Add parallel Print Page Options

Dzombe, Moto ndi Chingwe Chowongolera Khoma

Zimene Ambuye Yehova anandionetsa ndi izi: Yehova ankasonkhanitsa gulu la dzombe nthawi imene gawo la zokolola za mfumu linali litakololedwa kale ndipo mbewu zachiwiri zinali zitangoyamba kumera kumene. Dzombelo litadya zomera zonse za mʼdzikomo, Ine ndinafuwula kuti, “Ambuye Yehova, khululukani! Kodi Yakobo adzapulumuka bwanji? Iye ndi wofowoka kwambiri!”

Kotero Yehova anakhululuka.

Yehovayo anati, “Izi sizidzachitika.”

Zimene Ambuye Yehova anandionetsa ndi izi: Ambuye Yehova ankayitana malawi a moto kuti alange anthu. Motowo unawumitsa nyanja yakuya ndi kupsereza dziko. Tsono ine ndinafuwula kuti, “Ambuye Yehova, chonde ndikukupemphani, lekani! Kodi Yakobo adzapulumuka bwanji? Iye ndi wofowoka kwambiri!”

Kotero Yehova anakhululuka.

Ambuye Yehova anati, “Izinso sizidzachitika.”

Zimene Iye anandionetsa ndi izi: Ambuye anayima pambali pa khoma lomangamanga, mʼmanja mwake muli chingwe chowongolera khoma. Ndipo Ambuye anandifunsa kuti, “Amosi, nʼchiyani ukuonachi?”

Ine ndinayankha kuti, “Chingwe chowongolera khoma.”

Ndipo Yehova anati, “Taona, Ine ndikuyika chingwe chowongolerachi pakati pa anthu anga, Aisraeli; sindidzawalekereranso.

“Malo achipembedzo a Isake adzawonongedwa
    ndipo malo opatulika a Israeli adzasanduka bwinja;
    ndidzagwetsa nyumba ya Yeroboamu ndi lupanga langa.”

Amosi ndi Amaziya

10 Pamenepo Amaziya wansembe wa ku Beteli anatumiza uthenga kwa Yeroboamu mfumu ya Israeli kuti, “Amosi akukuutsirani chiwembu pakati pa Aisraeli. Dziko silingalekerere zonena zake zonsezo. 11 Pakuti zimene Amosi akunena ndi izi:

“ ‘Yeroboamu adzaphedwa ndi lupanga,
    ndipo Israeli adzapita ndithu ku ukapolo,
    kutali ndi dziko lake.’ ”

12 Ndipo Amaziya anawuza Amosi kuti, “Choka, mlosi iwe! Bwerera ku dziko la Yuda. Uzikalosera kumeneko ndipo anthu a kumeneko azikakudyetsa. 13 Usanenerenso ku Beteli, chifukwa kumeneko ndi malo opatulika a mfumu ndiponso ndi malo a nyumba yachipembedzo yaufumu.”

14 Amosi anayankha Amaziya kuti, “Ine sindine mneneri kapena mwana wa mneneri; koma ndine woweta ziweto, ndiponso mlimi wa nkhuyu. 15 Koma Yehova ananditenga ndikuweta nkhosa ndipo anati, ‘Pita ukanenere kwa anthu anga Aisraeli.’ 16 Tsono imva mawu a Yehova. Iwe ukunena kuti,

“ ‘Usanenere zotsutsa Israeli,
    ndipo siya kulalikira motsutsa nyumba ya Isake.’ ”

17 “Tsono zimene akunena Yehova ndi izi:

“ ‘Mkazi wako adzasanduka wachiwerewere mu mzindamu,
    ndipo ana ako aamuna ndi aakazi adzaphedwa ndi lupanga.
Munda wako udzayezedwa ndi chingwe ndi kugawidwa,
    ndipo iwe mwini udzafera mʼdziko la anthu osapembedza Mulungu.
Ndipo Israeli adzatengedwa ndithu kupita ku ukapolo,
    kutali ndi dziko lake.’ ”

Locusts, Fire and a Plumb Line

This is what the Sovereign Lord showed me:(A) He was preparing swarms of locusts(B) after the king’s share had been harvested and just as the late crops were coming up. When they had stripped the land clean,(C) I cried out, “Sovereign Lord, forgive! How can Jacob survive?(D) He is so small!(E)

So the Lord relented.(F)

“This will not happen,” the Lord said.(G)

This is what the Sovereign Lord showed me: The Sovereign Lord was calling for judgment by fire;(H) it dried up the great deep and devoured(I) the land. Then I cried out, “Sovereign Lord, I beg you, stop! How can Jacob survive? He is so small!(J)

So the Lord relented.(K)

“This will not happen either,” the Sovereign Lord said.(L)

This is what he showed me: The Lord was standing by a wall that had been built true to plumb,[a] with a plumb line[b] in his hand. And the Lord asked me, “What do you see,(M) Amos?(N)

“A plumb line,(O)” I replied.

Then the Lord said, “Look, I am setting a plumb line among my people Israel; I will spare them no longer.(P)

“The high places(Q) of Isaac will be destroyed
    and the sanctuaries(R) of Israel will be ruined;
    with my sword I will rise against the house of Jeroboam.(S)

Amos and Amaziah

10 Then Amaziah the priest of Bethel(T) sent a message to Jeroboam(U) king of Israel: “Amos is raising a conspiracy(V) against you in the very heart of Israel. The land cannot bear all his words.(W) 11 For this is what Amos is saying:

“‘Jeroboam will die by the sword,
    and Israel will surely go into exile,(X)
    away from their native land.’”(Y)

12 Then Amaziah said to Amos, “Get out, you seer!(Z) Go back to the land of Judah. Earn your bread there and do your prophesying there.(AA) 13 Don’t prophesy anymore at Bethel,(AB) because this is the king’s sanctuary and the temple(AC) of the kingdom.(AD)

14 Amos answered Amaziah, “I was neither a prophet(AE) nor the son of a prophet, but I was a shepherd, and I also took care of sycamore-fig trees.(AF) 15 But the Lord took me from tending the flock(AG) and said to me, ‘Go,(AH) prophesy(AI) to my people Israel.’(AJ) 16 Now then, hear(AK) the word of the Lord. You say,

“‘Do not prophesy against(AL) Israel,
    and stop preaching against the descendants of Isaac.’

17 “Therefore this is what the Lord says:

“‘Your wife will become a prostitute(AM) in the city,
    and your sons and daughters will fall by the sword.
Your land will be measured and divided up,
    and you yourself will die in a pagan[c] country.
And Israel will surely go into exile,(AN)
    away from their native land.(AO)’”

Footnotes

  1. Amos 7:7 The meaning of the Hebrew for this phrase is uncertain.
  2. Amos 7:7 The meaning of the Hebrew for this phrase is uncertain; also in verse 8.
  3. Amos 7:17 Hebrew an unclean