Add parallel Print Page Options

Mawu Achilimbikitso Otsiriza

13 Pitirizani kukondana monga abale. Musayiwale kusamalira alendo, pakuti pochita zimenezi anthu ena anasamalira angelo amene samawadziwa. Muzikumbukira amene ali mʼndende ngati kuti inunso ndi omangidwa, ndiponso amene akusautsidwa ngati inunso mukuvutika.

Ukwati muziwulemekeza nonse, ndipo mwamuna ndi mkazi azikhala wokhulupirika, pakuti anthu adama ndi achigololo Mulungu adzawalanga. Mtima wanu usakonde ndalama koma mukhutitsidwe ndi zimene muli nazo, chifukwa Mulungu anati,

“Sadzakusiyani,
    kapena kukutayani konse.”

Kotero ife tikunena molimba mtima kuti,

“Ambuye ndiye mthandizi wanga;
    sindidzachita mantha. Munthu angandichitenji ine?”

Muzikumbukira atsogoleri anu, amene amakulalikirani Mawu a Mulungu. Ganizirani zamoyo wawo ndipo tsatirani chikhulupiriro chawo. Yesu Khristu ndi yemweyo dzulo, lero ndi kunthawi zonse.

Musasocheretsedwe ndi ziphunzitso zosiyanasiyana zachilendo. Nʼkwabwino kuti mitima yathu ilimbikitsidwe ndi chisomo osati ndi chakudya, chimene sichipindulitsa iwo amene amachidya. 10 Ife tili ndi guwa lansembe, ndipo ansembe otumikira mʼtenti cha Ayuda, saloledwa kudya zochokera pamenepo.

11 Mkulu wa ansembe amatenga magazi kukapereka nsembe chifukwa cha machimo, koma nyamayo imawotchedwa kunja kwa msasa. 12 Nʼchifukwa chakenso Yesu anafera kunja kwa mzinda kuti ayeretse anthu ake kudzera mʼmagazi ake. 13 Tiyeni tsono, tipite kwa iye kunja kwa msasa, titasenza chitonzo chake. 14 Pakuti ife tilibe mzinda wokhazikika koma tikudikira mzinda umene ukubwera.

15 Tsono, tiyeni kudzera mwa Yesu tipereke nsembe zachiyamiko kwa Mulungu osalekeza, chipatso cha milomo imene imavomereza dzina lake. 16 Ndipo musayiwale kumachita zabwino ndi kuthandiza ena, pakuti Mulungu amakondwera ndi nsembe zotere. 17 Muzimvera atsogoleri anu ndi kugonjera ulamuliro wawo, iwo amakuyangʼanirani monga anthu amene adzayenera kufotokoza za ntchito yawo pamaso pa Mulungu. Muziwamvera kuti agwire ntchito yawo ndi chimwemwe osati molemedwa pakuti izi sizingakupindulireni.

18 Mutipempherere ifenso. Pakuti tikutsimikiza kuti tili ndi chikumbumtima changwiro ndipo timafuna kuchita zinthu zonse mwaulemu. 19 Ine ndikukupemphani kuti mundipempherere kuti Mulungu andibwezere kwa inu msanga.

20 Mulungu wamtendere, amene kudzera mʼmagazi a pangano lamuyaya anaukitsa Ambuye athu Yesu kwa akufa, amene ndi Mʼbusa wamkulu, 21 akupatseni chilichonse chabwino kuti muchite chifuniro chake ndipo Mulungu achite mwa ife, chimene chingamukomere kudzera mwa Yesu Khristu. Kwa Iye kukhale ulemerero ku nthawi zanthawi, Ameni.

22 Ndikukupemphani abale kuti mulandire mawu anga achilimbikitso, pakuti ndakulemberani mwachidule.

23 Ine ndikufuna kuti inu mudziwe kuti mʼbale wathu Timoteyo wamasulidwa. Ngati iye angafike msanga ndibwera naye kudzakuonani.

24 Mupereke moni kwa atsogoleri anu onse ndiponso kwa anthu onse a Mulungu. Abale ochokera ku Italiya akupereka moni.

25 Chisomo chikhale ndi inu nonse.

Concluding Exhortations

13 Keep on loving one another as brothers and sisters.(A) Do not forget to show hospitality to strangers,(B) for by so doing some people have shown hospitality to angels without knowing it.(C) Continue to remember those in prison(D) as if you were together with them in prison, and those who are mistreated as if you yourselves were suffering.

Marriage should be honored by all,(E) and the marriage bed kept pure, for God will judge the adulterer and all the sexually immoral.(F) Keep your lives free from the love of money(G) and be content with what you have,(H) because God has said,

“Never will I leave you;
    never will I forsake you.”[a](I)

So we say with confidence,

“The Lord is my helper; I will not be afraid.
    What can mere mortals do to me?”[b](J)

Remember your leaders,(K) who spoke the word of God(L) to you. Consider the outcome of their way of life and imitate(M) their faith. Jesus Christ is the same yesterday and today and forever.(N)

Do not be carried away by all kinds of strange teachings.(O) It is good for our hearts to be strengthened(P) by grace, not by eating ceremonial foods,(Q) which is of no benefit to those who do so.(R) 10 We have an altar from which those who minister at the tabernacle(S) have no right to eat.(T)

11 The high priest carries the blood of animals into the Most Holy Place as a sin offering,(U) but the bodies are burned outside the camp.(V) 12 And so Jesus also suffered outside the city gate(W) to make the people holy(X) through his own blood.(Y) 13 Let us, then, go to him(Z) outside the camp, bearing the disgrace he bore.(AA) 14 For here we do not have an enduring city,(AB) but we are looking for the city that is to come.(AC)

15 Through Jesus, therefore, let us continually offer to God a sacrifice(AD) of praise—the fruit of lips(AE) that openly profess his name. 16 And do not forget to do good and to share with others,(AF) for with such sacrifices(AG) God is pleased.

17 Have confidence in your leaders(AH) and submit to their authority, because they keep watch over you(AI) as those who must give an account. Do this so that their work will be a joy, not a burden, for that would be of no benefit to you.

18 Pray for us.(AJ) We are sure that we have a clear conscience(AK) and desire to live honorably in every way. 19 I particularly urge you to pray so that I may be restored to you soon.(AL)

Benediction and Final Greetings

20 Now may the God of peace,(AM) who through the blood of the eternal covenant(AN) brought back from the dead(AO) our Lord Jesus, that great Shepherd of the sheep,(AP) 21 equip you with everything good for doing his will,(AQ) and may he work in us(AR) what is pleasing to him,(AS) through Jesus Christ, to whom be glory for ever and ever. Amen.(AT)

22 Brothers and sisters, I urge you to bear with my word of exhortation, for in fact I have written to you quite briefly.(AU)

23 I want you to know that our brother Timothy(AV) has been released. If he arrives soon, I will come with him to see you.

24 Greet all your leaders(AW) and all the Lord’s people. Those from Italy(AX) send you their greetings.

25 Grace be with you all.(AY)

Footnotes

  1. Hebrews 13:5 Deut. 31:6
  2. Hebrews 13:6 Psalm 118:6,7