Add parallel Print Page Options

Aisraeli Azunzidwa ku Igupto

Awa ndi mayina a ana a Israeli amene anapita ku Igupto pamodzi ndi Yakobo abambo awo, aliyense ndi banja lake: Rubeni, Simeoni, Levi, Yuda; Isakara, Zebuloni, Benjamini; Dani, Nafutali; Gadi ndi Aseri. Anthu onse obadwa mwa Yakobo analipo 70. Yosefe nʼkuti ali kale ku Igupto.

Tsono Yosefe ndi abale ake onse ndiponso mʼbado wawo wonse anamwalira. Koma Aisraeli anaberekana ndi kuchuluka kwambiri nakhala amphamvu kwambiri, kotero kuti anadzaza dzikolo.

Pambuyo pake mfumu yatsopano imene sinkamudziwa Yosefe, inayamba kulamulira dziko la Igupto. Iyo inati kwa anthu ake, “Taonani, Aisraeli achuluka ndipo ndi amphamvu kwambiri kuposa ife. 10 Tiyeni tiwachenjerere. Tikapanda kutero adzachuluka kuposa ife, ndipo ngati kutakhala nkhondo, adzadziphatika kwa adani athu nadzamenyana nafe, kenaka nʼkudzachoka mʼdziko muno.”

11 Kotero anayika akapitawo kuti aziwazunza ndi kuwagwiritsa ntchito yolemetsa mokakamiza. Iwo anamangira Farao mizinda ya Pitomu ndi Ramesesi kumene ankasungirako chakudya. 12 Koma pamene ankawazunza kwambiri, Aisraeli ndiye ankachulukirachulukira mpaka kubalalikira mʼdziko lonse. Kotero Aigupto anayamba kuopa Aisraeliwo 13 ndipo anawagwiritsa ntchito mwankhanza kwambiri. 14 Aigupto anachititsa moyo wa Aisraeli kukhala owawa kwambiri powagwiritsa ntchito yakalavulagaga yowumba njerwa ndi kuponda dothi lomangira, pamodzi ndi ntchito zina zosiyanasiyana zamʼminda. Iwo anakakamiza Aisraeli mwankhanza kuti agwire ntchito yowawayi.

Azamba Akana Kumvera Mfumu

15 Mfumu ya Igupto inati kwa azamba a Chihebri omwe mayina awo anali Sifira ndi Puwa, 16 “Mukamathandiza amayi a Chihebri pa mwala wochirira, muzionetsetsa kuti akabadwa mwana wamwamuna muzipha, koma akakhala wamkazi muzimuleka akhale ndi moyo.” 17 Koma azambawo ankaopa Mulungu ndipo sanachite zimene mfumu ya Igupto inawawuza kuti achite. Iwo analeka ana aamuna kuti akhale ndi moyo. 18 Kenaka mfumu ya Igupto inayitanitsa azamba aja ndi kuwafunsa kuti, “Chifukwa chiyani mwachita zimenezi? Bwanji mwasiya ana aamuna kuti akhale ndi moyo?”

19 Azambawo anamuyankha Farao kuti, “Amayi a Chihebri sali ngati amayi a Chiigupto; Iwo ndi amphamvu ndipo amachira azamba asanafike.”

20 Kotero Mulungu anawakomera mtima azambawo, ndipo Aisraeli anapitirirabe kuchulukana nakhala amphamvu kwambiri. 21 Pakuti azambawo ankaopa Mulungu, Iye anawapatsa mabanja awoawo.

22 Pamenepo Farao analamulira anthu ake onse kuti, “Mwana wamwamuna aliyense akabadwa, mukamuponye mu mtsinje wa Nailo, koma wamkazi mulekeni akhale ndi moyo.”

The Israelites Oppressed

These are the names of the sons of Israel(A) who went to Egypt with Jacob, each with his family: Reuben, Simeon, Levi and Judah; Issachar, Zebulun and Benjamin; Dan and Naphtali; Gad and Asher.(B) The descendants of Jacob numbered seventy[a] in all;(C) Joseph was already in Egypt.

Now Joseph and all his brothers and all that generation died,(D) but the Israelites were exceedingly fruitful; they multiplied greatly, increased in numbers(E) and became so numerous that the land was filled with them.

Then a new king, to whom Joseph meant nothing, came to power in Egypt.(F) “Look,” he said to his people, “the Israelites have become far too numerous(G) for us.(H) 10 Come, we must deal shrewdly(I) with them or they will become even more numerous and, if war breaks out, will join our enemies, fight against us and leave the country.”(J)

11 So they put slave masters(K) over them to oppress them with forced labor,(L) and they built Pithom and Rameses(M) as store cities(N) for Pharaoh. 12 But the more they were oppressed, the more they multiplied and spread; so the Egyptians came to dread the Israelites 13 and worked them ruthlessly.(O) 14 They made their lives bitter with harsh labor(P) in brick(Q) and mortar and with all kinds of work in the fields; in all their harsh labor the Egyptians worked them ruthlessly.(R)

15 The king of Egypt said to the Hebrew midwives,(S) whose names were Shiphrah and Puah, 16 “When you are helping the Hebrew women during childbirth on the delivery stool, if you see that the baby is a boy, kill him; but if it is a girl, let her live.”(T) 17 The midwives, however, feared(U) God and did not do what the king of Egypt had told them to do;(V) they let the boys live. 18 Then the king of Egypt summoned the midwives and asked them, “Why have you done this? Why have you let the boys live?”

19 The midwives answered Pharaoh, “Hebrew women are not like Egyptian women; they are vigorous and give birth before the midwives arrive.”(W)

20 So God was kind to the midwives(X) and the people increased and became even more numerous. 21 And because the midwives feared(Y) God, he gave them families(Z) of their own.

22 Then Pharaoh gave this order to all his people: “Every Hebrew boy that is born you must throw into the Nile,(AA) but let every girl live.”(AB)

Footnotes

  1. Exodus 1:5 Masoretic Text (see also Gen. 46:27); Dead Sea Scrolls and Septuagint (see also Acts 7:14 and note at Gen. 46:27) seventy-five