Add parallel Print Page Options

21 “Uwawuze Aisraeli malamulo awa:

Antchito a Chihebri

“Mukagula kapolo wa Chihebri, azikugwirirani ntchito zaka zisanu ndi chimodzi. Koma mʼchaka cha chisanu ndi chiwiri muzimumasula, ndipo asalipire kanthu. Ngati anabwera yekha, amasulidwenso yekha. Koma ngati anali ndi mkazi pamene ankabwera, mkaziyo apite nayenso. Ngati bwana wake amupatsa mkazi ndipo mkaziyo anabereka ana aamuna kapena aakazi, mkazi ndi anawo adzakhala a bwanayo ndipo mwamuna yekhayo ndiye adzamasulidwe.

“Koma ngati kapoloyo alengeza kuti, ‘Ine sindikufuna kumasulidwa chifukwa ndimakonda mbuye wanga, mkazi wanga ndi ana,’ mbuye wakeyo abwere naye kwa Yehova. Abwere naye pa chitseko kapena pa mphuthu zachitseko ndipo abowole khutu lake ndi chitsulo. Ndipo iye adzakhala kapolo wake moyo wake wonse.

“Ngati munthu agulitsa mwana wake wamkazi kukhala mdzakazi, mwanayo asamasulidwe monga achitira ndi akapolo aamuna. Koma ngati mkaziyo sakukondweretsa bwana wake amene wamusankha kuti amukwatire, amulole kuti awomboledwe. Bwanayo alibe mphamvu zomugulitsa kwa anthu achilendo, chifukwa iyeyo waphwanya pangano lake lomukwatira iye. Ngati anamusankha kuti akhale mkazi wa mwana wake, ayenera kumusunga ngati mwana wake wamkazi. 10 Ngati akwatira mkazi wina, asamumane woyambayo chakudya ngakhale chovala ndipo apiritirize kugona naye ngati mkazi wake. 11 Koma ngati sangathe kumuchitira zonsezi, ndiye amuleke apite popanda kulipira kanthu.

Munthu Akapwetekedwa

12 “Munthu aliyense amene amenya mnzake namupha, iyenso ayenera kuphedwa. 13 Koma ngati sanachite dala, ndipo Mulungu analola kuti zichitike, iyeyo athawire ku malo kumene ndidzakupatsani. 14 Koma ngati munthu akonza chiwembu ndi kupha mnzake mwadala, ameneyo muchotseni ngakhale ku guwa langa lansembe ndipo aphedwe.

15 “Munthu aliyense amene amenya abambo ake kapena mayi ake ayenera kuphedwa.

16 “Munthu aliyense amene aba munthu mnzake, ndi kukamugulitsa, kapena kumangomusunga, ayenera kuphedwa.

17 “Aliyense amene atemberera abambo ake kapena amayi ake ayenera kuphedwa.

18 “Ngati anthu awiri akangana ndipo wina amenya mnzake ndi mwala kapena nkhonya koma wosamupha, womenyedwayo akadwala nagona pa bedi, 19 kenaka nachira ndi kuyamba kuyenda ndi ndodo kutuluka kunja kwa nyumba yake, ndiye kuti womenya mnzakeyo sadzayimbidwa mlandu. Komabe adzayenera kulipira womenyedwayo chifukwa cha nthawi imene anagona pa bedi ija, ndiponso ayenera kumusala mpaka atachiritsitsa.

20 “Ngati munthu amenya kapolo wake wamwamuna kapena mdzakazi ndi ndodo, kapolo uja ndikufa chifukwa cha kumenyedwako, munthuyo ayenera kulangidwa. 21 Koma ngati kapolo uja akhala ndi moyo tsiku lonse kapena masiku awiri, ndiye kuti mbuye uja asalangidwe chifukwa kapolo ndi chuma chake.

22 “Ngati anthu akumenyana ndi kupweteka mayi woyembekezera, mayiyo napita padera, koma osavulala, wolakwayo ayenera kulipira chilichonse chimene mwamuna wake wa mkaziyo adzalamula ndipo bwalo lamilandu lavomereza. 23 Koma ngati wavulazidwa kwambiri, ndiye malipiro ake adzakhala motere: moyo kulipa moyo, 24 diso kulipira diso, dzino kulipira dzino, mkono kulipa mkono, phazi kulipa phazi. 25 Kutentha ndi moto kulipa kutentha ndi moto, bala kulipa bala, mkwingwirima kulipa mkwingwirima.

26 “Ngati munthu amenya wantchito wake wa mwamuna kapena mdzakazi wake pa diso ndi kuliwononga, wantchitoyo amasulidwe ngati malipiro a diso lake. 27 Ndipo ngati agulula dzino la wantchito wamwamuna kapena mdzakazi, wantchitoyo amasulidwe ngati malipiro a dzino lake.

28 “Ngati ngʼombe ipha munthu wamwamuna kapena wamkazi ndi nyanga yake, iponyedwe miyala ndipo nyama yake isadyedwe. Ndipo mwini ngʼombeyo asayimbidwe mlandu. 29 Koma ngati ngʼombeyo inali ndi chizolowezi chogunda anthu ndipo mwini wakeyo anachenjezedwa koma iye sanayimange ndipo yapha mwamuna kapena mkazi, ngʼombeyo iponyedwe miyala ndipo mwini wakeyo aphedwenso. 30 Koma ngati wauzidwa kuti alipire, iye apereke zimene wauzidwazo kuti awombole moyo wake. 31 Lamulo ili ligwirenso ntchito ngati ngʼombeyo yagunda mwana wamwamuna kapena wamkazi. 32 Ngati ngʼombeyo yagunda kapolo wamwamuna kapena mdzakazi, mwini ngʼombeyo apereke masekeli makumi atatu a siliva kwa mwini kapoloyo, ndipo ngʼombeyo iponyedwe miyala.

33 “Munthu akasiya dzenje lapululu kapena akakumba dzenje koma wosaphimbapo, ndipo ngʼombe kapena bulu nʼkugweramo, 34 mwini dzenjelo amulipire mwini chiweto chakufacho koma iye atenge chiwetocho.

35 “Ngati ngʼombe ya munthu wina ipha ngʼombe ya mnzake, ngʼombe yamoyo ija igulitsidwe ndipo anthu awiriwo agawane pakati ndalama yake. Achite chimodzimodzi ndi ngʼombe yakufa ija. 36 Koma zikadziwika kuti ngʼombeyo inali ndi khalidwe logunda, ndipo mwini wake samayitsekera mʼkhola, mwini ngʼombeyo alipire ngʼombe ina yamoyo koma atenge yakufayo.”

21 “These are the laws(A) you are to set before them:

Hebrew Servants(B)(C)

“If you buy a Hebrew servant,(D) he is to serve you for six years. But in the seventh year, he shall go free,(E) without paying anything. If he comes alone, he is to go free alone; but if he has a wife when he comes, she is to go with him. If his master gives him a wife and she bears him sons or daughters, the woman and her children shall belong to her master, and only the man shall go free.

“But if the servant declares, ‘I love my master and my wife and children and do not want to go free,’(F) then his master must take him before the judges.[a](G) He shall take him to the door or the doorpost and pierce(H) his ear with an awl. Then he will be his servant for life.(I)

“If a man sells his daughter as a servant, she is not to go free as male servants do. If she does not please the master who has selected her for himself,[b] he must let her be redeemed. He has no right to sell her to foreigners, because he has broken faith with her. If he selects her for his son, he must grant her the rights of a daughter. 10 If he marries another woman, he must not deprive the first one of her food, clothing and marital rights.(J) 11 If he does not provide her with these three things, she is to go free, without any payment of money.

Personal Injuries

12 “Anyone who strikes a person with a fatal blow is to be put to death.(K) 13 However, if it is not done intentionally, but God lets it happen, they are to flee to a place(L) I will designate. 14 But if anyone schemes and kills someone deliberately,(M) that person is to be taken from my altar and put to death.(N)

15 “Anyone who attacks[c] their father or mother is to be put to death.

16 “Anyone who kidnaps someone is to be put to death,(O) whether the victim has been sold(P) or is still in the kidnapper’s possession.

17 “Anyone who curses their father or mother is to be put to death.(Q)

18 “If people quarrel and one person hits another with a stone or with their fist[d] and the victim does not die but is confined to bed, 19 the one who struck the blow will not be held liable if the other can get up and walk around outside with a staff; however, the guilty party must pay the injured person for any loss of time and see that the victim is completely healed.

20 “Anyone who beats their male or female slave with a rod must be punished if the slave dies as a direct result, 21 but they are not to be punished if the slave recovers after a day or two, since the slave is their property.(R)

22 “If people are fighting and hit a pregnant woman and she gives birth prematurely[e] but there is no serious injury, the offender must be fined whatever the woman’s husband demands(S) and the court allows. 23 But if there is serious injury, you are to take life for life,(T) 24 eye for eye, tooth for tooth,(U) hand for hand, foot for foot, 25 burn for burn, wound for wound, bruise for bruise.

26 “An owner who hits a male or female slave in the eye and destroys it must let the slave go free to compensate for the eye. 27 And an owner who knocks out the tooth of a male or female slave must let the slave go free to compensate for the tooth.

28 “If a bull gores a man or woman to death, the bull is to be stoned to death,(V) and its meat must not be eaten. But the owner of the bull will not be held responsible. 29 If, however, the bull has had the habit of goring and the owner has been warned but has not kept it penned up(W) and it kills a man or woman, the bull is to be stoned and its owner also is to be put to death. 30 However, if payment is demanded, the owner may redeem his life by the payment of whatever is demanded.(X) 31 This law also applies if the bull gores a son or daughter. 32 If the bull gores a male or female slave, the owner must pay thirty shekels[f](Y) of silver to the master of the slave, and the bull is to be stoned to death.

33 “If anyone uncovers a pit(Z) or digs one and fails to cover it and an ox or a donkey falls into it, 34 the one who opened the pit must pay the owner for the loss and take the dead animal in exchange.

35 “If anyone’s bull injures someone else’s bull and it dies, the two parties are to sell the live one and divide both the money and the dead animal equally. 36 However, if it was known that the bull had the habit of goring, yet the owner did not keep it penned up,(AA) the owner must pay, animal for animal, and take the dead animal in exchange.

Footnotes

  1. Exodus 21:6 Or before God
  2. Exodus 21:8 Or master so that he does not choose her
  3. Exodus 21:15 Or kills
  4. Exodus 21:18 Or with a tool
  5. Exodus 21:22 Or she has a miscarriage
  6. Exodus 21:32 That is, about 12 ounces or about 345 grams