Add parallel Print Page Options

Chakudya Choyeretsedwa ndi Chodetsedwa

11 Yehova anayankhula ndi Mose ndi Aaroni kuti, “Awuze Aisraeli kuti, ‘Nyama zomwe mukhoza kudya mwa nyama zonse za dziko lapansi ndi izi: Nyama iliyonse imene ili ndi chipondero chogawikana pakati ndi yobzikula mukhoza kudya.

“ ‘Koma pali nyama zina zimene zimabzikula kokha kapena ndi zogawikana zipondero zimene simukuyenera kudya. Nyama zimenezi ndi ngamira, ngakhale imabzikula ilibe zipondero zogawikana. Choncho ndi yodetsedwa, musadye. Ina ndi mbira, ngakhale imabzikula, zipondero zake nʼzosagawikana. Choncho ndi yodetsedwa, musadye. Inanso ndi kalulu, ngakhale amabzikula, zipondero zake nʼzosagawikana. Choncho ndi wodetsedwa, musadye. Nkhumba simabzikula ngakhale ili ndi zipondero zogawikana. Choncho ndi yodetsedwa, musadye. Musamadye nyama yake kapena kukhudza imene yafa chifukwa ndi yodetsedwa.

“ ‘Mwa zamoyo zonse zimene zimakhala mʼmadzi a mʼnyanja ndi a mʼmitsinje mukhoza kudya chilichonse chimene chili ndi minga ya pa msana ndi mamba. 10 Koma zamoyo zonse za mʼnyanja kapena za mʼmitsinje zimene zilibe minga ya pa msana ndi mamba, kaya ndi tizirombo tonse ta mʼmadzi ndi zamoyo zonse zopezeka mʼmenemo ndi zodetsedwa kwa inu. 11 Pakuti zimenezi ndi zodetsedwa kwa inu, nyama yake musadye, ndipo zikafa zikhalebe zodetsedwa kwa inu. 12 Chamoyo chilichonse cha mʼmadzi chimene chilibe minga ya pa msana kapena mamba ndi chodetsedwa kwa inu.

13 “ ‘Mbalame zimene simukuyenera kudya chifukwa ndi zodetsedwa ndi izi: mphungu, nkhwazi, mwimba, 14 nankapakapa, akamtema a mitundu yonse, 15 akhungubwi a mitundu yonse, 16 kadzidzi wamphondo, kadzidzi wodzuma, chipudo ndi mtundu uliwonse wa akabawi 17 kadzidzi wamngʼono, chiswankhono ndi mantchichi, 18 tsekwe, vuwo, dembo, 19 indwa, zimeza za mitundu yonse, nsadzu ndi mleme.

20 “ ‘Zowuluka zonse za miyendo inayi ndi zodetsedwa. 21 Komabe mwa zowuluka zokhala ndi miyendo inayi zimene mukhoza kudya ndi zokhazo zimene zili ndi miyendo yolumphira. 22 Pa zimenezo mungathe kudya izi: dzombe la mitundu yonse, atsokonombwe a mitundu yonse, nkhululu za mitundu yonse, ndi ziwala za mitundu yonse. 23 Koma za mapiko zina zonse zokhala ndi miyendo inayi muzitenge kukhala zodetsedwa kwa inu.

24 “ ‘Zimenezi zidzakudetsani. Aliyense wozikhudza zitafa adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo. 25 Aliyense wonyamula chiwalo chilichonse cha nyama zakufazo ayenera kuchapa zovala zake, ndipo adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo.

26 “ ‘Nyama iliyonse imene ili ndi ziboda zogawikana koma mapazi ake wosagawikana, kapena imene sibzikula muyiyese yodetsedwa kwa inu ndipo munthu aliyense akakhudza nyama yakufayo, adzakhala wodetsedwa. 27 Mwa nyama zonse zoyenda ndi miyendo inayi, nyama zonse zokhala ndi zikhadabo kuphazi muzitenge kukhala zodetsedwa ndipo aliyense wozikhudza zitafa adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo. 28 Aliyense wonyamula nyamazi zitafa ayenera kuchapa zovala zake, ndipo adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo. Zimenezi ndi zodetsedwa kwa inu.

29 “ ‘Mwa nyama zokwawa, zimene zili zodetsedwa kwa inu ndi izi: likongwe, mbewa, msambulu za mitundu yonse, 30 gondwa, mngʼazi, buluzi, dududu ndi nanzikambe. 31 Mwa nyama zonse zoyenda pansi, zimenezi ndi zodetsedwa kwa inu. Munthu aliyense wozikhudza zitafa adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo. 32 Iliyonse mwa nyama zimenezi ikafa ndi kugwera pa chiwiya chilichonse, kaya chimagwira ntchito yotani, kaya ndi chopangidwa ndi mtengo, kaya ndi cha nsalu, kaya ndi cha chikopa kapena chiguduli chiwiyacho chidzakhala chodetsedwa. Muchiviyike mʼmadzi chiwiyacho komabe chidzakhala chodetsedwa mpaka madzulo, ndipo kenaka chidzakhala choyeretsedwa. 33 Tsono nyama ina iliyonse mwa zimenezi ikagwera mʼmbiya ya dothi, ndiye kuti chilichonse cha mʼmbiyamo chidzakhala chodetsedwa, ndipo muyenera kuswa mbiyayo. 34 Chakudya chilichonse chimene mungadye chikakhala kuti chathiridwa mʼmbiyamo, ndiye kuti chakudyacho chidzakhala chodetsedwa, ndipo madzi akumwa wochokera mʼmbiya zotere ndi wodetsedwa. 35 Chiwalo chilichonse cha nyama yakufa chikagwera pa chinthu chilichonse kaya pa uvuni, kapena pa mʼphika, ndiye kuti zinthuzo zidzakhala zodetsedwa, ndipo ziphwanyidwe popeza ndi zodetsedwa. 36 Koma kasupe kapena chitsime chamadzi chidzakhala choyeretsedwa ngakhale kuti chilichonse chokhudza nyama yakufayo chidzakhala chodetsedwa. Zimenezi muzitenge kukhala zodetsedwa. 37 Chiwalo chilichonse cha nyama yakufayo chikagwera pa mbewu zimene akuti adzale, mbewu zimenezo zidzakhalabe zabwino. 38 Koma mbewuzo zikakhala zonyowa ndi madzi, ndipo chiwalo chilichonse cha nyama zakufazo chikagwera pa mbewuzo, mbewuzo zikhale zodetsedwa kwa inu.

39 “ ‘Ngati nyama imene mumaloledwa kudya yafa yokha, ndiye kuti aliyense wokhudza nyama yakufayo adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo. 40 Aliyense amene adyako nyama yakufayo achape zovala zake, ndipo adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo. Aliyense amene wanyamula nyama yakufayo ayenera kuchapa zovala zake, ndipo adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo.

41 “ ‘Chinthu chilichonse chokwawa pansi ndi chonyansa, simuyenera kudya. 42 Musadye chilichonse chokwawa pansi, choyenda chamimba kapena choyenda ndi miyendo inayi kapenanso yambiri popeza ndi chodetsedwa. 43 Musadzisandutse nokha odetsedwa ndi chokwawa chilichonse. Musadziyipitse nazo, kuti mukhale odetsedwa. 44 Ine ndine Yehova Mulungu wanu, choncho dziyeretseni kuti mukhale woyera, chifukwa Ine ndine woyera. Musadzisandutse odetsedwa ndi chokwawa chilichonse. 45 Ine ndine Yehova amene ndinakutulutsani ku Igupto kuti ndikhale Mulungu wanu. Tsono mukhale woyera, chifukwa Ine ndine woyera.

46 “ ‘Amenewa ndi malamulo onena za nyama, mbalame, chamoyo chilichonse choyenda mʼmadzi ndiponso chamoyo chilichonse chokwawa. 47 Muzisiyanitsa pakati pa chodetsedwa ndi choyeretsedwa, komanso pakati pa zomwe mutha kudya ndi zomwe simuyenera kudya.’ ”

Clean and Unclean Food(A)

11 The Lord said to Moses and Aaron, “Say to the Israelites: ‘Of all the animals that live on land, these are the ones you may eat:(B) You may eat any animal that has a divided hoof and that chews the cud.

“‘There are some that only chew the cud or only have a divided hoof, but you must not eat them.(C) The camel, though it chews the cud, does not have a divided hoof; it is ceremonially unclean for you. The hyrax, though it chews the cud, does not have a divided hoof; it is unclean for you. The rabbit, though it chews the cud, does not have a divided hoof; it is unclean for you. And the pig,(D) though it has a divided hoof, does not chew the cud; it is unclean for you. You must not eat their meat or touch their carcasses; they are unclean for you.(E)

“‘Of all the creatures living in the water of the seas and the streams you may eat any that have fins and scales. 10 But all creatures in the seas or streams that do not have fins and scales—whether among all the swarming things or among all the other living creatures in the water—you are to regard as unclean.(F) 11 And since you are to regard them as unclean, you must not eat their meat; you must regard their carcasses as unclean.(G) 12 Anything living in the water that does not have fins and scales is to be regarded as unclean by you.(H)

13 “‘These are the birds you are to regard as unclean and not eat because they are unclean: the eagle,[a] the vulture, the black vulture, 14 the red kite, any kind(I) of black kite, 15 any kind of raven,(J) 16 the horned owl, the screech owl, the gull, any kind of hawk, 17 the little owl, the cormorant, the great owl, 18 the white owl,(K) the desert owl, the osprey, 19 the stork,(L) any kind(M) of heron, the hoopoe and the bat.(N)

20 “‘All flying insects that walk on all fours are to be regarded as unclean by you.(O) 21 There are, however, some flying insects that walk on all fours that you may eat: those that have jointed legs for hopping on the ground. 22 Of these you may eat any kind of locust,(P) katydid, cricket or grasshopper. 23 But all other flying insects that have four legs you are to regard as unclean.

24 “‘You will make yourselves unclean by these;(Q) whoever touches their carcasses will be unclean till evening.(R) 25 Whoever picks up one of their carcasses must wash their clothes,(S) and they will be unclean till evening.(T)

26 “‘Every animal that does not have a divided hoof or that does not chew the cud is unclean for you; whoever touches the carcass of any of them will be unclean. 27 Of all the animals that walk on all fours, those that walk on their paws are unclean for you; whoever touches their carcasses will be unclean till evening. 28 Anyone who picks up their carcasses must wash their clothes, and they will be unclean till evening.(U) These animals are unclean for you.

29 “‘Of the animals that move along the ground, these are unclean for you:(V) the weasel, the rat,(W) any kind of great lizard, 30 the gecko, the monitor lizard, the wall lizard, the skink and the chameleon. 31 Of all those that move along the ground, these are unclean for you. Whoever touches them when they are dead will be unclean till evening. 32 When one of them dies and falls on something, that article, whatever its use, will be unclean, whether it is made of wood, cloth, hide or sackcloth.(X) Put it in water; it will be unclean till evening, and then it will be clean. 33 If one of them falls into a clay pot, everything in it will be unclean, and you must break the pot.(Y) 34 Any food you are allowed to eat that has come into contact with water from any such pot is unclean, and any liquid that is drunk from such a pot is unclean. 35 Anything that one of their carcasses falls on becomes unclean; an oven or cooking pot must be broken up. They are unclean, and you are to regard them as unclean. 36 A spring, however, or a cistern for collecting water remains clean, but anyone who touches one of these carcasses is unclean. 37 If a carcass falls on any seeds that are to be planted, they remain clean. 38 But if water has been put on the seed and a carcass falls on it, it is unclean for you.

39 “‘If an animal that you are allowed to eat dies,(Z) anyone who touches its carcass(AA) will be unclean till evening. 40 Anyone who eats some of its carcass(AB) must wash their clothes, and they will be unclean till evening.(AC) Anyone who picks up the carcass must wash their clothes, and they will be unclean till evening.

41 “‘Every creature that moves along the ground is to be regarded as unclean; it is not to be eaten. 42 You are not to eat any creature that moves along the ground, whether it moves on its belly or walks on all fours or on many feet; it is unclean. 43 Do not defile yourselves by any of these creatures.(AD) Do not make yourselves unclean by means of them or be made unclean by them. 44 I am the Lord your God;(AE) consecrate yourselves(AF) and be holy,(AG) because I am holy.(AH) Do not make yourselves unclean by any creature that moves along the ground.(AI) 45 I am the Lord, who brought you up out of Egypt(AJ) to be your God;(AK) therefore be holy, because I am holy.(AL)

46 “‘These are the regulations concerning animals, birds, every living thing that moves about in the water and every creature that moves along the ground. 47 You must distinguish between the unclean and the clean, between living creatures that may be eaten and those that may not be eaten.(AM)’”

Footnotes

  1. Leviticus 11:13 The precise identification of some of the birds, insects and animals in this chapter is uncertain.