Add parallel Print Page Options

Yakobo Apita ku Igupto

46 Israeli anasonkhanitsa zonse anali nazo napita ku Beeriseba kukapereka nsembe kwa Mulungu wa abambo ake Isake.

Ndipo Mulungu anayankhula ndi Israeli mʼmasomphenya usiku nati, “Yakobo! Yakobo!”

Iye anayankha, “Ee, Ambuye.”

Mulungu anati, “Ine ndine Mulungu. Mulungu wa abambo ako. Usachite mantha kupita ku Igupto, pakuti ndidzachulukitsa zidzukulu zako kumeneko moti zidzakhala mtundu waukulu. Ine ndidzapita ku Igupto pamodzi ndi iwe ndipo mosakayika konse zidzukulu zako ndidzazibweretsa konkuno. Yosefe adzakhalapo pa nthawi yako yomwalira.”

Yakobo anachoka ku Beeriseba, ndipo ana ake anakweza abambo awo, ana awo, pamodzi ndi akazi awo pa ngolo zimene Farao anatumiza kuti adzakwerepo. Iwo anatenganso ziweto zawo ndi katundu wawo amene anali naye ku Kanaani, ndipo Yakobo pamodzi ndi ana ndi zidzukulu zake anapita ku Igupto. Ndiye kuti popita ku Igupto Yakobo anatenga ana aamuna, zidzukulu zazimuna, ana aakazi ndi zidzukulu zazikazi.

Nawa ana a Israeli (ndiye kuti Yakobo ndi ana ake) amene anapita ku Igupto:

Rubeni mwana woyamba wa Yakobo.

Ana aamuna a Rubeni ndi awa:

Hanoki, Palu, Hezironi ndi Karimi.

10 Ana aamuna a Simeoni ndi awa:

Yemueli, Yamini, Ohadi, Yakini, Zohari ndi Shaulo amene mayi wake anali wa ku Kanaani.

11 Ana aamuna a Levi ndi awa:

Geresoni, Kohati ndi Merari.

12 Ana aamuna a Yuda ndi awa:

Eri, Onani, Sela, Perezi ndi Zera. Koma Eri ndi Onani anamwalira mʼdziko la Kanaani.

Ana a Perezi anali

Hezironi ndi Hamuli.

13 Ana aamuna a Isakara ndi awa:

Tola, Puwa, Yobi ndi Simironi.

14 Ana aamuna a Zebuloni ndi awa:

Seredi, Eloni ndi Yahaleeli.

15 Amenewa ndi ana aamuna a Leya amene anamubalira Yakobo ku Padanaramu. Panali mwana wamkazi dzina lake Dina. Ana onse analipo 33.

16 Ana aamuna a Gadi ndi awa:

Zifioni, Hagi, Suni, Eziboni, Eri, Arodi ndi Areli.

17 Ana aamuna a Aseri ndi awa:

Imuna, Isiva, Isivi, Beriya

ndi Sera mlongo wawo.

Ana aamuna a Beriya ndi awa:

Heberi ndi Malikieli.

18 Amenewa ndi zidzukulu za Yakobo mwa Zilipa amene Labani anapereka kwa mwana wake, Leya. Onse pamodzi analipo 16.

19 Ana aamuna a Rakele mkazi wa Yakobo anali:

Yosefe ndi Benjamini. 20 Ku Igupto, Asenati mwana wa Potifara wansembe wa Oni, anamuberekera Yosefe ana awa: Manase ndi Efereimu.

21 Ana aamuna a Benjamini ndi awa:

Bela, Bekeri, Asibeli, Gera, Naamani, Ehi, Rosi, Mupimu, Hupimu ndi Aridi.

22 Amenewa ndi zidzukulu za Yakobo mwa mkazi wake Rakele. Onse analipo khumi ndi anayi.

23 Mwana wa mwamuna wa Dani anali:

Husimu.

24 Ana aamuna a Nafutali ndi awa:

Yahazeeli, Guni, Yezeri ndi Silemu.

25 Amenewa ndi zidzukulu za Yakobo mwa Biliha amene Labani anapereka kwa mwana wake Rakele. Onse pamodzi analipo asanu ndi awiri.

26 Onse amene anapita ndi Yakobo (iwo amene anali akeake, osawerengera akazi a ana ake), analipo 66. 27 Pophatikiza ana awiri a Yosefe obadwira ku Igupto, anthu a pa banja la Yakobo amene anapita ku Igupto, onse pamodzi analipo 70.

28 Tsopano Yakobo anatumiza Yuda kwa Yosefe kukamupempha kuti akakumane naye ku Goseni. Iwo atafika ku chigawo cha Goseni, 29 Yosefe anakonza galeta nakwerapo ndi kupita ku Goseni kukakumana ndi abambo ake, Israeli. Yosefe atangofika pamaso pa abambo ake, anawakumbatira nalira kwa nthawi yayitali.

30 Israeli anati kwa Yosefe, “Tsopano ndikhoza kumwalira poti ndaona nkhope yako kuti ukanali ndi moyo.”

31 Ndipo Yosefe anati kwa abale ake pamodzi ndi a pa banja la abambo ake, “Ndipita kwa Farao ndipo ndikamuwuza kuti, ‘Abale anga pamodzi ndi onse a mʼnyumba ya abambo anga amene amakhala mʼdziko la Kanaani abwera kuno kwa ine. 32 Anthuwa ndi abusa; amaweta ziweto zawo ndipo abwera ndi nkhosa ndi ngʼombe zawo, pamodzi ndi antchito awo.’ 33 Tsono Farao akakuyitanani nakufunsani kuti, ‘Kodi mumagwira ntchito yanji?’ 34 Muyankhe kuti, ‘Ife, bwana ndife oweta ziweto kuyambira ubwana wathu mpaka tsopano. Takhala tikuweta ziweto monga mmene ankachitira makolo athu.’ Mukadzayankha choncho, ndiye kuti mudzakhala mʼdziko la Goseni chifukwa anthu a ku Igupto amanyansidwa nawo anthu oweta ziweto.”

Jacob Goes to Egypt

46 So Israel(A) set out with all that was his, and when he reached Beersheba,(B) he offered sacrifices(C) to the God of his father Isaac.(D)

And God spoke to Israel(E) in a vision at night(F) and said, “Jacob! Jacob!”

“Here I am,”(G) he replied.

“I am God, the God of your father,”(H) he said. “Do not be afraid(I) to go down to Egypt,(J) for I will make you into a great nation(K) there.(L) I will go down to Egypt with you, and I will surely bring you back again.(M) And Joseph’s own hand will close your eyes.(N)

Then Jacob left Beersheba,(O) and Israel’s(P) sons took their father Jacob and their children and their wives in the carts(Q) that Pharaoh had sent to transport him. So Jacob and all his offspring went to Egypt,(R) taking with them their livestock and the possessions(S) they had acquired(T) in Canaan. Jacob brought with him to Egypt(U) his sons and grandsons and his daughters and granddaughters—all his offspring.(V)

These are the names of the sons of Israel(W) (Jacob and his descendants) who went to Egypt:

Reuben the firstborn(X) of Jacob.

The sons of Reuben:(Y)

Hanok, Pallu,(Z) Hezron and Karmi.(AA)

10 The sons of Simeon:(AB)

Jemuel,(AC) Jamin, Ohad, Jakin, Zohar(AD) and Shaul the son of a Canaanite woman.

11 The sons of Levi:(AE)

Gershon,(AF) Kohath(AG) and Merari.(AH)

12 The sons of Judah:(AI)

Er,(AJ) Onan,(AK) Shelah, Perez(AL) and Zerah(AM) (but Er and Onan had died in the land of Canaan).(AN)

The sons of Perez:(AO)

Hezron and Hamul.(AP)

13 The sons of Issachar:(AQ)

Tola, Puah,[a](AR) Jashub[b](AS) and Shimron.

14 The sons of Zebulun:(AT)

Sered, Elon and Jahleel.

15 These were the sons Leah bore to Jacob in Paddan Aram,[c](AU) besides his daughter Dinah.(AV) These sons and daughters of his were thirty-three in all.

16 The sons of Gad:(AW)

Zephon,[d](AX) Haggi, Shuni, Ezbon, Eri, Arodi and Areli.

17 The sons of Asher:(AY)

Imnah, Ishvah, Ishvi and Beriah.

Their sister was Serah.

The sons of Beriah:

Heber and Malkiel.

18 These were the children born to Jacob by Zilpah,(AZ) whom Laban had given to his daughter Leah(BA)—sixteen in all.

19 The sons of Jacob’s wife Rachel:(BB)

Joseph and Benjamin.(BC) 20 In Egypt, Manasseh(BD) and Ephraim(BE) were born to Joseph(BF) by Asenath daughter of Potiphera, priest of On.[e](BG)

21 The sons of Benjamin:(BH)

Bela, Beker, Ashbel, Gera, Naaman, Ehi, Rosh, Muppim, Huppim and Ard.(BI)

22 These were the sons of Rachel(BJ) who were born to Jacob—fourteen in all.

23 The son of Dan:(BK)

Hushim.(BL)

24 The sons of Naphtali:(BM)

Jahziel, Guni, Jezer and Shillem.

25 These were the sons born to Jacob by Bilhah,(BN) whom Laban had given to his daughter Rachel(BO)—seven in all.

26 All those who went to Egypt with Jacob—those who were his direct descendants, not counting his sons’ wives—numbered sixty-six persons.(BP) 27 With the two sons[f] who had been born to Joseph in Egypt,(BQ) the members of Jacob’s family, which went to Egypt, were seventy[g] in all.(BR)

28 Now Jacob sent Judah(BS) ahead of him to Joseph to get directions to Goshen.(BT) When they arrived in the region of Goshen, 29 Joseph had his chariot(BU) made ready and went to Goshen to meet his father Israel.(BV) As soon as Joseph appeared before him, he threw his arms around his father[h] and wept(BW) for a long time.(BX)

30 Israel(BY) said to Joseph, “Now I am ready to die, since I have seen for myself that you are still alive.”(BZ)

31 Then Joseph said to his brothers and to his father’s household, “I will go up and speak to Pharaoh and will say to him, ‘My brothers and my father’s household, who were living in the land of Canaan,(CA) have come to me.(CB) 32 The men are shepherds;(CC) they tend livestock,(CD) and they have brought along their flocks and herds and everything they own.’(CE) 33 When Pharaoh calls you in and asks, ‘What is your occupation?’(CF) 34 you should answer, ‘Your servants(CG) have tended livestock from our boyhood on, just as our fathers did.’(CH) Then you will be allowed to settle(CI) in the region of Goshen,(CJ) for all shepherds are detestable to the Egyptians.(CK)

Footnotes

  1. Genesis 46:13 Samaritan Pentateuch and Syriac (see also 1 Chron. 7:1); Masoretic Text Puvah
  2. Genesis 46:13 Samaritan Pentateuch and some Septuagint manuscripts (see also Num. 26:24 and 1 Chron. 7:1); Masoretic Text Iob
  3. Genesis 46:15 That is, Northwest Mesopotamia
  4. Genesis 46:16 Samaritan Pentateuch and Septuagint (see also Num. 26:15); Masoretic Text Ziphion
  5. Genesis 46:20 That is, Heliopolis
  6. Genesis 46:27 Hebrew; Septuagint the nine children
  7. Genesis 46:27 Hebrew (see also Exodus 1:5 and note); Septuagint (see also Acts 7:14) seventy-five
  8. Genesis 46:29 Hebrew around him