Add parallel Print Page Options

Ine ndine munthu amene ndaona masautso
    ndi ndodo ya ukali wake.
Wandipititsa kutali ndipo wandiyendetsa
    mu mdima osati mʼkuwala;
zoonadi anandikantha ndi dzanja lake
    mobwerezabwereza tsiku lonse.

Wakalambitsa khungu langa ndi mnofu wanga,
    ndipo waphwanya mafupa anga.
Wandizinga ndi kundizungulira
    ndi zowawa ndi zolemetsa.
Wandikhazika mu mdima
    ngati amene anafa kale.

Wandimangira khoma kotero kuti sindingathawe,
    wandimanga ndi maunyolo.
Ngakhale pamene ndifuwula kapena kupempha chithandizo,
    amakana pemphero langa.
Wanditsekera njira yanga ndi miyala yosema;
    ndipo wakhotetsa tinjira tanga.

10 Wandidikirira ngati chimbalangondo,
    wandibisalira ngati mkango.
11 Wandikokera pambali ndi kundingʼambangʼamba,
    ndipo wandisiya wopanda thandizo.
12 Wakoka uta wake
    ndipo walunjikitsa mivi yake pa ine.

13 Walasa mtima wanga
    ndi mivi ya mʼphodo mwake.
14 Ndinakhala choseketsa cha anthu anga onse;
    amandinyodola mʼnyimbo zawo tsiku lonse.
15 Wandidyetsa zowawa
    ndipo wandimwetsa ndulu.

16 Wathyola mano anga ndi miyala;
    wandiviviniza mʼfumbi;
17 Wandichotsera mtendere;
    ndayiwala kuti kupeza bwino nʼchiyani.
18 Choncho ndikuti, “Ulemerero wanga wachoka
    ndi zonse zimene ndimayembekeza kwa Yehova.”

19 Kukumbukira masautso anga ndi kusowa pokhala,
    zili ngati zowawa ndi ndulu.
20 Ine ndikuzikumbukira bwino izi,
    ndipo moyo wanga wathedwa mʼkati mwanga.
21 Komabe ndimakumbukira zimenezi,
    nʼchifukwa chake ndili ndi chiyembekezo.

22 Ife sitinawonongekeretu chifukwa chikondi cha Yehova ndi chachikulu,
    ndi chifundo chake ndi chosatha.
23 Zimaoneka zatsopano mmawa uliwonse;
    kukhulupirika kwanu nʼkwakukulu.
24 Mu mtima mwanga ndimati, “Yehova ndiye zanga zonse;
    motero ndimamuyembekezera.”

25 Yehova ndi wabwino kwa amene amayembekezera Iye,
    kwa munthu amene amafunafuna Iyeyo;
26 nʼkwabwino kudikira chipulumutso cha
    Yehova modekha.
27 Nʼkwabwino kuti munthu asenze goli
    pamene ali wamngʼono.

28 Akhale chete pa yekha,
    chifukwa Yehova wamusenzetsa golilo.
29 Abise nkhope yake mʼfumbi
    mwina chiyembekezo nʼkukhalapobe.
30 Apereke tsaya lake kwa iye amene angamumenye,
    ndipo amuchititse manyazi.

31 Chifukwa Ambuye satayiratu
    anthu nthawi zonse.
32 Ngakhale amabweretsa zowawa, Iye adzawachitira chifundo,
    chifukwa chikondi chake ndi chosatha.
33 Pakuti sabweretsa masautso mwadala,
    kapena zowawa kwa ana a anthu.

34 Kuphwanya ndi phazi
    a mʼndende onse a mʼdziko,
35 kukaniza munthu ufulu wake
    pamaso pa Wammwambamwamba,
36 kumana munthu chiweruzo cholungama—
    kodi Ambuye saona zonsezi?

37 Kodi ndani angayankhule zinthu nʼkuchitika
    ngati Ambuye sanavomereze?
38 Kodi zovuta ndi zabwino sizituluka
    mʼkamwa mwa Wammwambamwamba?
39 Kodi nʼchifukwa chiyani munthu aliyense wamoyo amadandaula
    akalangidwa chifukwa cha machimo ake?

40 Tiyeni tisanthule ndi kuyesa njira zathu,
    ndipo tiyeni tibwerere kwa Yehova.
41 Tiyeni tikweze mitima yathu ndi manja athu
    kwa Mulungu kumwamba ndipo tinene kuti:
42 “Ife tachimwa ndi kuwukira
    ndipo inu simunakhululuke.

43 “Mwadzikuta ndi mkwiyo ndi kutilondola ndipo
    mwatitha mopanda chifundo.
44 Mwadzikuta mu mtambo
    kotero mapemphero athu sakukufikani.
45 Mwatisandutsa zinyatsi ndi zinyalala
    pakati pa mitundu ya anthu.

46 “Adani anthu atitsekulira pakamwa.
47 Ife tadzazidwa ndi mantha pakuti tagwa mʼdzenje,
    tapasuka ndi kuwonongedwa.”
48 Misozi mʼmaso mwanga ikungoti mbwembwembwe
    chifukwa anthu anga akuwonongedwa.

49 Misozi idzatsika kosalekeza,
    ndipo sidzasiya,
50 mpaka Yehova ayangʼane pansi
    kuchokera kumwamba ndi kuona.
51 Mtima wanga ukupweteka poona zimenezi
    chifukwa cha akazi onse a mu mzinda.

52 Akundisaka ngati mbalame,
    amene anali adani anga, popanda chifukwa.
53 Ayesa kundipha pondiponya mʼdzenje
    ndi kundiponya miyala;
54 madzi anamiza mutu wanga
    ndipo ndinkaganiza kuti imfa yayandikira.

55 Ndinayitana dzina lanu Inu Yehova,
    kuchokera mʼdzenje lozama.
56 Inu munamva kudandaula kwanga. “Mundimvere
    kulira kwanga kopempha thandizo.”
57 Munafika pafupi pamene ndinakuyitanani,
    ndipo munati, “Usaope.”

58 Inu Ambuye munandiwombola ku mlandu wanga;
    munapulumutsa moyo wanga.
59 Yehova, mwaona zoyipa zimene andichitira.
    Mundiweruzire ndinu!
60 Mwaona kuzama kwa kubwezera kwawo,
    chiwembu chawo chonse pa ine.

61 Inu Yehova mwamva kunyoza kwawo,
    chiwembu chawo chonse pa ine,
62 manongʼonongʼo a adani anga
    ondiwukira ine tsiku lonse.
63 Tawaonani! Kaya ali pansi kapena kuyimirira,
    akundinyoza mu nyimbo zawo.

64 Inu Yehova, muwabwezere chowayenera,
    chifukwa cha zimene manja awo achita.
65 Phimbani mitima yawo,
    ndipo matemberero anu akhale pa iwo!
66 Muwalondole mwaukali ndipo
    muwawonongeretu pa dziko lapansi.