Add parallel Print Page Options

Mʼndandanda wa Akuluakulu a Mabanja Amene Anabwera ndi Ezara

Nawa mayina a atsogoleri a mabanja amene anabwera nane kuchokera ku Babuloni nthawi ya ulamuliro wa mfumu Aritasasita:

Geresomu wa fuko la Finehasi;

Danieli wa fuko la Itamara;

Hatusi mwana wa Sekaniya wa fuko la Davide;

Zekariya wa fuko la Parosi. Pamodzi ndi iyeyu panalembedwa anthu ena 150;

Elihunai mwana wa Zerahiya, wa fuko la Pahati-Mowabu. Pamodzi ndi iyeyu panalinso anthu ena 400.

Sekaniya, mwana wa Yahazieli wa fuko la Zatu. Pamodzi ndi iyeyu panalembedwanso anthu 300.

Ebedi, mwana wa Yonatani wa fuko la Adini. Pamodzi naye analembedwanso anthu ena makumi asanu.

Yesaiya, mwana wa Ataliya wa fuko la Elamu. Pamodzi naye panali anthu ena 70.

Zebadiya, mwana wa Mikayeli wa fuko la Sefatiya. Pamodzi naye panalinso anthu 80.

Obadiya, mwana wa Yehieli wa fuko la Yowabu. Pamodzi naye panalinso anthu 218.

10 Selomiti mwana wa Yosifiya wa fuko la Bani. Pamodzi ndi iyeyu panalinso anthu 160.

11 Zekariya, mwana wa Bebai wa fuko la Babai. Pamodzi naye analembedwanso anthu 28.

12 Yohanani, mwana wa Hakatani wa fuko la Azigadi. Pamodzi naye panalinso anthu 110.

13 Atsogoleri a fuko la Adonikamu, anthu amene anabwera pambuyo pake mayina awo anali Elifeleti, Yeiyeli ndi Semaya. Pamodzi ndi iwowa panalinso anthu 60.

14 Atsogoleri a fuko la Bigivai anali Utai ndi Zakuri. Pamodzi ndi iwowa panali anthu 70.

Kubwerera ku Yerusalemu

15 Anthu onse ndinawasonkhanitsa ku mtsinje umene umapita mpaka ku Ahava, ndipo kumeneko tinagona mʼmisasa masiku atatu. Nditayangʼana pakati pa anthu ndi ansembe, ndinapeza kuti panalibe Alevi. 16 Choncho ndinayitana atsogoleri awa: Eliezara, Arieli, Semaiya, Elinatani, Yaribu, Elinatani, Natani, Zekariya ndi Mesulamu, pamodzi ndi aphunzitsi awiri, Yoyaribu ndi Elinatani, 17 ndipo ndinawatuma kwa Ido, mtsogoleri wa malo otchedwa Kasifiya. Ine ndinawawuza zoti akanene kwa Ido ndi kwa abale ake, ogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu ku Kasifiyako, kuti atitumizire anthu odzatumikira ku Nyumba ya Mulungu. 18 Chifukwa cha kutikomera mtima kwa Mulungu wathu, Ido anatitumizira munthu wanzeru, Serabiya, wa fuko la Mahili, mwana wa Levi, mwana wa Israeli, pamodzi ndi ana ake aamuna ndi abale ake, anthu 18. 19 Anatitumiziranso Hasabiya ndi Yesaiya wa fuko la Merari pamodzi ndi abale ake ndi adzukulu ake, anthu makumi awiri. 20 Panalinso anthu ena 220 mwa anthu ogwira ntchito mʼNyumba ya Mulungu amene Davide ndi nduna zake anawasankha kuti azitumikira Alevi. Anthu onsewa analembedwa potsata mayina awo.

21 Ku mtsinje wa Ahava, ndinalengeza kuti anthu onse asale zakudya, adzichepetse pamaso pa Mulungu wathu ndi kupempha kuti atiyendetse bwino ife ndi ana athu, ndi kuteteza katundu wathu yense. 22 Ine ndinali ndi manyazi kupempha mfumu kuti atipatse asilikali oyenda pansi ndi ena okwera pa akavalo kuti atiteteze kwa adani athu pa ulendo wathuwu popeza tinali titawuza kale mfumu kuti “Yehova amateteza aliyense amene amamudalira, koma amakwiyira onse amene amamukana.” 23 Choncho tinasala zakudya ndi kupemphera kwa Mulungu wathu kuti atiteteze ndipo Iye anamva pemphero lathu.

24 Tsono ndinasankha atsogoleri a ansembe khumi ndi awiri awa, Serebiya, Hasabiya ndi abale awo khumi 25 ndipo ndinawayezera siliva ndi golide, ndiponso ziwiya ndi zopereka za ku Nyumba ya Mulungu wathu zimene mfumu ndi alangizi ake, nduna zake ndi Aisraeli onse amene anali kumeneko anazipereka. 26 Nditayeza zonse, ndinapereka mʼmanja mwawo, matani 22 asiliva, ziwiya zasiliva zolemera makilogalamu 70, ndiponso makilogalamu 3,400 a golide, 27 mbale zagolide makumi awiri zolemera makilogalamu asanu ndi atatu ndi theka ndiponso ziwiya ziwiri zamkuwa wosalala, wonyezimira bwino ngati golide wamtengowapatali.

28 Kenaka ndinawawuza kuti, “Inu ndi opatulika a Yehova, ndiponso mphatso zonsezi ndi zopatulika. Siliva ndi golideyu ndi zopereka zaufulu kwa Yehova, Mulungu wa makolo anu. 29 Muzisamale bwino mpaka mutaziyeza pamaso pa atsogoleri a ansembe ndi Alevi ndi akulu a mabanja a Israeli mʼzipinda za mʼNyumba ya Mulungu ku Yerusalemu.” 30 Choncho ansembe ndi Alevi analandira zonse zoyezedwa zija, siliva, golide pamodzi ndi ziwiya kuti apite nazo ku Nyumba ya Yehova ku Yerusalemu.

31 Pa tsiku la khumi ndi chiwiri la mwezi woyamba, tinachoka ku mtsinje wa Ahava kupita ku Yerusalemu. Ndipo Mulungu wathu anali nafe, ndipo anatiteteza kwa adani athu makamaka otibisalira pa njira. 32 Tinafika ku Yerusalemu, komwe tinapumula masiku atatu.

33 Pa tsiku la chinayi lake, mʼNyumba ya Mulungu wathu, tinayeza siliva ndi golide ndi ziwiya zija nʼkuzipereka mʼmanja mwa Meremoti mwana wa wansembe Uriya. Pamodzi ndi iyeyo panali Eliezara mwana wa Finehasi ndiponso Alevi awa: Yozabadi mwana wa Yesuwa ndi Nowadiya mwana wa Binuyi. 34 Zonsezi anaziwerenga ndi kuziyeza ndipo analemba kulemera kwa chinthu chilichonse.

35 Pamenepo anthu amene anatengedwa ukapolo aja anabwerera, anapereka nsembe zopsereza kwa Mulungu wa Israeli: ngʼombe zazimuna khumi ndi ziwiri, kuperekera Aisraeli onse, nkhosa zazimuna 96, ana ankhosa 77, ndiponso mbuzi zazimuna khumi ndi ziwiri ngati nsembe yopepesera machimo. Zonsezi zinali nsembe yopsereza zopereka kwa Yehova. 36 Iwo anaperekanso chidziwitso cha mfumu chija kwa akuluakulu a mfumu ndi kwa akazembe a mʼdera la Patsidya pa Yufurate. Pamenepo iwo anathandiza Ayuda ndiponso ntchito za pa Nyumba ya Mulungu.

List of the Family Heads Returning With Ezra

These are the family heads and those registered with them who came up with me from Babylon during the reign of King Artaxerxes:(A)

of the descendants of Phinehas, Gershom;

of the descendants of Ithamar, Daniel;

of the descendants of David, Hattush of the descendants of Shekaniah;(B)

of the descendants of Parosh,(C) Zechariah, and with him were registered 150 men;

of the descendants of Pahath-Moab,(D) Eliehoenai son of Zerahiah, and with him 200 men;

of the descendants of Zattu,[a] Shekaniah son of Jahaziel, and with him 300 men;

of the descendants of Adin,(E) Ebed son of Jonathan, and with him 50 men;

of the descendants of Elam, Jeshaiah son of Athaliah, and with him 70 men;

of the descendants of Shephatiah, Zebadiah son of Michael, and with him 80 men;

of the descendants of Joab, Obadiah son of Jehiel, and with him 218 men;

10 of the descendants of Bani,[b] Shelomith son of Josiphiah, and with him 160 men;

11 of the descendants of Bebai, Zechariah son of Bebai, and with him 28 men;

12 of the descendants of Azgad, Johanan son of Hakkatan, and with him 110 men;

13 of the descendants of Adonikam,(F) the last ones, whose names were Eliphelet, Jeuel and Shemaiah, and with them 60 men;

14 of the descendants of Bigvai, Uthai and Zakkur, and with them 70 men.

The Return to Jerusalem

15 I assembled them at the canal that flows toward Ahava,(G) and we camped there three days. When I checked among the people and the priests, I found no Levites(H) there. 16 So I summoned Eliezer, Ariel, Shemaiah, Elnathan, Jarib, Elnathan, Nathan, Zechariah and Meshullam, who were leaders, and Joiarib and Elnathan, who were men of learning, 17 and I ordered them to go to Iddo, the leader in Kasiphia. I told them what to say to Iddo and his fellow Levites, the temple servants(I) in Kasiphia, so that they might bring attendants to us for the house of our God. 18 Because the gracious hand of our God was on us,(J) they brought us Sherebiah,(K) a capable man, from the descendants of Mahli son of Levi, the son of Israel, and Sherebiah’s sons and brothers, 18 in all; 19 and Hashabiah, together with Jeshaiah from the descendants of Merari, and his brothers and nephews, 20 in all. 20 They also brought 220 of the temple servants(L)—a body that David and the officials had established to assist the Levites. All were registered by name.

21 There, by the Ahava Canal,(M) I proclaimed a fast, so that we might humble ourselves before our God and ask him for a safe journey(N) for us and our children, with all our possessions. 22 I was ashamed to ask the king for soldiers(O) and horsemen to protect us from enemies on the road, because we had told the king, “The gracious hand of our God is on everyone(P) who looks to him, but his great anger is against all who forsake him.(Q) 23 So we fasted(R) and petitioned our God about this, and he answered our prayer.

24 Then I set apart twelve of the leading priests, namely, Sherebiah,(S) Hashabiah and ten of their brothers, 25 and I weighed out(T) to them the offering of silver and gold and the articles that the king, his advisers, his officials and all Israel present there had donated for the house of our God. 26 I weighed out to them 650 talents[c] of silver, silver articles weighing 100 talents,[d] 100 talents[e] of gold, 27 20 bowls of gold valued at 1,000 darics,[f] and two fine articles of polished bronze, as precious as gold.

28 I said to them, “You as well as these articles are consecrated to the Lord.(U) The silver and gold are a freewill offering to the Lord, the God of your ancestors. 29 Guard them carefully until you weigh them out in the chambers of the house of the Lord in Jerusalem before the leading priests and the Levites and the family heads of Israel.” 30 Then the priests and Levites received the silver and gold and sacred articles that had been weighed out to be taken to the house of our God in Jerusalem.

31 On the twelfth day of the first month we set out from the Ahava Canal(V) to go to Jerusalem. The hand of our God was on us,(W) and he protected us from enemies and bandits along the way. 32 So we arrived in Jerusalem, where we rested three days.(X)

33 On the fourth day, in the house of our God, we weighed out(Y) the silver and gold and the sacred articles into the hands of Meremoth(Z) son of Uriah, the priest. Eleazar son of Phinehas was with him, and so were the Levites Jozabad(AA) son of Jeshua and Noadiah son of Binnui.(AB) 34 Everything was accounted for by number and weight, and the entire weight was recorded at that time.

35 Then the exiles who had returned from captivity sacrificed burnt offerings to the God of Israel: twelve bulls(AC) for all Israel,(AD) ninety-six rams, seventy-seven male lambs and, as a sin offering,[g] twelve male goats.(AE) All this was a burnt offering to the Lord. 36 They also delivered the king’s orders(AF) to the royal satraps and to the governors of Trans-Euphrates,(AG) who then gave assistance to the people and to the house of God.(AH)

Footnotes

  1. Ezra 8:5 Some Septuagint manuscripts (also 1 Esdras 8:32); Hebrew does not have Zattu.
  2. Ezra 8:10 Some Septuagint manuscripts (also 1 Esdras 8:36); Hebrew does not have Bani.
  3. Ezra 8:26 That is, about 24 tons or about 22 metric tons
  4. Ezra 8:26 That is, about 3 3/4 tons or about 3.4 metric tons
  5. Ezra 8:26 That is, about 3 3/4 tons or about 3.4 metric tons
  6. Ezra 8:27 That is, about 19 pounds or about 8.4 kilograms
  7. Ezra 8:35 Or purification offering