Ezekieli 7
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
Chimaliziro Chafika
7 Yehova anandipatsa uthenga uwu kuti, 2 “Iwe mwana wa munthu, Ine Ambuye Yehova ndikuwuza dziko la Israeli kuti:
“Chimaliziro! Chimaliziro chafika
ku ngodya zinayi za dziko.
3 Chimaliziro chili pa iwe tsopano.
Mkwiyo wanga ndidzawuthira pa iwe.
Ndidzakuweruza molingana ndi machitidwe ako
ndi kukulanga chifukwa cha zonyansa zako.
4 Ine sindidzakumvera chisoni
kapena kukuleka.
Ndidzakulanga ndithu chifukwa cha ntchito zako zoyipa
komanso chifukwa cha miyambo yako yonyansa imene ili pakati pako.
Pamenepo udzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”
5 “Zimene ndikunena Ine Ambuye Yehova ndi izi:
“Chiwonongeko! Chiwonongeko chimene sichinamvekepo!
Taona chikubwera!
6 Chimaliziro chafika!
Chimaliziro chafika!
Chiwonongeko chakugwera.
Taona chafika!
7 Inu anthu okhala mʼdziko,
chiwonongeko chakugwerani.
Nthawi yafika, tsiku layandikira; tsiku la chisokonezo osati la chimwemwe pa mapiri.
8 Ine ndili pafupi kukukwiyirani,
ndipo ukali wanga udzathera pa iwe;
Ine ndidzakuweruza molingana ndi machitidwe ako
ndiponso ndidzakulanga chifukwa cha miyambo yako yonyansa.
9 Ine sindidzakumvera chisoni
kapena kukuleka.
Ndidzakulanga malingana ndi ntchito zako
ndiponso chifukwa cha miyambo yako yonyansa pakati pako.
‘Pamenepo udzadziwa kuti Ine Yehova ndine amene ndimakantha.’
10 “Taona, tsikulo!
Taona, lafika!
Chiwonongeko chako chabwera.
Ndodo yaphuka mphundu za maluwa.
Kudzitama kwaphuka.
11 Chiwawa chasanduka ndodo
yowakwapulira chifukwa cha kuyipa kwawo.
Palibe mwa anthu amenewo amene adzatsale.
Palibe ndi mmodzi yemwe mwa unyinji wawo.
Palibiretu ndipo sipadzapezeka
munthu wowalira maliro.
12 Nthawi yafika!
Tsiku layandikira!
Munthu wogula asakondwere
ndipo wogulitsa asamve chisoni,
popeza ukali wanga uli pa gulu lonse.
13 Wogulitsa sadzazipezanso zinthu
zimene anagulitsa kwa wina
chinkana onse awiri akanali ndi moyo,
pakuti chilango chidzagwera onsewo
ndipo sichingasinthike.
Chifukwa cha machimo awo, palibe aliyense
amene adzapulumutsa moyo wake.
14 “Lipenga lalira,
ndipo zonse zakonzeka.
Koma palibe ndi mmodzi yemwe amene akupita ku nkhondo,
pakuti mkwiyo wanga uli pa gulu lonse.
15 Ku bwalo kuli kumenyana
ndipo mʼkati muli mliri ndi njala.
Anthu okhala ku midzi
adzafa ndi nkhondo.
Iwo okhala ku mizinda
adzafa ndi mliri ndi njala.
16 Onse amene adzapulumuka
ndi kumakakhala ku mapiri,
azidzalira ngati nkhunda za ku zigwa.
Aliyense azidzabuwula chifukwa cha machimo ake.
17 Dzanja lililonse lidzalefuka,
ndipo bondo lililonse lidzalobodoka ngati madzi.
18 Iwo adzavala ziguduli
ndipo adzagwidwa ndi mantha.
Adzakhala ndi nkhope zamanyazi
ndipo mitu yawo adzameta mpala.
19 “Iwo adzataya siliva wawo mʼmisewu
ndipo golide wawo adzakhala chinthu chonyansa.
Siliva ndi golide wawo
sizidzatha kuwapulumutsa
pa tsiku la ukali wa Yehova.
Chuma chawochi sichidzawathandiza kuthetsa njala,
kapena kukhala okhuta,
pakuti ndicho chinawagwetsa mʼmachimo.
20 Iwo ankanyadira zodzikongoletsera zawo zamakaka
ndipo ankazigwiritsa ntchito kupanga mafano awo onyansa ndi zonyansa zawo zina.
Nʼchifukwa chake Ine ndidzazisandutsa
kukhala zowanyansa.
21 Ndidzazipereka kwa alendo kuti azifunkhe.
Anthu oyipa a dziko lapansi adzazilanda
ndi kudziyipitsa.
22 Ine ndidzawalekerera anthuwo
ndipo adzayipitsa malo anga apamtima.
Adzalowamo ngati mbala
ndi kuyipitsamo.
23 “Konzani maunyolo,
chifukwa dziko ladzaza ndi anthu opha anzawo
ndipo mzinda wadzaza ndi chiwawa.
24 Ndidzabweretsa mitundu ya anthu oyipitsitsa
kuti idzalande nyumba zawo.
Ndidzathetsa kunyada kwa anthu amphamvu
pamene anthu akunja adzalowa mʼmalo awo achipembedzo ndi kuyipitsamo.
25 Nkhawa ikadzawafikira
adzafunafuna mtendere koma osawupeza.
26 Tsoka lidzatsatana ndi tsoka linzake,
ndipo mphekesera idzatsatana ndi mphekesera inzake.
Iwo adzayesa kufuna masomphenya kuchokera kwa mneneri.
Adzasowa ansembe owaphunzitsa malamulo,
ndipo anthu akuluakulu sadzakhalanso ndi uphungu.
27 Mfumu idzalira,
kalonga adzagwidwa ndi mantha.
Manja a anthu a mʼdzikomo azidzangonjenjemera ndi mantha.
Ine ndidzawalanga molingana ndi machitidwe awo,
ndipo ndidzawaweruza molingana ndi momwe anaweruzira anzawo.
Choncho adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”
Ezekiel 7
New International Version
The End Has Come
7 The word of the Lord came to me: 2 “Son of man, this is what the Sovereign Lord says to the land of Israel:
“‘The end!(A) The end has come
upon the four corners(B) of the land!
3 The end is now upon you,
and I will unleash my anger against you.
I will judge you according to your conduct(C)
and repay you for all your detestable practices.(D)
4 I will not look on you with pity;(E)
I will not spare you.
I will surely repay you for your conduct
and for the detestable practices among you.
“‘Then you will know that I am the Lord.’(F)
5 “This is what the Sovereign Lord says:
“‘Disaster!(G) Unheard-of[a] disaster!
See, it comes!
6 The end(H) has come!
The end has come!
It has roused itself against you.
See, it comes!
7 Doom has come upon you,
upon you who dwell in the land.
The time has come! The day(I) is near!(J)
There is panic, not joy, on the mountains.
8 I am about to pour out my wrath(K) on you
and spend my anger against you.
I will judge you according to your conduct
and repay you for all your detestable practices.(L)
9 I will not look on you with pity;
I will not spare you.(M)
I will repay you for your conduct
and for the detestable practices among you.(N)
“‘Then you will know that it is I the Lord who strikes you.(O)
10 “‘See, the day!
See, it comes!
Doom has burst forth,
the rod(P) has budded,
arrogance has blossomed!
11 Violence(Q) has arisen,[b]
a rod to punish the wicked.
None of the people will be left,
none of that crowd—
none of their wealth,
nothing of value.(R)
12 The time has come!
The day has arrived!
Let not the buyer(S) rejoice
nor the seller grieve,
for my wrath is on the whole crowd.(T)
13 The seller will not recover
the property that was sold—
as long as both buyer and seller live.
For the vision concerning the whole crowd
will not be reversed.
Because of their sins, not one of them
will preserve their life.(U)
14 “‘They have blown the trumpet,(V)
they have made all things ready,
but no one will go into battle,
for my wrath(W) is on the whole crowd.
15 Outside is the sword;
inside are plague and famine.
Those in the country
will die by the sword;
those in the city
will be devoured by famine and plague.(X)
16 The fugitives(Y) who escape
will flee to the mountains.
Like doves(Z) of the valleys,
they will all moan,
each for their own sins.(AA)
17 Every hand will go limp;(AB)
every leg will be wet with urine.(AC)
18 They will put on sackcloth(AD)
and be clothed with terror.(AE)
Every face will be covered with shame,
and every head will be shaved.(AF)
19 “‘They will throw their silver into the streets,(AG)
and their gold will be treated as a thing unclean.
Their silver and gold
will not be able to deliver them
in the day of the Lord’s wrath.(AH)
It will not satisfy(AI) their hunger
or fill their stomachs,
for it has caused them to stumble(AJ) into sin.(AK)
20 They took pride in their beautiful jewelry
and used it to make(AL) their detestable idols.
They made it into vile images;(AM)
therefore I will make it a thing unclean for them.(AN)
21 I will give their wealth as plunder(AO) to foreigners
and as loot to the wicked of the earth,
who will defile it.(AP)
22 I will turn my face(AQ) away from the people,
and robbers will desecrate the place I treasure.
They will enter it
and will defile it.(AR)
23 “‘Prepare chains!
For the land is full of bloodshed,(AS)
and the city is full of violence.(AT)
24 I will bring the most wicked of nations
to take possession of their houses.
I will put an end to the pride of the mighty,
and their sanctuaries(AU) will be desecrated.(AV)
25 When terror comes,
they will seek peace in vain.(AW)
26 Calamity upon calamity(AX) will come,
and rumor upon rumor.
They will go searching for a vision from the prophet,(AY)
priestly instruction in the law will cease,
the counsel of the elders will come to an end.(AZ)
27 The king will mourn,
the prince will be clothed with despair,(BA)
and the hands of the people of the land will tremble.
I will deal with them according to their conduct,(BB)
and by their own standards I will judge them.
“‘Then they will know that I am the Lord.(BC)’”
Footnotes
- Ezekiel 7:5 Most Hebrew manuscripts; some Hebrew manuscripts and Syriac Disaster after
- Ezekiel 7:11 Or The violent one has become
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.
Holy Bible, New International Version®, NIV® Copyright ©1973, 1978, 1984, 2011 by Biblica, Inc.® Used by permission. All rights reserved worldwide.
NIV Reverse Interlinear Bible: English to Hebrew and English to Greek. Copyright © 2019 by Zondervan.