Add parallel Print Page Options

Chimaliziro Chafika

Yehova anandipatsa uthenga uwu kuti, “Iwe mwana wa munthu, Ine Ambuye Yehova ndikuwuza dziko la Israeli kuti:

“Chimaliziro! Chimaliziro chafika
    ku ngodya zinayi za dziko.
Chimaliziro chili pa iwe tsopano.
    Mkwiyo wanga ndidzawuthira pa iwe.
Ndidzakuweruza molingana ndi machitidwe ako
    ndi kukulanga chifukwa cha zonyansa zako.
Ine sindidzakumvera chisoni
    kapena kukuleka.
Ndidzakulanga ndithu chifukwa cha ntchito zako zoyipa
    komanso chifukwa cha miyambo yako yonyansa imene ili pakati pako.

Pamenepo udzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”

“Zimene ndikunena Ine Ambuye Yehova ndi izi:

“Chiwonongeko! Chiwonongeko chimene sichinamvekepo!
    Taona chikubwera!
Chimaliziro chafika!
    Chimaliziro chafika!
Chiwonongeko chakugwera.
    Taona chafika!
Inu anthu okhala mʼdziko,
    chiwonongeko chakugwerani.
Nthawi yafika, tsiku layandikira; tsiku la chisokonezo osati la chimwemwe pa mapiri.
Ine ndili pafupi kukukwiyirani,
    ndipo ukali wanga udzathera pa iwe;
Ine ndidzakuweruza molingana ndi machitidwe ako
    ndiponso ndidzakulanga chifukwa cha miyambo yako yonyansa.
Ine sindidzakumvera chisoni
    kapena kukuleka.
Ndidzakulanga malingana ndi ntchito zako
ndiponso chifukwa cha miyambo yako yonyansa pakati pako.

‘Pamenepo udzadziwa kuti Ine Yehova ndine amene ndimakantha.’

10 “Taona, tsikulo!
    Taona, lafika!
Chiwonongeko chako chabwera.
    Ndodo yaphuka mphundu za maluwa.
    Kudzitama kwaphuka.
11 Chiwawa chasanduka ndodo
    yowakwapulira chifukwa cha kuyipa kwawo.
Palibe mwa anthu amenewo amene adzatsale.
    Palibe ndi mmodzi yemwe mwa unyinji wawo.
Palibiretu ndipo sipadzapezeka
    munthu wowalira maliro.
12 Nthawi yafika!
    Tsiku layandikira!
Munthu wogula asakondwere
    ndipo wogulitsa asamve chisoni,
    popeza ukali wanga uli pa gulu lonse.
13 Wogulitsa sadzazipezanso zinthu
    zimene anagulitsa kwa wina
    chinkana onse awiri akanali ndi moyo,
pakuti chilango chidzagwera onsewo
    ndipo sichingasinthike.
Chifukwa cha machimo awo, palibe aliyense
    amene adzapulumutsa moyo wake.

14 “Lipenga lalira,
    ndipo zonse zakonzeka.
Koma palibe ndi mmodzi yemwe amene akupita ku nkhondo,
    pakuti mkwiyo wanga uli pa gulu lonse.
15 Ku bwalo kuli kumenyana
    ndipo mʼkati muli mliri ndi njala.
Anthu okhala ku midzi
    adzafa ndi nkhondo.
Iwo okhala ku mizinda
    adzafa ndi mliri ndi njala.
16 Onse amene adzapulumuka
    ndi kumakakhala ku mapiri,
azidzalira ngati nkhunda za ku zigwa.
    Aliyense azidzabuwula chifukwa cha machimo ake.
17 Dzanja lililonse lidzalefuka,
    ndipo bondo lililonse lidzalobodoka ngati madzi.
18 Iwo adzavala ziguduli
    ndipo adzagwidwa ndi mantha.
Adzakhala ndi nkhope zamanyazi
    ndipo mitu yawo adzameta mpala.

19 “Iwo adzataya siliva wawo mʼmisewu
    ndipo golide wawo adzakhala chinthu chonyansa.
Siliva ndi golide wawo
    sizidzatha kuwapulumutsa
    pa tsiku la ukali wa Yehova.
Chuma chawochi sichidzawathandiza kuthetsa njala,
    kapena kukhala okhuta,
    pakuti ndicho chinawagwetsa mʼmachimo.
20 Iwo ankanyadira zodzikongoletsera zawo zamakaka
    ndipo ankazigwiritsa ntchito kupanga mafano awo onyansa ndi zonyansa zawo zina.
Nʼchifukwa chake Ine ndidzazisandutsa
    kukhala zowanyansa.
21 Ndidzazipereka kwa alendo kuti azifunkhe.
    Anthu oyipa a dziko lapansi adzazilanda
    ndi kudziyipitsa.
22 Ine ndidzawalekerera anthuwo
    ndipo adzayipitsa malo anga apamtima.
Adzalowamo ngati mbala
    ndi kuyipitsamo.

23 “Konzani maunyolo,

    chifukwa dziko ladzaza ndi anthu opha anzawo
    ndipo mzinda wadzaza ndi chiwawa.
24 Ndidzabweretsa mitundu ya anthu oyipitsitsa
    kuti idzalande nyumba zawo.
Ndidzathetsa kunyada kwa anthu amphamvu
    pamene anthu akunja adzalowa mʼmalo awo achipembedzo ndi kuyipitsamo.
25 Nkhawa ikadzawafikira
    adzafunafuna mtendere koma osawupeza.
26 Tsoka lidzatsatana ndi tsoka linzake,
    ndipo mphekesera idzatsatana ndi mphekesera inzake.
Iwo adzayesa kufuna masomphenya kuchokera kwa mneneri.
    Adzasowa ansembe owaphunzitsa malamulo,
    ndipo anthu akuluakulu sadzakhalanso ndi uphungu.
27 Mfumu idzalira,
    kalonga adzagwidwa ndi mantha.
    Manja a anthu a mʼdzikomo azidzangonjenjemera ndi mantha.
Ine ndidzawalanga molingana ndi machitidwe awo,
    ndipo ndidzawaweruza molingana ndi momwe anaweruzira anzawo.

Choncho adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”

The End Has Come

The word of the Lord came to me: “Son of man, this is what the Sovereign Lord says to the land of Israel:

“‘The end!(A) The end has come
    upon the four corners(B) of the land!
The end is now upon you,
    and I will unleash my anger against you.
I will judge you according to your conduct(C)
    and repay you for all your detestable practices.(D)
I will not look on you with pity;(E)
    I will not spare you.
I will surely repay you for your conduct
    and for the detestable practices among you.

“‘Then you will know that I am the Lord.’(F)

“This is what the Sovereign Lord says:

“‘Disaster!(G) Unheard-of[a] disaster!
    See, it comes!
The end(H) has come!
    The end has come!
It has roused itself against you.
    See, it comes!
Doom has come upon you,
    upon you who dwell in the land.
The time has come! The day(I) is near!(J)
    There is panic, not joy, on the mountains.
I am about to pour out my wrath(K) on you
    and spend my anger against you.
I will judge you according to your conduct
    and repay you for all your detestable practices.(L)
I will not look on you with pity;
    I will not spare you.(M)
I will repay you for your conduct
    and for the detestable practices among you.(N)

“‘Then you will know that it is I the Lord who strikes you.(O)

10 “‘See, the day!
    See, it comes!
Doom has burst forth,
    the rod(P) has budded,
    arrogance has blossomed!
11 Violence(Q) has arisen,[b]
    a rod to punish the wicked.
None of the people will be left,
    none of that crowd—
none of their wealth,
    nothing of value.(R)
12 The time has come!
    The day has arrived!
Let not the buyer(S) rejoice
    nor the seller grieve,
    for my wrath is on the whole crowd.(T)
13 The seller will not recover
    the property that was sold—
    as long as both buyer and seller live.
For the vision concerning the whole crowd
    will not be reversed.
Because of their sins, not one of them
    will preserve their life.(U)

14 “‘They have blown the trumpet,(V)
    they have made all things ready,
but no one will go into battle,
    for my wrath(W) is on the whole crowd.
15 Outside is the sword;
    inside are plague and famine.
Those in the country
    will die by the sword;
those in the city
    will be devoured by famine and plague.(X)
16 The fugitives(Y) who escape
    will flee to the mountains.
Like doves(Z) of the valleys,
    they will all moan,
    each for their own sins.(AA)
17 Every hand will go limp;(AB)
    every leg will be wet with urine.(AC)
18 They will put on sackcloth(AD)
    and be clothed with terror.(AE)
Every face will be covered with shame,
    and every head will be shaved.(AF)

19 “‘They will throw their silver into the streets,(AG)
    and their gold will be treated as a thing unclean.
Their silver and gold
    will not be able to deliver them
    in the day of the Lord’s wrath.(AH)
It will not satisfy(AI) their hunger
    or fill their stomachs,
    for it has caused them to stumble(AJ) into sin.(AK)
20 They took pride in their beautiful jewelry
    and used it to make(AL) their detestable idols.
They made it into vile images;(AM)
    therefore I will make it a thing unclean for them.(AN)
21 I will give their wealth as plunder(AO) to foreigners
    and as loot to the wicked of the earth,
    who will defile it.(AP)
22 I will turn my face(AQ) away from the people,
    and robbers will desecrate the place I treasure.
They will enter it
    and will defile it.(AR)

23 “‘Prepare chains!
    For the land is full of bloodshed,(AS)
    and the city is full of violence.(AT)
24 I will bring the most wicked of nations
    to take possession of their houses.
I will put an end to the pride of the mighty,
    and their sanctuaries(AU) will be desecrated.(AV)
25 When terror comes,
    they will seek peace in vain.(AW)
26 Calamity upon calamity(AX) will come,
    and rumor upon rumor.
They will go searching for a vision from the prophet,(AY)
    priestly instruction in the law will cease,
    the counsel of the elders will come to an end.(AZ)
27 The king will mourn,
    the prince will be clothed with despair,(BA)
    and the hands of the people of the land will tremble.
I will deal with them according to their conduct,(BB)
    and by their own standards I will judge them.

“‘Then they will know that I am the Lord.(BC)’”

Footnotes

  1. Ezekiel 7:5 Most Hebrew manuscripts; some Hebrew manuscripts and Syriac Disaster after
  2. Ezekiel 7:11 Or The violent one has become