Masalimo 44
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Ndakatulo ya ana a Kora.
44 Ife tamva ndi makutu athu, Inu Mulungu;
makolo athu atiwuza
zimene munachita mʼmasiku awo,
masiku akalekalewo.
2 Ndi dzanja lanu munathamangitsa mitundu ya anthu ena
ndi kudzala makolo athu;
Inu munakantha mitundu ya anthu,
koma makolo athuwo Inu munawapatsa ufulu.
3 Sanalande dziko ndi lupanga lawo,
si mkono wawo umene unawabweretsera chigonjetso,
koma ndi dzanja lanu lamanja, mkono wanu ndi kuwala kwa nkhope yanu,
pakuti munawakonda.
4 Inu ndinu Mfumu yanga ndi Mulungu wanga
amene mumalamulira chigonjetso cha Yakobo.
5 Kudzera kwa inu ife timabweza adani athu;
kudzera mʼdzina lanu timapondereza otiwukirawo.
6 Sindidalira uta wanga,
lupanga langa silindibweretsera chigonjetso;
7 koma Inu mumatigonjetsera adani athu,
mumachititsa manyazi amene amadana nafe.
8 Timanyadira mwa Mulungu wathu tsiku lonse,
ndipo tidzatamanda dzina lanu kwamuyaya.
9 Koma tsopano mwatikana ndi kutichepetsa;
Inu simupitanso ndi ankhondo athu.
10 Munachititsa ife kubwerera mʼmbuyo pamaso pa mdani
ndipo amene amadana nafe atilanda katundu.
11 Inu munatipereka kuti tiwonongedwe monga nkhosa
ndipo mwatibalalitsa pakati pa anthu a mitundu ina.
12 Inu munagulitsa anthu anu pa mtengo wotsika,
osapindulapo kanthu pa malondawo.
13 Mwachititsa kuti tikhale chochititsa manyazi kwa anthu a mitundu ina,
chonyozeka ndi chothetsa nzeru kwa iwo amene atizungulira.
14 Mwachititsa kuti tikhale onyozeka pakati pa anthu a mitundu ina;
anthu amapukusa mitu yawo akationa.
15 Manyazi anga ali pamaso panga tsiku lonse
ndipo nkhope yanga yaphimbidwa ndi manyazi
16 chifukwa cha mawu otonza a iwo amene amandinyoza ndi kundichita chipongwe,
chifukwa cha mdani amene watsimikiza kubwezera.
17 Zonsezi zinatichitikira
ngakhale kuti ifeyo sitinayiwale Inu
kapena kuonetsa kusakhulupirika pa pangano lanu.
18 Mitima yathu sinabwerere mʼmbuyo;
mapazi athu sanatayike pa njira yanu.
19 Koma Inu mwatiphwanya ndi kuchititsa kuti tikhale ozunzidwa ndi ankhandwe
ndipo mwatiphimba ndi mdima waukulu.
20 Tikanayiwala dzina la Mulungu wathu
kapena kutambasulira manja athu kwa mulungu wachilendo,
21 kodi Mulungu wathu sakanazidziwa zimenezi,
pakuti Iye amadziwa zinsinsi zamumtima?
22 Komabe chifukwa cha Inu timakumana ndi imfa tsiku lonse,
tili ngati nkhosa zoyenera kuti ziphedwe.
23 Dzukani Ambuye! Nʼchifukwa chiyani mukugona!
Dziwutseni nokha! Musatikane kwamuyaya.
24 Nʼchifukwa chiyani mukubisa nkhope yanu,
ndi kuyiwala mavuto athu ndi kuponderezedwa kwathu?
25 Tatsitsidwa pansi mpaka pa fumbi;
matupi athu amatirira pa dothi.
26 Imirirani ndi kutithandiza,
tiwomboleni chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika.
Psalm 44
New International Version
Psalm 44[a]
For the director of music. Of the Sons of Korah. A maskil.[b]
1 We have heard it with our ears,(A) O God;
our ancestors have told us(B)
what you did in their days,
in days long ago.(C)
2 With your hand you drove out(D) the nations
and planted(E) our ancestors;
you crushed(F) the peoples
and made our ancestors flourish.(G)
3 It was not by their sword(H) that they won the land,
nor did their arm bring them victory;
it was your right hand,(I) your arm,(J)
and the light(K) of your face, for you loved(L) them.
4 You are my King(M) and my God,(N)
who decrees[c] victories(O) for Jacob.
5 Through you we push back(P) our enemies;
through your name we trample(Q) our foes.
6 I put no trust in my bow,(R)
my sword does not bring me victory;
7 but you give us victory(S) over our enemies,
you put our adversaries to shame.(T)
8 In God we make our boast(U) all day long,(V)
and we will praise your name forever.[d](W)
9 But now you have rejected(X) and humbled us;(Y)
you no longer go out with our armies.(Z)
10 You made us retreat(AA) before the enemy,
and our adversaries have plundered(AB) us.
11 You gave us up to be devoured like sheep(AC)
and have scattered us among the nations.(AD)
12 You sold your people for a pittance,(AE)
gaining nothing from their sale.
13 You have made us a reproach(AF) to our neighbors,(AG)
the scorn(AH) and derision(AI) of those around us.
14 You have made us a byword(AJ) among the nations;
the peoples shake their heads(AK) at us.
15 I live in disgrace(AL) all day long,
and my face is covered with shame(AM)
16 at the taunts(AN) of those who reproach and revile(AO) me,
because of the enemy, who is bent on revenge.(AP)
17 All this came upon us,
though we had not forgotten(AQ) you;
we had not been false to your covenant.
18 Our hearts had not turned(AR) back;
our feet had not strayed from your path.
19 But you crushed(AS) us and made us a haunt for jackals;(AT)
you covered us over with deep darkness.(AU)
20 If we had forgotten(AV) the name of our God
or spread out our hands to a foreign god,(AW)
21 would not God have discovered it,
since he knows the secrets of the heart?(AX)
22 Yet for your sake we face death all day long;
we are considered as sheep(AY) to be slaughtered.(AZ)
Footnotes
- Psalm 44:1 In Hebrew texts 44:1-26 is numbered 44:2-27.
- Psalm 44:1 Title: Probably a literary or musical term
- Psalm 44:4 Septuagint, Aquila and Syriac; Hebrew King, O God; / command
- Psalm 44:8 The Hebrew has Selah (a word of uncertain meaning) here.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.
Holy Bible, New International Version®, NIV® Copyright ©1973, 1978, 1984, 2011 by Biblica, Inc.® Used by permission. All rights reserved worldwide.
NIV Reverse Interlinear Bible: English to Hebrew and English to Greek. Copyright © 2019 by Zondervan.