Nehemiya 7
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
7 Khoma linamangidwa ndipo zitseko zinayikidwa. Pambuyo pake alonda a Nyumba ya Mulungu, oyimba nyimbo ndiponso Alevi anasankhidwa. 2 Kenaka ine ndinasankha mʼbale wanga Hanani pamodzi ndi Hananiya woyangʼanira nsanja yankhondo kukhala olamulira Yerusalemu chifukwa iyeyu anali munthu odalirika ndi woopa Mulungu kuposa anthu ena. 3 Ine ndinawawuza kuti, “Musalole kuti zipata za Yerusalemu zitsekulidwe mpaka dzuwa litatentha, ndipo alonda asanaweruke aonetsetse kuti atseka zitseko ndi kuzipiringidza. Musankhe alonda pakati pa anthu okhala mu Yerusalemu, ena akhale pa malo pawo ndi ena akhale moyangʼanana ndi nyumba zawo.”
Mndandanda wa Anthu Oyamba Kubwera Kuchokera ku Ukapolo
4 Tsono mzinda wa Yerusalemu unali wotambasuka ndiponso waukulu koma munali anthu ochepa ndipo nyumba zinali zisanamangidwe. 5 Ndipo Mulungu wanga anayika mu mtima mwanga maganizo oti ndisonkhanitse anthu olemekezeka, akuluakulu ndi anthu onse kuti alembetse mayina mwa mabanja awo. Ndinapeza buku limene munalembedwa mayina a mabanja a iwo amene anayamba kubwera kuchokera ku ukapolo. Izi ndi zimene ndinazipeza zitalembedwa mʼmenemo:
6 Awa ndi anthu a mʼchigawo cha Yuda amene anabwerera kuchokera ku ukapolo amene Nebukadinezara mfumu ya Babuloni anawatenga ukapolo. Iwo anabwerera ku Yerusalemu ndi ku Yuda, aliyense ku mzinda wa makolo ake. 7 Anabwera pamodzi ndi atsogoleri awa: Zerubabeli, Yesuwa, Nehemiya, Azariya, Raamiya, Nahamani, Mordekai, Bilisani, Misipereti, Bigivai, Nehumu ndi Baana.
Tsono chiwerengero cha anthu a ku Israeli chinali chotere:
8 Zidzukulu za Parosi | 2,172 |
9 Zidzukulu za Sefatiya | 372 |
10 Zidzukulu za Ara | 652 |
11 Zidzukulu za Pahati-Mowabu (kudzera mu mʼbado wa Yesuwa ndi Yowabu) | 2,818 |
12 Zidzukulu za Elamu | 1,254 |
13 Zidzukulu za Zatu | 845 |
14 Zidzukulu za Zakai | 760 |
15 Zidzukulu za Binuyi | 648 |
16 Zidzukulu za Bebai | 628 |
17 Zidzukulu za Azigadi | 2,322 |
18 Zidzukulu za Adonikamu | 667 |
19 Zidzukulu za Abigivai | 2,067 |
20 Zidzukulu za Adini | 655 |
21 Zidzukulu za Ateri (kudzera mwa Hezekiya) | 98 |
22 Zidzukulu za Hasumu | 328 |
23 Zidzukulu za Bezayi | 324 |
24 Zidzukulu za Harifu | 112 |
25 Zidzukulu za Gibiyoni | 95. |
26 Anthu a ku Betelehemu ndi Netofa | 188 |
27 Anthu a ku Anatoti | 128 |
28 Anthu a ku Beti-Azimaveti | 42 |
29 Anthu a ku Kiriati Yeyarimu Kefira ndi Beeroti | 743 |
30 Anthu a ku Rama ndi Geba | 621 |
31 Anthu a ku Mikimasi | 122 |
32 Anthu a ku Beteli ndi Ai | 123 |
33 Anthu a ku Nebo winayo | 52 |
34 Ana a Elamu wina | 1,254 |
35 Zidzukulu za Harimu | 320 |
36 Zidzukulu za Yeriko | 345 |
37 Zidzukulu za Lodi, Hadidi ndi Ono | 721 |
38 Zidzukulu za Senaya | 3,930. |
39 Ansembe anali awa:
A banja la Yedaya (ndiye kuti zidzukulu za Yesuwa) | 973 |
40 Zidzukulu za Imeri | 1,052 |
41 Zidzukulu za Pasi-Huri | 1,247 |
42 Zidzukulu za Harimu | 1,017. |
43 Alevi anali awa:
A banja la Yesuwa ndi Kadimieli, ndiye kuti zidzukulu za Hodaviya | 74. |
44 Anthu oyimba:
Zidzukulu za Asafu | 148. |
45 Alonda a ku Nyumba ya Mulungu anali awa:
Zidzukulu za | |
Salumu, Ateri, Talimoni, Hatita ndi Sobai | 138. |
46 Anthu ogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu anali awa:
Zidzukulu za |
Ziha, zidzukulu za Hasufa, zidzukulu za Tabaoti, |
47 Zidzukulu Kerosi, zidzukulu za Siya, zidzukulu za Padoni |
48 Zidzukulu za Lebana za Hagaba, ndi za Salimayi, |
49 Zidzukulu za Hanani, zidzukulu za Gideli, zidzukulu za Gahari, |
50 Zidzukulu za Reyaya, zidzukulu za Rezini, zidzukulu za Nehoda, |
51 Zidzukulu za Gazamu, zidzukulu za Uza, zidzukulu za Paseya, |
52 Zidzukulu za Besai, zidzukulu za Meunimu, zidzukulu za Nefusimu, |
53 Zidzukulu za Bakibuku, zidzukulu za Hakufa, zidzukulu za Harihuri, |
54 Zidzukulu za Baziliti, zidzukulu za Mehida, zidzukulu za Harisa, |
55 Zidzukulu za Barikosi, zidzukulu za Sisera, zidzukulu za Tema |
56 Zidzukulu za Neziya, ndi zidzukulu za Hatifa. |
57 Zidzukulu za antchito a Solomoni:
Zidzukulu za | |
Sotai, zidzukulu za Sofereti, zidzukulu za Perida | |
58 zidzukulu za Yaala, zidzukulu za Darikoni, zidzukulu za Gideli, | |
59 zidzukulu za Sefatiya, zidzukulu za Hatilu | |
zidzukulu za Pokereti-Hazebaimu ndi zidzukulu Amoni. | |
60 Anthu onse ogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu pamodzi ndi zidzukulu za antchito a Solomoni analipo | 392. |
61 Ali munsiwa anachokera ku Teli-Mela, Teri-Harisa, Kerubi, Adoni, ndi Imeri, koma sanathe kunena mwa tchutchutchu kuti makolo awo kapena mafuko awo analidi Aisraeli kapena ayi.
62 Zidzukulu za | |
Delaya, zidzukulu za Tobiya ndi zidzukulu za Nekoda | 642. |
63 Ndiponso ena pakati pa ansembe anali awa:
zidzukulu za
Hobiya, zidzukulu za Hakozi ndi zidzukulu za Barizilai (munthu amene anakwatira mwana wamkazi wa Barizilai wa ku Giliyadi ndipo amatchedwa dzina limenelo).
64 Iwowa anafufuzafufuza mayina awo mʼbuku la mibado ya mabanja awo ndipo sanapeze mayina awo kotero anachotsedwa pa unsembe nawerengedwa ngati odetsedwa pa chipembedzo. 65 Choncho bwanamkubwa anawawuza anthuwo kuti asamadye nawo chakudya china chilichonse choperekedwa kwa Mulungu mpaka patapezeka wansembe wodziwa kugwiritsa bwino ntchito ya Urimu ndi Tumimu.
66 Chiwerengero chonse cha anthuwa chinali 42,360. 67 Kuwonjezera pamenepa panali antchito awo aamuna ndi aakazi 7,337 ndiponso anthu aamuna ndi aakazi oyimba nyimbo okwanira 245. 68 Panali akavalo 736, abulu angʼonoangʼono 245. 69 Ngamira zawo zinalipo 435 ndipo abulu analipo 6,720.
70 Atsogoleri ena a mabanja anapereka mphatso zothandizira ntchito. Bwanamkubwa anapereka ku thumba losungira chuma, ndalama zagolide za makilogalamu asanu ndi atatu, mabeseni makumi asanu ndi zovala za ansembe 530. 71 Atsogoleri ena amabanja anapereka ku thumba losungira chuma ndalama zagolide zokwana makilogalamu 168, ndiponso ndalama za siliva zokwana makilogalamu 1,250. 72 Anthu ena onse otsala anapereka ndalama zagolide zokwana makilogalamu 168, ndalama za siliva zokwana makilogalamu 140, ndiponso zovala za ansembe 67.
73 Choncho ansembe, Alevi, alonda a Nyumba ya Mulungu, anthu oyimba nyimbo, ena mwa anthu wamba, ogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu pamodzi ndi Aisraeli ena onse ankakhala mʼmizinda yawo.
Ezara Awerenga Malamulo
Pofika mwezi wachisanu ndi chiwiri Aisraeli onse anali atakhazikika mʼmizinda yawo.
Nehemiah 7
New International Version
7 After the wall had been rebuilt and I had set the doors in place, the gatekeepers,(A) the musicians(B) and the Levites(C) were appointed. 2 I put in charge of Jerusalem my brother Hanani,(D) along with Hananiah(E) the commander of the citadel,(F) because he was a man of integrity and feared(G) God more than most people do. 3 I said to them, “The gates of Jerusalem are not to be opened until the sun is hot. While the gatekeepers are still on duty, have them shut the doors and bar them. Also appoint residents of Jerusalem as guards, some at their posts and some near their own houses.”
The List of the Exiles Who Returned(H)
4 Now the city was large and spacious, but there were few people in it,(I) and the houses had not yet been rebuilt. 5 So my God put it into my heart to assemble the nobles, the officials and the common people for registration by families. I found the genealogical record of those who had been the first to return. This is what I found written there:
6 These are the people of the province who came up from the captivity of the exiles(J) whom Nebuchadnezzar king of Babylon had taken captive (they returned to Jerusalem and Judah, each to his own town, 7 in company with Zerubbabel,(K) Joshua, Nehemiah, Azariah, Raamiah, Nahamani, Mordecai, Bilshan, Mispereth, Bigvai, Nehum and Baanah):
The list of the men of Israel:
8 the descendants of Parosh | 2,172 |
9 of Shephatiah | 372 |
10 of Arah | 652 |
11 of Pahath-Moab (through the line of Jeshua and Joab) | 2,818 |
12 of Elam | 1,254 |
13 of Zattu | 845 |
14 of Zakkai | 760 |
15 of Binnui | 648 |
16 of Bebai | 628 |
17 of Azgad | 2,322 |
18 of Adonikam | 667 |
19 of Bigvai | 2,067 |
20 of Adin(L) | 655 |
21 of Ater (through Hezekiah) | 98 |
22 of Hashum | 328 |
23 of Bezai | 324 |
24 of Hariph | 112 |
25 of Gibeon | 95 |
26 the men of Bethlehem and Netophah(M) | 188 |
27 of Anathoth(N) | 128 |
28 of Beth Azmaveth | 42 |
29 of Kiriath Jearim, Kephirah(O) and Beeroth(P) | 743 |
30 of Ramah and Geba | 621 |
31 of Mikmash | 122 |
32 of Bethel and Ai(Q) | 123 |
33 of the other Nebo | 52 |
34 of the other Elam | 1,254 |
35 of Harim | 320 |
36 of Jericho(R) | 345 |
37 of Lod, Hadid and Ono(S) | 721 |
38 of Senaah | 3,930 |
39 The priests:
the descendants of Jedaiah (through the family of Jeshua) | 973 |
40 of Immer | 1,052 |
41 of Pashhur | 1,247 |
42 of Harim | 1,017 |
43 The Levites:
the descendants of Jeshua (through Kadmiel through the line of Hodaviah) | 74 |
44 The musicians:(T)
the descendants of Asaph | 148 |
45 The gatekeepers:(U)
the descendants of | |
Shallum, Ater, Talmon, Akkub, Hatita and Shobai | 138 |
46 The temple servants:(V)
the descendants of |
Ziha, Hasupha, Tabbaoth, |
47 Keros, Sia, Padon, |
48 Lebana, Hagaba, Shalmai, |
49 Hanan, Giddel, Gahar, |
50 Reaiah, Rezin, Nekoda, |
51 Gazzam, Uzza, Paseah, |
52 Besai, Meunim, Nephusim, |
53 Bakbuk, Hakupha, Harhur, |
54 Bazluth, Mehida, Harsha, |
55 Barkos, Sisera, Temah, |
56 Neziah and Hatipha |
57 The descendants of the servants of Solomon:
the descendants of |
Sotai, Sophereth, Perida, |
58 Jaala, Darkon, Giddel, |
59 Shephatiah, Hattil, |
Pokereth-Hazzebaim and Amon |
60 The temple servants and the descendants of the servants of Solomon(W) | 392 |
61 The following came up from the towns of Tel Melah, Tel Harsha, Kerub, Addon and Immer, but they could not show that their families were descended from Israel:
62 the descendants of | |
Delaiah, Tobiah and Nekoda | 642 |
63 And from among the priests:
the descendants of |
Hobaiah, Hakkoz and Barzillai (a man who had married a daughter of Barzillai the Gileadite and was called by that name). |
64 These searched for their family records, but they could not find them and so were excluded from the priesthood as unclean. 65 The governor, therefore, ordered them not to eat any of the most sacred food until there should be a priest ministering with the Urim and Thummim.(X)
66 The whole company numbered 42,360, 67 besides their 7,337 male and female slaves; and they also had 245 male and female singers. 68 There were 736 horses, 245 mules,[a] 69 435 camels and 6,720 donkeys.
70 Some of the heads of the families contributed to the work. The governor gave to the treasury 1,000 darics[b] of gold, 50 bowls and 530 garments for priests. 71 Some of the heads of the families(Y) gave to the treasury for the work 20,000 darics[c] of gold and 2,200 minas[d] of silver. 72 The total given by the rest of the people was 20,000 darics of gold, 2,000 minas[e] of silver and 67 garments for priests.(Z)
73 The priests, the Levites, the gatekeepers, the musicians and the temple servants,(AA) along with certain of the people and the rest of the Israelites, settled in their own towns.(AB)
Ezra Reads the Law
When the seventh month came and the Israelites had settled in their towns,(AC)
Footnotes
- Nehemiah 7:68 Some Hebrew manuscripts (see also Ezra 2:66); most Hebrew manuscripts do not have this verse.
- Nehemiah 7:70 That is, about 19 pounds or about 8.4 kilograms
- Nehemiah 7:71 That is, about 375 pounds or about 170 kilograms; also in verse 72
- Nehemiah 7:71 That is, about 1 1/3 tons or about 1.2 metric tons
- Nehemiah 7:72 That is, about 1 1/4 tons or about 1.1 metric tons
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.
Holy Bible, New International Version®, NIV® Copyright ©1973, 1978, 1984, 2011 by Biblica, Inc.® Used by permission. All rights reserved worldwide.
NIV Reverse Interlinear Bible: English to Hebrew and English to Greek. Copyright © 2019 by Zondervan.