Add parallel Print Page Options

Lonjezo la Mzimu Woyera

Mʼbuku langa loyamba, ndinakulembera iwe Teofilo zonse zimene Yesu anayamba kuchita ndi kuphunzitsa, mpaka tsiku limene anatengedwa kupita kumwamba, mwamphamvu ya Mzimu Woyera, atawalangiza atumwi amene anawasankha. Zitatha zowawa zake Yesu anadzionetsa kwa ophunzira ake, ndi kuonetsanso maumboni ambiri kuti anali wamoyo. Iye anadzionetsera kwa iwo ndi kuwaphunzitsa za ufumu wa Mulungu pa masiku makumi anayi. Nthawi ina atasonkhana nawo pamodzi, Yesu analamulira ophunzira ake kuti, “Musachoke mu Yerusalemu, koma mudikire mphatso imene Atate anga analonjeza yomwe ndinakuwuzani. Pakuti Yohane anakubatizani ndi madzi, koma posachedwapa inu mudzabatizidwa ndi Mzimu Woyera.”

Yesu Akwera Kumwamba

Atumwi atasonkhana pamodzi, iwo anamufunsa Iye kuti, “Ambuye, kodi nthawi ino mubwezeretsa ufumu kwa Israeli?”

Yesu anawawuza kuti, “Sikofunika kuti mudziwe za nthawi kapena masiku amene Atate ayika mwa ulamuliro wawo. Koma mudzalandira mphamvu Mzimu Woyera akadzafika pa inu; ndipo mudzakhala mboni zanga mu Yerusalemu, ku Yudeya konse ndi ku Samariya, mpaka ku malekezero a dziko lapansi.”

Atatha kuyankhula zimenezi, Yesu anatengedwa kupita kumwamba ophunzira ake akuona, ndipo anabisika mʼmitambo.

10 Yesu akukwera kumwamba, ophunzira ake anayangʼanitsitsa ndi chidwi mʼmitambo. Mwadzidzidzi anaona anthu awiri ovala zoyera atayimirira pambali pawo. 11 Iwo anati, “Inu, anthu a ku Galileya, chifukwa chiyani mukuyima ndi kumayangʼana mʼmitambo? Yesu amene wachotsedwa pakati panu ndi kupita kumwamba, adzabweranso mʼnjira yomweyi mwamuona akupita kumwamba.”

Matiyasi Alowa Mʼmalo mwa Yudasi Isikarioti

12 Pamenepo atumwi anabwerera ku Yerusalemu kuchokera ku phiri la Olivi, mtunda wosakwana kilomita kuchokera mu mzindamo. 13 Atafika mu mzindamo, analowa mʼchipinda chammwamba kumene amakhala. Amene analipo anali awa: Petro, Yohane, Yakobo ndi Andreya; Filipo ndi Tomasi, Bartumeyu ndi Mateyu; Yakobo mwana wa Alifeyo ndi Simoni Zelote ndi Yuda mwana wa Yakobo. 14 Onsewa ndi mtima umodzi anapitiriza kupemphera pamodzi ndi amayi, ndi Mariya amayi ake a Yesu, ndiponso abale ake a Yesu.

15 Pa nthawi imeneyo Petro anayimirira pakati pa okhulupirira (gulu la anthu pafupifupi 120). 16 Iye anati, “Abale anga, Malemba anayenera kukwaniritsidwa omwe Mzimu Woyera anayankhula kalekale kudzera mwa Davide za Yudasi, amene anatsogolera amene anamugwira Yesu. 17 Iye anali mmodzi wa gulu lathu ndipo anatumikira pamodzi ndi ife.”

18 (Yudasi anagula munda ndi ndalama zimene anazipeza pochita zoyipa zija; kumeneko, iye anagwa chamutu, naphulika pakati ndipo matumbo ake wonse anakhuthuka. 19 Aliyense mu Yerusalemu anamva zimenezi, kotero anatcha mundawo mʼchiyankhulo chawo kuti Akeledama, kutanthauza, Munda wa Magazi).

20 Petro anati, “Pakuti kwalembedwa mʼbuku la Masalimo kuti,

“Nyumba yake isanduke bwinja,
    ndipo pasakhale wogonamo.

Ndiponso,

“Wina atenge ntchito yake yautsogoleri.

21 Chifukwa chake ndi kofunika kusankha mmodzi wa anthu amene akhala nafe nthawi yonse imene Ambuye Yesu ankayenda nafe, 22 kuyambira pa nthawi ya ubatizo wa Yohane mpaka nthawi imene Yesu anatengedwa pakati pathu. Pakuti mmodzi wa anthu awa ayenera kukhala mboni pamodzi ndi ife zakuuka kwake.”

23 Pamenepo anasankha anthu awiri, Yosefe wotchedwa Barsaba (wodziwikanso kuti Yusto) ndi Matiyasi. 24 Kenaka iwo anapemphera nati, “Ambuye mukudziwa mtima wa aliyense. Tionetseni amene mwamusankha mwa awiri awa 25 kuti atenge ntchito iyi ya utumwi, imene Yudasi anasiya napita kumalo womuyenera.” 26 Tsono anachita maere, ndipo maerewo anagwera Matiyasi. Tsono iye anawonjezedwa pa gulu la atumwi khumi ndi mmodziwo.

Jesus Taken Up Into Heaven

In my former book,(A) Theophilus, I wrote about all that Jesus began to do and to teach(B) until the day he was taken up to heaven,(C) after giving instructions(D) through the Holy Spirit to the apostles(E) he had chosen.(F) After his suffering, he presented himself to them and gave many convincing proofs that he was alive. He appeared to them(G) over a period of forty days and spoke about the kingdom of God.(H) On one occasion, while he was eating with them, he gave them this command: “Do not leave Jerusalem, but wait(I) for the gift my Father promised, which you have heard me speak about.(J) For John baptized with[a] water,(K) but in a few days you will be baptized with[b] the Holy Spirit.”(L)

Then they gathered around him and asked him, “Lord, are you at this time going to restore(M) the kingdom to Israel?”

He said to them: “It is not for you to know the times or dates the Father has set by his own authority.(N) But you will receive power when the Holy Spirit comes on you;(O) and you will be my witnesses(P) in Jerusalem, and in all Judea and Samaria,(Q) and to the ends of the earth.”(R)

After he said this, he was taken up(S) before their very eyes, and a cloud hid him from their sight.

10 They were looking intently up into the sky as he was going, when suddenly two men dressed in white(T) stood beside them. 11 “Men of Galilee,”(U) they said, “why do you stand here looking into the sky? This same Jesus, who has been taken from you into heaven, will come back(V) in the same way you have seen him go into heaven.”

Matthias Chosen to Replace Judas

12 Then the apostles returned to Jerusalem(W) from the hill called the Mount of Olives,(X) a Sabbath day’s walk[c] from the city. 13 When they arrived, they went upstairs to the room(Y) where they were staying. Those present were Peter, John, James and Andrew; Philip and Thomas, Bartholomew and Matthew; James son of Alphaeus and Simon the Zealot, and Judas son of James.(Z) 14 They all joined together constantly in prayer,(AA) along with the women(AB) and Mary the mother of Jesus, and with his brothers.(AC)

15 In those days Peter stood up among the believers (a group numbering about a hundred and twenty) 16 and said, “Brothers and sisters,[d](AD) the Scripture had to be fulfilled(AE) in which the Holy Spirit spoke long ago through David concerning Judas,(AF) who served as guide for those who arrested Jesus. 17 He was one of our number(AG) and shared in our ministry.”(AH)

18 (With the payment(AI) he received for his wickedness, Judas bought a field;(AJ) there he fell headlong, his body burst open and all his intestines spilled out. 19 Everyone in Jerusalem heard about this, so they called that field in their language(AK) Akeldama, that is, Field of Blood.)

20 “For,” said Peter, “it is written in the Book of Psalms:

“‘May his place be deserted;
    let there be no one to dwell in it,’[e](AL)

and,

“‘May another take his place of leadership.’[f](AM)

21 Therefore it is necessary to choose one of the men who have been with us the whole time the Lord Jesus was living among us, 22 beginning from John’s baptism(AN) to the time when Jesus was taken up from us. For one of these must become a witness(AO) with us of his resurrection.”

23 So they nominated two men: Joseph called Barsabbas (also known as Justus) and Matthias. 24 Then they prayed,(AP) “Lord, you know everyone’s heart.(AQ) Show us(AR) which of these two you have chosen 25 to take over this apostolic ministry, which Judas left to go where he belongs.” 26 Then they cast lots, and the lot fell to Matthias; so he was added to the eleven apostles.(AS)

Footnotes

  1. Acts 1:5 Or in
  2. Acts 1:5 Or in
  3. Acts 1:12 That is, about 5/8 mile or about 1 kilometer
  4. Acts 1:16 The Greek word for brothers and sisters (adelphoi) refers here to believers, both men and women, as part of God’s family; also in 6:3; 11:29; 12:17; 16:40; 18:18, 27; 21:7, 17; 28:14, 15.
  5. Acts 1:20 Psalm 69:25
  6. Acts 1:20 Psalm 109:8