Masalimo 137
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
137 Mʼmbali mwa mitsinje ya ku Babuloni tinakhala pansi ndi kulira
pamene tinakumbukira Ziyoni.
2 Kumeneko, pa mitengo ya misondozi
tinapachika apangwe athu,
3 pakuti anthu otigwira ukapolo anatipempha kuti tiyimbe nyimbo.
Otizunza athu anafuna nyimbo zachisangalalo;
iwo anati, “Tiyimbireni imodzi mwa nyimbo za ku Ziyoni!”
4 Tingayimbe bwanji nyimbo za Yehova
mʼdziko lachilendo?
5 Ndikakuyiwala iwe Yerusalemu,
dzanja langa lamanja liyiwale luso lake.
6 Lilime langa limamatire ku nkhama za mʼkamwa mwanga
ndikapanda kukukumbukira iwe Yerusalemu,
ngati sindiyesa iwe
chimwemwe changa chachikulu.
7 Kumbukirani, Inu Yehova, zimene Aedomu anachita
pa tsiku limene Yerusalemu anagonja.
Iwowo anafuwula kuti, “Mugwetseni pansi, mugwetseni pansi
mpaka pa maziko ake!”
8 Iwe mwana wa mkazi wa Babuloni, woyenera kuwonongedwa,
wodalitsika ndi yemwe adzakubwezera
pa zimene watichitira.
9 Amene adzagwira makanda ako
ndi kuwakankhanthitsa pa miyala.
Psalm 137
New International Version
Psalm 137
1 By the rivers of Babylon(A) we sat and wept(B)
when we remembered Zion.(C)
2 There on the poplars(D)
we hung our harps,(E)
3 for there our captors(F) asked us for songs,
our tormentors demanded(G) songs of joy;
they said, “Sing us one of the songs of Zion!”(H)
4 How can we sing the songs of the Lord(I)
while in a foreign land?
5 If I forget you,(J) Jerusalem,
may my right hand forget its skill.
6 May my tongue cling to the roof(K) of my mouth
if I do not remember(L) you,
if I do not consider Jerusalem(M)
my highest joy.
7 Remember, Lord, what the Edomites(N) did
on the day Jerusalem fell.(O)
“Tear it down,” they cried,
“tear it down to its foundations!”(P)
8 Daughter Babylon, doomed to destruction,(Q)
happy is the one who repays you
according to what you have done to us.
9 Happy is the one who seizes your infants
and dashes them(R) against the rocks.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.
Holy Bible, New International Version®, NIV® Copyright ©1973, 1978, 1984, 2011 by Biblica, Inc.® Used by permission. All rights reserved worldwide.
NIV Reverse Interlinear Bible: English to Hebrew and English to Greek. Copyright © 2019 by Zondervan.