Add parallel Print Page Options

Kuphukira kwa Ndodo ya Aaroni

17 Yehova anawuza Mose kuti, “Yankhula ndi Aisraeli ndipo akupatse ndodo khumi ndi ziwiri, imodzi kuchokera kwa mtsogoleri wa fuko lililonse. Ulembe dzina la munthu aliyense pa ndodo yake. Pa ndodo ya Levi ulembepo dzina la Aaroni, chifukwa pafunika ndodo imodzi ya mtsogoleri pa fuko lililonse. Uyike ndodozo mu tenti ya msonkhano, kutsogolo kwa Bokosi la Umboni, kumene ndimakumana nawe. Ndodo ya munthu amene ndamusankha idzachita maluwa potero ndidzaletsa madandawulo osatha a Aisraeli otsutsana nawe.”

Choncho Mose anayankhula ndi Aisraeli, ndipo atsogoleri awo anapereka ndodo khumi ndi ziwiri, imodzi kuchokera kwa mtsogoleri wa fuko lililonse ndipo ndodo ya Aaroni inali pakati pa ndodo zawozo. Mose anayika ndodozo pamaso pa Yehova mu tenti ya msonkhano.

Pa tsiku lotsatira Mose analowa mu tenti ya msonkhanoyo ndipo anaona kuti ndodo ya Aaroni, yomwe inkayimira fuko la Levi, sinangophuka masamba chabe, komanso inachita maluwa nʼkubala zipatso za alimondi. Choncho Mose anatulutsa ndodo zonse pamaso pa Yehova napita nazo kwa Aisraeli onse. Iwowo anaziona ndipo munthu aliyense anatenga ndodo yake.

10 Yehova anawuza Mose kuti, “Bwezera ndodo ya Aaroni patsogolo pa Bokosi la Umboni, kuti chikhale chizindikiro cha kuwukira kwawo. Zimenezi zidzathetsa kudandaula kwawo kotsutsana nane, kuopa kuti angafe.” 11 Mose anachita monga Yehova anamulamulira.

12 Aisraeli anati kwa Mose, “Tikufa! Tatayika, tonse tatayika! 13 Aliyense woyandikira chihema adzafa. Kodi ndiye kuti tonse tikufa?”

The Budding of Aaron’s Staff

17 [a]The Lord said to Moses, “Speak to the Israelites and get twelve staffs(A) from them, one from the leader of each of their ancestral tribes.(B) Write the name of each man on his staff. On the staff of Levi write Aaron’s name,(C) for there must be one staff for the head of each ancestral tribe. Place them in the tent of meeting(D) in front of the ark of the covenant law,(E) where I meet with you.(F) The staff belonging to the man I choose(G) will sprout,(H) and I will rid myself of this constant grumbling(I) against you by the Israelites.”

So Moses spoke to the Israelites, and their leaders gave him twelve staffs, one for the leader of each of their ancestral tribes, and Aaron’s staff was among them. Moses placed the staffs before the Lord in the tent of the covenant law.(J)

The next day Moses entered the tent(K) and saw that Aaron’s staff,(L) which represented the tribe of Levi, had not only sprouted but had budded, blossomed and produced almonds.(M) Then Moses brought out all the staffs(N) from the Lord’s presence to all the Israelites. They looked at them, and each of the leaders took his own staff.

10 The Lord said to Moses, “Put back Aaron’s staff(O) in front of the ark of the covenant law, to be kept as a sign to the rebellious.(P) This will put an end to their grumbling against me, so that they will not die.” 11 Moses did just as the Lord commanded him.

12 The Israelites said to Moses, “We will die! We are lost, we are all lost!(Q) 13 Anyone who even comes near the tabernacle of the Lord will die.(R) Are we all going to die?”

Footnotes

  1. Numbers 17:1 In Hebrew texts 17:1-13 is numbered 17:16-28.