Add parallel Print Page Options

137 Mʼmbali mwa mitsinje ya ku Babuloni tinakhala pansi ndi kulira
    pamene tinakumbukira Ziyoni.
Kumeneko, pa mitengo ya misondozi
    tinapachika apangwe athu,
pakuti anthu otigwira ukapolo anatipempha kuti tiyimbe nyimbo.
    Otizunza athu anafuna nyimbo zachisangalalo;
    iwo anati, “Tiyimbireni imodzi mwa nyimbo za ku Ziyoni!”

Tingayimbe bwanji nyimbo za Yehova
    mʼdziko lachilendo?
Ndikakuyiwala iwe Yerusalemu,
    dzanja langa lamanja liyiwale luso lake.
Lilime langa limamatire ku nkhama za mʼkamwa mwanga
    ndikapanda kukukumbukira iwe Yerusalemu,
ngati sindiyesa iwe
    chimwemwe changa chachikulu.

Kumbukirani, Inu Yehova, zimene Aedomu anachita
    pa tsiku limene Yerusalemu anagonja.
Iwowo anafuwula kuti, “Mugwetseni pansi, mugwetseni pansi
    mpaka pa maziko ake!”

Iwe mwana wa mkazi wa Babuloni, woyenera kuwonongedwa,
    wodalitsika ndi yemwe adzakubwezera
    pa zimene watichitira.
Amene adzagwira makanda ako
    ndi kuwakankhanthitsa pa miyala.

Psalm 137

By the rivers of Babylon(A) we sat and wept(B)
    when we remembered Zion.(C)
There on the poplars(D)
    we hung our harps,(E)
for there our captors(F) asked us for songs,
    our tormentors demanded(G) songs of joy;
    they said, “Sing us one of the songs of Zion!”(H)

How can we sing the songs of the Lord(I)
    while in a foreign land?
If I forget you,(J) Jerusalem,
    may my right hand forget its skill.
May my tongue cling to the roof(K) of my mouth
    if I do not remember(L) you,
if I do not consider Jerusalem(M)
    my highest joy.

Remember, Lord, what the Edomites(N) did
    on the day Jerusalem fell.(O)
“Tear it down,” they cried,
    “tear it down to its foundations!”(P)
Daughter Babylon, doomed to destruction,(Q)
    happy is the one who repays you
    according to what you have done to us.
Happy is the one who seizes your infants
    and dashes them(R) against the rocks.