Add parallel Print Page Options

Salimo la ana a Kora. Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a nyimbo yoti: “Pa Matenda ndi pa Mazunzo.” Ndakatulo ya Hemani, wa banja la Ezara.

88 Inu Yehova, Mulungu amene mumandipulumutsa,
    usana ndi usiku ndimalira pamaso panu.
Pemphero langa lifike pamaso panu;
    tcherani khutu lanu kuti mumve kulira kwanga.

Pakuti ndili ndi mavuto ambiri
    ndipo moyo wanga ukuyandikira ku manda.
Ndikuwerengedwa pamodzi ndi iwo amene akutsikira ku dzenje;
    ndine munthu wopanda mphamvu.
Ndayikidwa pambali pamodzi ndi anthu akufa,
    monga ophedwa amene agona mʼmanda,
amene Inu simuwakumbukiranso,
    amene achotsedwa pa chisamaliro chanu.

Mwandiyika pansi pa dzenje penipeni,
    mʼmalo akuya a mdima waukulu.
Ukali wanu ukundipsinja kwambiri,
    mwandiopseza kwambiri ndi mafunde anu onse.
            Sela
Mwandichotsa pakati pa abwenzi anga enieni
    ndipo mwachititsa kuti ndikhale chonyansa kwa iwo.
Ndatsekerezedwa ndipo sindingathe kuthawa;
    maso anga ada ndi chisoni.

Ndimayitana Inu Yehova tsiku lililonse;
    ndimakweza manja anga kwa Inu.
10 Kodi mumaonetsa zozizwitsa zanu kwa anthu akufa?
    Kodi iwo amene afa amaukanso ndi kutamanda Inu?
            Sela
11 Kodi chikondi chanu chimalalikidwa mʼmanda,
    za kukhulupirika kwanu ku malo a chiwonongeko?
12 Kodi zozizwitsa zanu zimadziwika ku malo a mdima,
    kapena ntchito zanu zolungama ku dziko la anthu oyiwalika?

13 Inu Yehova, Ine ndimalirira thandizo;
    mmawa mapemphero anga amafika pamaso panu.
14 Inu Yehova nʼchifukwa chiyani mukundikana
    ndi kundibisira nkhope yanu?

15 Kuyambira ubwana wanga ndakhala ndikuzunzika pafupi kufa;
    ndakhala ndikuchita mantha ndipo ndine wothedwa nzeru.
16 Ukali wanu wandimiza;
    zoopsa zanu zandiwononga.
17 Tsiku lonse zimandizungulira ngati chigumula;
    zandimiza kwathunthu.
18 Inu mwatenga anzanga ndi okondedwa anga kuwachotsa pamaso panga;
    mdima ndiye bwenzi langa lenileni.

Psalm 88[a]

A song. A psalm of the Sons of Korah. For the director of music. According to mahalath leannoth.[b] A maskil[c] of Heman the Ezrahite.

Lord, you are the God who saves me;(A)
    day and night I cry out(B) to you.
May my prayer come before you;
    turn your ear to my cry.

I am overwhelmed with troubles(C)
    and my life draws near to death.(D)
I am counted among those who go down to the pit;(E)
    I am like one without strength.(F)
I am set apart with the dead,
    like the slain who lie in the grave,
whom you remember no more,
    who are cut off(G) from your care.

You have put me in the lowest pit,
    in the darkest depths.(H)
Your wrath(I) lies heavily on me;
    you have overwhelmed me with all your waves.[d](J)
You have taken from me my closest friends(K)
    and have made me repulsive to them.
I am confined(L) and cannot escape;(M)
    my eyes(N) are dim with grief.

I call(O) to you, Lord, every day;
    I spread out my hands(P) to you.
10 Do you show your wonders to the dead?
    Do their spirits rise up and praise you?(Q)
11 Is your love declared in the grave,
    your faithfulness(R) in Destruction[e]?
12 Are your wonders known in the place of darkness,
    or your righteous deeds in the land of oblivion?

13 But I cry to you for help,(S) Lord;
    in the morning(T) my prayer comes before you.(U)
14 Why, Lord, do you reject(V) me
    and hide your face(W) from me?

15 From my youth(X) I have suffered(Y) and been close to death;
    I have borne your terrors(Z) and am in despair.(AA)
16 Your wrath(AB) has swept over me;
    your terrors(AC) have destroyed me.
17 All day long they surround me like a flood;(AD)
    they have completely engulfed me.
18 You have taken from me friend(AE) and neighbor—
    darkness is my closest friend.

Footnotes

  1. Psalm 88:1 In Hebrew texts 88:1-18 is numbered 88:2-19.
  2. Psalm 88:1 Title: Possibly a tune, “The Suffering of Affliction”
  3. Psalm 88:1 Title: Probably a literary or musical term
  4. Psalm 88:7 The Hebrew has Selah (a word of uncertain meaning) here and at the end of verse 10.
  5. Psalm 88:11 Hebrew Abaddon