatly in the Lord that at last you renewed your concern for me.(N) Indeed, you were concerned, but you had no opportunity to show it. 11 I am not saying this because I am in need, for I have learned to be content(O) whatever the circumstances. 12 I know what it is to be in need, and I know what it is to have plenty. I have learned the secret of being content in any and every situation, whether well fed or hungry,(P) whether living in plenty or in want.(Q) 13 I can do all this through him who gives me strength.(R)

14 Yet it was good of you to share(S) in my troubles. 15 Moreover, as you Philippians know, in the early days(T) of your acquaintance with the gospel, when I set out from Macedonia,(U) not one church shared with me in the matter of giving and receiving, except you only;(V) 16 for even when I was in Thessalonica,(W) you sent me aid more than once when I was in need.(X) 17 Not that I desire your gifts; what I desire is that more be credited to your account.(Y) 18 I have received full payment and have more than enough. I am amply supplied, now that I have received from Epaphroditus(Z) the gifts you sent. They are a fragrant(AA) offering, an acceptable sacrifice, pleasing to God. 19 And my God will meet all your needs(AB) according to the riches of his glory(AC) in Christ Jesus.

20 To our God and Father(AD) be glory for ever and ever. Amen.(AE)

Final Greetings

21 Greet all God’s people in Christ Jesus. The brothers and sisters who are with me(AF) send greetings. 22 All God’s people(AG) here send you greetings, especially those who belong to Caesar’s household.

23 The grace of the Lord Jesus Christ(AH) be with your spirit.(AI) Amen.[a]

Footnotes

  1. Philippians 4:23 Some manuscripts do not have Amen.