Add parallel Print Page Options

Salimo la Davide.

23 Yehova ndiye mʼbusa wanga, sindidzasowa kanthu.
    Amandigoneka pa msipu wobiriwira,
amanditsogolera ku madzi akumwa abwino,
    amatsitsimutsa moyo wanga.
Amanditsogolera mʼnjira zachilungamo
    chifukwa cha dzina lake.
Ngakhale ndiyende
    mʼchigwa cha mdima wakuda bii,
sindidzaopa choyipa,
    pakuti Inu muli ndi ine;
chibonga chanu ndi ndodo yanu
    zimanditonthoza.

Mumandikonzera chakudya
    adani anga akuona.
Mumadzoza mutu wanga ndi mafuta;
    chikho changa chimasefukira.
Zoonadi, zokoma ndi chikondi chosasinthika zidzanditsata
    masiku onse a moyo wanga,
ndipo ndidzakhala mʼNyumba ya Yehova
    kwamuyaya.

Psalm 23

A psalm of David.

The Lord is my shepherd,(A) I lack nothing.(B)
    He makes me lie down in green pastures,
he leads me beside quiet waters,(C)
    he refreshes my soul.(D)
He guides me(E) along the right paths(F)
    for his name’s sake.(G)
Even though I walk
    through the darkest valley,[a](H)
I will fear no evil,(I)
    for you are with me;(J)
your rod and your staff,
    they comfort me.

You prepare a table(K) before me
    in the presence of my enemies.
You anoint my head with oil;(L)
    my cup(M) overflows.
Surely your goodness and love(N) will follow me
    all the days of my life,
and I will dwell in the house of the Lord
    forever.

Footnotes

  1. Psalm 23:4 Or the valley of the shadow of death