Add parallel Print Page Options

Salimo la Davide.

29 Perekani kwa Yehova, inu anthu amphamvu,
    perekani kwa Yehova ulemerero ndi mphamvu.
Perekani kwa Yehova ulemerero woyenera dzina lake,
    pembedzani Yehova mwa kukongola kwa chiyero chake.

Liwu la Yehova lili pamwamba pa madzi;
    Mulungu waulemerero abangula,
    Yehova abangula pamwamba pa madzi amphamvu.
Liwu la Yehova ndi lamphamvu;
    liwu la Yehova ndi laulemerero.
Liwu la Yehova limathyola mikungudza;
    Yehova amathyolathyola mikungudza ya ku Lebanoni.
Iye amachititsa Lebanoni kulumphalumpha ngati mwana wangʼombe,
    Siriyoni ngati mwana wa njati:
Liwu la Yehova limakantha
    ngati kungʼanima kwa mphenzi.
Liwu la Yehova limagwedeza chipululu;
    Yehova amagwedeza chipululu cha Kadesi.
Liwu la Yehova limapindapinda mibawa
    ndi kuyeretsa nkhalango.
Ndipo mʼNyumba mwake onse amafuwula kuti, “Ulemerero!”

10 Yehova amakhala pamwamba pa madzi osefukira,
    Yehova ndiye mfumu kwamuyaya.
11 Yehova amapereka mphamvu kwa anthu ake;
    Yehova amadalitsa anthu ake ndi mtendere.

Psalm 29

A psalm of David.

Ascribe to the Lord,(A) you heavenly beings,(B)
    ascribe to the Lord glory(C) and strength.
Ascribe to the Lord the glory due his name;
    worship the Lord in the splendor of his[a] holiness.(D)

The voice(E) of the Lord is over the waters;
    the God of glory(F) thunders,(G)
    the Lord thunders over the mighty waters.(H)
The voice of the Lord is powerful;(I)
    the voice of the Lord is majestic.
The voice of the Lord breaks the cedars;
    the Lord breaks in pieces the cedars of Lebanon.(J)
He makes Lebanon leap(K) like a calf,
    Sirion[b](L) like a young wild ox.(M)
The voice of the Lord strikes
    with flashes of lightning.(N)
The voice of the Lord shakes the desert;
    the Lord shakes the Desert of Kadesh.(O)
The voice of the Lord twists the oaks[c](P)
    and strips the forests bare.
And in his temple all cry, “Glory!”(Q)

10 The Lord sits enthroned over the flood;(R)
    the Lord is enthroned as King forever.(S)
11 The Lord gives strength to his people;(T)
    the Lord blesses his people with peace.(U)

Footnotes

  1. Psalm 29:2 Or Lord with the splendor of
  2. Psalm 29:6 That is, Mount Hermon
  3. Psalm 29:9 Or Lord makes the deer give birth