Add parallel Print Page Options

Timoteyo Atsagana ndi Paulo ndi Sila

16 Paulo anafika ku Derbe ndi Lusitra, kumene kumakhala ophunzira wina dzina lake Timoteyo. Amayi ake anali Myuda wokhulupirira, koma abambo ake anali Mgriki. Abale a ku Lusitra ndi Ikoniya anamuchitira iye umboni wabwino. Paulo anafuna kumutenga pa ulendo, kotero anachita mdulidwe chifukwa cha Ayuda amene amakhala mʼderalo pakuti onse amadziwa kuti abambo ake anali Mgriki. Pamene amayenda mzinda ndi mzinda, amafotokoza zimene atumwi ndi akulu ampingo ku Yerusalemu anagwirizana kuti anthu azitsatire. Kotero mipingo inalimbikitsidwa mʼchikhulupiriro ndipo anthu amachulukirachulukirabe tsiku ndi tsiku.

Paulo Awona Masomphenya

Paulo ndi anzake anadutsa mayiko a Frugiya ndi Galatiya, Mzimu Woyera atawaletsa kulalikira Mawu a Mulungu ku Asiya. Atafika ku malire a Musiya, anayesa kulowa ku Bituniya, koma Mzimu wa Yesu sunawalole kutero. Ndipo iwo anadutsa Musiya ndipo anapita ku Trowa. Nthawi ya usiku Paulo anaona masomphenya, munthu wa ku Makedoniya atayimirira ndi kumupempha kuti, “Bwerani ku Makedoniya, mudzatithandize.” 10 Paulo ataona masomphenyawa, tinakonzeka kupita ku Makedoniya, kutsimikiza kuti Mulungu anatiyitana kuti tikalalikire Uthenga Wabwino.

Lidia Atembenuka Mtima ku Filipi

11 Kuchokera ku Trowa tinakwera sitima ya pamadzi kupita ku Samotrake ndipo mmawa mwake tinapitirira mpaka ku Neapoli. 12 Kuchokera kumeneko tinapita ku Filipi, boma la Aroma ndiponso mzinda waukulu wa dera la Makedoniya. Tinakhala kumeneko masiku owerengeka.

13 Pa tsiku la Sabata tinatuluka mu mzindawo kupita ku mtsinje kumene timayembekezera kukapeza malo opempherera. Tinakhala pansi ndipo tinayamba kuyankhula ndi amayi amene anasonkhana pamenepo. 14 Mmodzi wa amayi amene amamvetserawo ndi Lidiya amene amagulitsa nsalu zofiira, wochokera ku mzinda wa Tiyatira, ndipo amapembedza Mulungu. Ambuye anatsekula mtima wake kuti amve mawu a Paulo. 15 Iye ndi a mʼbanja lake atabatizidwa, anatiyitana kuti tipite ku nyumba yake. Iye anati, “Ngati mwanditenga ine kukhala wokhulupirira mwa Ambuye, bwerani mudzakhale mʼnyumba mwanga.” Ndipo anatiwumiriza ife kwambiri.

Paulo ndi Sila Mʼndende

16 Tsiku lina pamene timapita kumalo wopempherera, tinakumana ndi mtsikana wina amene anali ndi mzimu woyipa umene umanena zamʼtsogolo. Iye amapezera ndalama zambiri ambuye ake pa ulosi wake. 17 Mtsikanayu anatsatira Paulo ndi ife, akufuwula kuti, “Anthu awa ndi atumiki a Mulungu Wammwambamwamba, amene akukuwuzani inu njira yachipulumutso.” 18 Iye anachita izi masiku ambiri. Kenaka Paulo anavutika mu mtima, natembenuka ndipo anati kwa mzimuwo, “Ndikukulamula iwe mʼdzina la Yesu Khristu kuti utuluke mwa iye!” Nthawi yomweyo mzimuwo unatuluka.

19 Pamene ambuye a mtsikana uja anazindikira kuti chiyembekezo chawo chopezera ndalama chatha, anagwira Paulo ndi Sila nawakokera ku bwalo la akulu. 20 Anawabweretsa iwo kwa oweruza milandu ndipo anati, “Anthu awa ndi Ayuda, iwo akuvutitsa mu mzinda wathu. 21 Ndipo akuphunzitsa miyambo imene ife Aroma sitiloledwa kuyilandira kapena kuyichita.”

22 Gulu la anthu linatsutsana ndi Paulo ndi Sila, ndipo woweruza milandu analamula kuti avulidwe ndi kumenyedwa. 23 Atawakwapula kwambiri anawaponya mʼndende, nalamula woyangʼanira kuti awasunge mosamalitsa. 24 Chifukwa cha mawu amenewa woyangʼanira ndende anakawayika mʼchipinda chamʼkati mwa ndende, nawamangirira miyendo yawo mʼzigologolo.

25 Koma pakati pa usiku Paulo ndi Sila ankapemphera ndi kuyimba nyimbo zolemekeza Mulungu, ndipo akayidi ena ankamvetsera. 26 Mwadzidzidzi kunachitika chivomerezi champhamvu kotero kuti maziko a ndende anagwedezeka. Nthawi yomweyo zitseko zonse za ndende zinatsekuka, ndipo maunyolo a aliyense anamasuka. 27 Woyangʼanira ndende uja atadzuka ku tulo, anaona kuti zitseko za ndende zinali zotsekula, ndipo anasolola lupanga lake nafuna kudzipha chifukwa ankaganiza kuti amʼndende athawa. 28 Koma Paulo anafuwula kuti, “Usadzipweteke! Tonse tilipo!”

29 Woyangʼanira ndendeyo anayitanitsa nyale, nathamangira mʼkati ndipo anadzigwetsa pa mapazi a Paulo ndi Sila akunjenjemera. 30 Iye anawatulutsa kunja ndipo anawafunsa kuti, “Amuna inu, ndichite chiyani kuti ndipulumuke?”

31 Iwo anayankha kuti, “Khulupirira Ambuye Yesu ndipo udzapulumuka, iwe ndi a mʼbanja lako.” 32 Kenaka analalikira mawu a Ambuye kwa iyeyo ndi onse amene anali mʼnyumba mwake. 33 Usiku womwewo woyangʼanira ndendeyo anawatenga nakawatsuka mabala awo; ndipo pomwepo iye ndi a mʼbanja lake anabatizidwa. 34 Woyangʼanira ndendeyo anapita nawo ku nyumba yake, nakawapatsa chakudya, ndipo banja lonse linadzazidwa ndi chimwemwe chifukwa anakhulupirira Mulungu.

35 Kutacha, woweruza milandu uja anatuma asilikali kwa woyangʼanira ndendeyo kukanena kuti, “Amasuleni anthu aja.” 36 Woyangʼanira ndendeyo anawuza Paulo kuti, “Woweruza milandu walamula kuti iwe ndi Sila mumasulidwe. Tsopano muzipita. Pitani mumtendere.”

37 Koma Paulo anati kwa asilikaliwo: “Iwo anatikwapula pa gulu la anthu asanatiweruze, ngakhale kuti ndife nzika za Chiroma natiponya mʼndende. Kodi tsopano akufuna kutitulutsa mwamseri? Ayi! Asiyeni abwere okha kuti adzatitulutse.”

38 Asilikali aja anakafotokozera woweruza milandu ndipo pamene anamva kuti Paulo ndi Sila anali nzika za Chiroma, anachita mantha. 39 Iye anabwera kudzawapepesa ndipo anawatulutsa mʼndende, nawapempha kuti achoke mu mzindawo. 40 Paulo ndi Sila atatuluka mʼndende, anapita ku nyumba ya Lidiya, kumene anakumana ndi abale nawalimbikitsa. Kenaka anachoka.

Timothy Joins Paul and Silas

16 Paul came to Derbe and then to Lystra,(A) where a disciple named Timothy(B) lived, whose mother was Jewish and a believer(C) but whose father was a Greek. The believers(D) at Lystra and Iconium(E) spoke well of him. Paul wanted to take him along on the journey, so he circumcised him because of the Jews who lived in that area, for they all knew that his father was a Greek.(F) As they traveled from town to town, they delivered the decisions reached by the apostles and elders(G) in Jerusalem(H) for the people to obey.(I) So the churches were strengthened(J) in the faith and grew daily in numbers.(K)

Paul’s Vision of the Man of Macedonia

Paul and his companions traveled throughout the region of Phrygia(L) and Galatia,(M) having been kept by the Holy Spirit from preaching the word in the province of Asia.(N) When they came to the border of Mysia, they tried to enter Bithynia, but the Spirit of Jesus(O) would not allow them to. So they passed by Mysia and went down to Troas.(P) During the night Paul had a vision(Q) of a man of Macedonia(R) standing and begging him, “Come over to Macedonia and help us.” 10 After Paul had seen the vision, we(S) got ready at once to leave for Macedonia, concluding that God had called us to preach the gospel(T) to them.

Lydia’s Conversion in Philippi

11 From Troas(U) we put out to sea and sailed straight for Samothrace, and the next day we went on to Neapolis. 12 From there we traveled to Philippi,(V) a Roman colony and the leading city of that district[a] of Macedonia.(W) And we stayed there several days.

13 On the Sabbath(X) we went outside the city gate to the river, where we expected to find a place of prayer. We sat down and began to speak to the women who had gathered there. 14 One of those listening was a woman from the city of Thyatira(Y) named Lydia, a dealer in purple cloth. She was a worshiper of God. The Lord opened her heart(Z) to respond to Paul’s message. 15 When she and the members of her household(AA) were baptized,(AB) she invited us to her home. “If you consider me a believer in the Lord,” she said, “come and stay at my house.” And she persuaded us.

Paul and Silas in Prison

16 Once when we were going to the place of prayer,(AC) we were met by a female slave who had a spirit(AD) by which she predicted the future. She earned a great deal of money for her owners by fortune-telling. 17 She followed Paul and the rest of us, shouting, “These men are servants of the Most High God,(AE) who are telling you the way to be saved.” 18 She kept this up for many days. Finally Paul became so annoyed that he turned around and said to the spirit, “In the name of Jesus Christ I command you to come out of her!” At that moment the spirit left her.(AF)

19 When her owners realized that their hope of making money(AG) was gone, they seized Paul and Silas(AH) and dragged(AI) them into the marketplace to face the authorities. 20 They brought them before the magistrates and said, “These men are Jews, and are throwing our city into an uproar(AJ) 21 by advocating customs unlawful for us Romans(AK) to accept or practice.”(AL)

22 The crowd joined in the attack against Paul and Silas, and the magistrates ordered them to be stripped and beaten with rods.(AM) 23 After they had been severely flogged, they were thrown into prison, and the jailer(AN) was commanded to guard them carefully. 24 When he received these orders, he put them in the inner cell and fastened their feet in the stocks.(AO)

25 About midnight(AP) Paul and Silas(AQ) were praying and singing hymns(AR) to God, and the other prisoners were listening to them. 26 Suddenly there was such a violent earthquake that the foundations of the prison were shaken.(AS) At once all the prison doors flew open,(AT) and everyone’s chains came loose.(AU) 27 The jailer woke up, and when he saw the prison doors open, he drew his sword and was about to kill himself because he thought the prisoners had escaped.(AV) 28 But Paul shouted, “Don’t harm yourself! We are all here!”

29 The jailer called for lights, rushed in and fell trembling before Paul and Silas.(AW) 30 He then brought them out and asked, “Sirs, what must I do to be saved?”(AX)

31 They replied, “Believe(AY) in the Lord Jesus, and you will be saved(AZ)—you and your household.”(BA) 32 Then they spoke the word of the Lord to him and to all the others in his house. 33 At that hour of the night(BB) the jailer took them and washed their wounds; then immediately he and all his household were baptized.(BC) 34 The jailer brought them into his house and set a meal before them; he(BD) was filled with joy because he had come to believe in God—he and his whole household.

35 When it was daylight, the magistrates sent their officers to the jailer with the order: “Release those men.” 36 The jailer(BE) told Paul, “The magistrates have ordered that you and Silas be released. Now you can leave. Go in peace.”(BF)

37 But Paul said to the officers: “They beat us publicly without a trial, even though we are Roman citizens,(BG) and threw us into prison. And now do they want to get rid of us quietly? No! Let them come themselves and escort us out.”

38 The officers reported this to the magistrates, and when they heard that Paul and Silas were Roman citizens, they were alarmed.(BH) 39 They came to appease them and escorted them from the prison, requesting them to leave the city.(BI) 40 After Paul and Silas came out of the prison, they went to Lydia’s house,(BJ) where they met with the brothers and sisters(BK) and encouraged them. Then they left.

Footnotes

  1. Acts 16:12 The text and meaning of the Greek for the leading city of that district are uncertain.