Add parallel Print Page Options

BUKU LACHITATU

Masalimo 73–89

Salimo la Asafu.

73 Mulungu ndi wabwino ndithu kwa Israeli,
    kwa iwo amene ndi oyera mtima.

Koma kunena za ine, mapazi anga anali pafupi kuterereka;
    ndinatsala pangʼono kugwa.
Pakuti ndinkachitira nsanje odzitamandira,
    pamene ndinaona mtendere wa anthu oyipa.

Iwo alibe zosautsa;
    matupi awo ndi athanzi ndi amphamvu.
Saona mavuto monga anthu ena;
    sazunzika ngati anthu ena onse.
Nʼchifukwa chake kunyada kuli monga mkanda wa mʼkhosi mwawo;
    amadziveka chiwawa.
Mʼmitima yawo yokhota mumachokera zolakwa;
    zoyipa zochokera mʼmaganizo awo sizidziwa malire.
Iwowo amanyogodola ndi kumayankhula zoyipa;
    mwa kudzikuza kwawo amaopseza ena nʼkumati, “Tikuponderezani.”
Pakamwa pawo pamayankhula monyoza Mulungu kumwamba
    ndipo lilime lawo limayenda pa dziko lapansi.
10 Nʼchifukwa chake anthu awo amapita kwa iwowo
    ndi kumwa madzi mochuluka.
11 Iwo amati, “Kodi Mulungu angadziwe bwanji?
    Kodi Wammwambamwamba angadziwe kalikonse?”

12 Umu ndi mmene oyipa alili;
    nthawi zonse ali pabwino ndipo chuma chawo chimachulukirachulukira.

13 Ndithudi ine ndawusunga pachabe mtima wanga woyera;
    pachabe ndasamba mʼmanja mwanga mwa kusalakwa kwanga.
14 Tsiku lonse ndapeza mavuto;
    ndakhala ndi kulangidwa mmawa uliwonse.

15 Ndikanati, “Ndidzayankhula motere,”
    ndikanachita chosakhulupirika kwa ana anu.
16 Pamene ndinayesa kuti ndimvetse zonsezi,
    zinandisautsa kwambiri
17 kufikira nditalowa mʼmalo opatulika a Mulungu;
    pamenepo ndinamvetsa mathero awo.

18 Zoonadi Inu munawayika pa malo woterera;
    Mumawagwetsa pansi kuti awonongeke.
19 Mwamsangamsanga iwo amawonongedwa,
    amasesedwa kwathunthu ndi mantha!
20 Monga loto pamene wina adzuka,
    kotero pamene Inu muuka, Inu Ambuye,
    mudzawanyoza ngati maloto chabe.

21 Pamene mtima wanga unasautsidwa
    ndi kuwawidwa mu mzimu mwanga,
22 ndinali wopusa ndi wosadziwa;
    ndinali chirombo chopanda nzeru pamaso panu.

23 Komabe ineyo ndili ndi Inu nthawi zonse;
    mumandigwira dzanja langa lamanja.
24 Inu mumanditsogolera ndi malangizo anu
    ndipo pambuyo pake mudzanditenga ku ulemerero.
25 Kodi kumwamba ndili ndi yani kupatula Inu?
    Ndipo dziko lapansi lilibe chilichonse chimene ndimachilakalaka koposa Inuyo.
26 Thupi ndi mtima wanga zitha kufowoka,
    koma Mulungu ndiye mphamvu ya mtima wanga
    ndi cholandira changa kwamuyaya.

27 Iwo amene ali kutali ndi Inu adzawonongeka;
    Inu mumawononga onse osakhulupirika pamaso panu.
28 Koma kunena za Ine ndi kwabwino kukhala pafupi ndi Mulungu.
    Ndatsimikiza kuti Ambuye Yehova ndiwo pothawirapo panga
    ndipo ndidzalalika ntchito zanu zonse.

BOOK III

Psalms 73–89

Psalm 73

A psalm of Asaph.

Surely God is good to Israel,
    to those who are pure in heart.(A)

But as for me, my feet had almost slipped;(B)
    I had nearly lost my foothold.(C)
For I envied(D) the arrogant
    when I saw the prosperity of the wicked.(E)

They have no struggles;
    their bodies are healthy and strong.[a]
They are free(F) from common human burdens;
    they are not plagued by human ills.
Therefore pride(G) is their necklace;(H)
    they clothe themselves with violence.(I)
From their callous hearts(J) comes iniquity[b];
    their evil imaginations have no limits.
They scoff, and speak with malice;(K)
    with arrogance(L) they threaten oppression.(M)
Their mouths lay claim to heaven,
    and their tongues take possession of the earth.
10 Therefore their people turn to them
    and drink up waters in abundance.[c]
11 They say, “How would God know?
    Does the Most High know anything?”

12 This is what the wicked are like—
    always free of care,(N) they go on amassing wealth.(O)

13 Surely in vain(P) I have kept my heart pure
    and have washed my hands in innocence.(Q)
14 All day long I have been afflicted,(R)
    and every morning brings new punishments.

15 If I had spoken out like that,
    I would have betrayed your children.
16 When I tried to understand(S) all this,
    it troubled me deeply
17 till I entered the sanctuary(T) of God;
    then I understood their final destiny.(U)

18 Surely you place them on slippery ground;(V)
    you cast them down to ruin.(W)
19 How suddenly(X) are they destroyed,
    completely swept away(Y) by terrors!
20 They are like a dream(Z) when one awakes;(AA)
    when you arise, Lord,
    you will despise them as fantasies.(AB)

21 When my heart was grieved
    and my spirit embittered,
22 I was senseless(AC) and ignorant;
    I was a brute beast(AD) before you.

23 Yet I am always with you;
    you hold me by my right hand.(AE)
24 You guide(AF) me with your counsel,(AG)
    and afterward you will take me into glory.
25 Whom have I in heaven but you?(AH)
    And earth has nothing I desire besides you.(AI)
26 My flesh and my heart(AJ) may fail,(AK)
    but God is the strength(AL) of my heart
    and my portion(AM) forever.

27 Those who are far from you will perish;(AN)
    you destroy all who are unfaithful(AO) to you.
28 But as for me, it is good to be near God.(AP)
    I have made the Sovereign Lord my refuge;(AQ)
    I will tell of all your deeds.(AR)

Footnotes

  1. Psalm 73:4 With a different word division of the Hebrew; Masoretic Text struggles at their death; / their bodies are healthy
  2. Psalm 73:7 Syriac (see also Septuagint); Hebrew Their eyes bulge with fat
  3. Psalm 73:10 The meaning of the Hebrew for this verse is uncertain.