Add parallel Print Page Options

Ntchito za Ansembe ndi Alevi

18 Yehova anawuza Aaroni kuti, “Iwe, ana ako aamuna ndi banja la abambo ako mudzasenza tchimo la malo wopatulika, koma iwe ndi ana ako aamuna okha mudzasenza tchimo lokhudza unsembe wanu. Ubweretse Alevi, abale ako, kuchokera ku fuko la abambo ako kuti azikhala ndi iwe ndi kumakuthandiza pamodzi ndi ana ako amuna pamene mukutumikira mu tenti ya umboni. Iwowo azikutumikirani ndipo azichita ntchito zonse za ku tenti, koma asamafike pafupi ndi zipangizo za ku malo opatulika kapena guwa lansembe, kuopa kuti iwo ndi inu mungafe. Azikhala ndi inu ndipo azisamalira ntchito yonse ya mu tenti ya msonkhano koma munthu wina aliyense wapadera sayenera kufika pafupi nanu.

“Inuyo muzisamalira malo wopatulika ndi guwa lansembe, kuti ukali wa Yehova usawagwerenso Aisraeli. Ine mwini ndasankha Alevi, abale ako, pakati pa Aisraeli ngati mphatso yako ndipo aperekedwa kwa Yehova kuti azigwira ntchito ku tenti ya msonkhano. Koma iwe wekha ndi ana ako aamuna muzitumikira ngati ansembe ndi zina zonse zokhudza pa guwa lansembe ndi za mʼkati mwa malo wopatulika kwambiri. Ndikukupatsani mphatso ya utumiki wa unsembe. Aliyense woyandikira malo wopatulika ayenera kuphedwa.

Zopereka za Ansembe ndi Alevi

“Kenaka Yehova anati kwa Aaroni, ona, Ine mwini ndikukuyika kuti ukhale woyangʼanira zopereka zobwera kwa Ine; zopereka zonse zopatulika za Aisraeli zimene amapereka kwa ine ndi kuzipereka kwa iwe ndi ana ako aamuna ngati gawo lanu la nthawi zonse. Uzilandiranso gawo la zopereka zopatulika kwambiri zomwe sizinawotchedwe pa moto. Kuchokera pa mphatso zonse zimene amabweretsa kwa Ine ngati zopatulika kwambiri, nsembe zachakudya kapena nsembe zopepesera machimo, gawo limenelo ndi lako ndi ana ako aamuna. 10 Muzidya zimenezo ngati zinthu zopatulika kwambiri; mwamuna aliyense adyeko. Uzitenge kukhala zopatulika.

11 “Izinso ndi zako: chilichonse chopatulidwa kuchokera ku mphatso zoweyula za Aisraeli ndapereka kwa iwe ndi ana ako aamuna ndi aakazi ngati gawo lako la nthawi zonse. Aliyense wa mʼnyumba mwako amene ali woyeretsedwa monga mwa mwambo angathe kudyako.

12 “Ndikukupatsani mafuta onse abwino kwambiri a olivi ndi vinyo yense watsopano wabwino kwambiri ndi tirigu yense zomwe Aisraeli amapereka kwa Yehova ngati zipatso zoyamba pa zokolola zawo. 13 Zipatso zonse zoyamba kucha za mʼdziko lawo zomwe amapereka kwa Yehova zidzakhala zako. Aliyense mʼnyumba mwako amene ali woyeretsedwa angathe kudyako.

14 “Chilichonse mu Israeli chomwe chapatulidwira Yehova ndi chako. 15 Chilichonse choyamba kubadwa kwa munthu kaya nyama, chomwe chaperekedwa kwa Yehova ndi chako. Koma uyenera kuwombola mwana aliyense wamwamuna ndi mwana aliyense woyamba wa nyama zodetsedwa. 16 Pamene zili ndi mwezi umodzi wa kubadwa, uziwombole pa mtengo wowombolera wa ndalama zisanu zasiliva, monga mwa ndalama za ku malo wopatulika.

17 “Koma usawombole ana oyamba kubadwa a ngʼombe, nkhosa kapena mbuzi. Iwo ndi opatulika. Uwaze magazi a nyamazi pa guwa lansembe ndi kutentha mafuta ake ngati nsembe yotentha ndi moto kuti likhale fungo lokoma kwa Yehova. 18 Nyama yake ikhale yanu monga momwe chimakhalira chidale cha nsembe yoweyula ndi ntchafu za miyendo ya kumanja, zonsezi ndi zako. 19 Zonse zimene mwazichotsa ku zopereka zoyera zomwe Aisraeli anapereka kwa Yehova ndazipereka kwa iwe ndi ana ako aamuna ndi aakazi ngati gawo lanu nthawi zonse. Ili ndi pangano losatha la mchere pamaso pa Yehova kwa iwe ndi ana ako.”

20 Ndipo Yehova anati kwa Aaroni, “Iweyo sudzakhala ndi cholowa mʼdziko lawo, ndiponso sudzalandira gawo lililonse pakati pawo. Ine ndine gawo lako ndi cholowa chako pakati pa Aisraeli.

21 “Taonani, ndawapatsa Alevi chakhumi chonse mu Israeli ngati cholowa chawo chifukwa cha ntchito ya ku tenti ya msonkhano. 22 Kuyambira tsopano mpaka mʼtsogolo Aisraeli asamapite pafupi ndi tenti ya msonkhano. Ngati atero adzasenza zotsatira za tchimo lawo ndipo adzafa. 23 Alevi ndi amene azidzagwira ntchito ya ku tenti ya msonkhano ndipo adzalangidwa chilichonse chikalakwika. Ili ndi lamulo losatha kwa mibado yawo yonse. Iwowo sadzalandira cholowa pakati pa Aisraeli. 24 Mʼmalo mwake, ndikuwapatsa Aleviwo chakhumi ngati cholowa chawo chimene Aisraeli amapereka kwa Yehova. Nʼchifukwa chake zokhudza iwo ndinati: ‘Sadzakhala ndi cholowa pakati pa Aisraeli.’ ”

25 Yehova anati kwa Mose, 26 “Yankhula ndi Alevi ndi kunena nawo kuti, ‘Pamene mulandira chakhumi kuchoka kwa Aisraeli chimene ndimakupatsani ngati cholowa chanu, muyenera kupereka chakhumi cha choperekacho kwa Yehova. 27 Chopereka chanucho chidzawerengedwa kwa inu ngati tirigu wochokera kopunthira kapena ngati mphesa zopsinya kuchokera kopsinyira mphesa. 28 Mwa njira imeneyi inunso muzipereka chopereka kwa Yehova kuchokera ku chakhumi chanu chilichonse chimene mumalandira kuchokera kwa Aisraeli. Kuchokera ku chakhumicho muziperekako gawo la Yehova kwa Aaroni, wansembe. 29 Muyenera kupereka monga gawo la Yehova magawo abwino kwambiri ndi opatulika a chilichonse chimene chapatsidwa kwa inu.’

30 “Nena kwa Alevi: ‘Pamene mupereka gawo labwino lopambana zonse, gawo limenelo lidzawerengedwa kwa inu ngati lochokera popunthira tirigu kapenanso kopsinyira mphesa. 31 Inu ndi a pa banja panu mungathe kudyera zimenezi paliponse chifukwa ndi malipiro a ntchito yanu ya ku tenti ya msonkhano. 32 Popereka gawo labwino kwambirilo simudzapezeka olakwa. Mukatero simudzadetsa zopereka zoyera za Aisraeli, ndipo simudzafa.’ ”

Duties of Priests and Levites

18 The Lord said to Aaron, “You, your sons and your family are to bear the responsibility for offenses connected with the sanctuary,(A) and you and your sons alone are to bear the responsibility for offenses connected with the priesthood. Bring your fellow Levites from your ancestral tribe to join you and assist you when you and your sons minister(B) before the tent of the covenant law. They are to be responsible to you(C) and are to perform all the duties of the tent,(D) but they must not go near the furnishings of the sanctuary or the altar. Otherwise both they and you will die.(E) They are to join you and be responsible for the care of the tent of meeting—all the work at the tent—and no one else may come near where you are.(F)

“You are to be responsible for the care of the sanctuary and the altar,(G) so that my wrath will not fall on the Israelites again. I myself have selected your fellow Levites from among the Israelites as a gift to you,(H) dedicated to the Lord to do the work at the tent of meeting.(I) But only you and your sons may serve as priests in connection with everything at the altar and inside the curtain.(J) I am giving you the service of the priesthood as a gift.(K) Anyone else who comes near the sanctuary is to be put to death.(L)

Offerings for Priests and Levites

Then the Lord said to Aaron, “I myself have put you in charge of the offerings presented to me; all the holy offerings the Israelites give me I give to you and your sons as your portion,(M) your perpetual share.(N) You are to have the part of the most holy offerings(O) that is kept from the fire. From all the gifts they bring me as most holy offerings, whether grain(P) or sin[a](Q) or guilt offerings,(R) that part belongs to you and your sons. 10 Eat it as something most holy; every male shall eat it.(S) You must regard it as holy.(T)

11 “This also is yours: whatever is set aside from the gifts of all the wave offerings(U) of the Israelites. I give this to you and your sons and daughters as your perpetual share.(V) Everyone in your household who is ceremonially clean(W) may eat it.

12 “I give you all the finest olive oil and all the finest new wine and grain(X) they give the Lord(Y) as the firstfruits of their harvest.(Z) 13 All the land’s firstfruits that they bring to the Lord will be yours.(AA) Everyone in your household who is ceremonially clean may eat it.(AB)

14 “Everything in Israel that is devoted[b] to the Lord(AC) is yours. 15 The first offspring of every womb, both human and animal, that is offered to the Lord is yours.(AD) But you must redeem(AE) every firstborn(AF) son and every firstborn male of unclean animals.(AG) 16 When they are a month old,(AH) you must redeem them at the redemption price set at five shekels[c](AI) of silver, according to the sanctuary shekel,(AJ) which weighs twenty gerahs.(AK)

17 “But you must not redeem the firstborn of a cow, a sheep or a goat; they are holy.(AL) Splash their blood(AM) against the altar and burn their fat(AN) as a food offering, an aroma pleasing to the Lord.(AO) 18 Their meat is to be yours, just as the breast of the wave offering(AP) and the right thigh are yours.(AQ) 19 Whatever is set aside from the holy(AR) offerings the Israelites present to the Lord I give to you and your sons and daughters as your perpetual share. It is an everlasting covenant of salt(AS) before the Lord for both you and your offspring.”

20 The Lord said to Aaron, “You will have no inheritance in their land, nor will you have any share among them;(AT) I am your share and your inheritance(AU) among the Israelites.

21 “I give to the Levites all the tithes(AV) in Israel as their inheritance(AW) in return for the work they do while serving at the tent of meeting.(AX) 22 From now on the Israelites must not go near the tent of meeting, or they will bear the consequences of their sin and will die.(AY) 23 It is the Levites who are to do the work at the tent of meeting and bear the responsibility for any offenses they commit against it. This is a lasting ordinance(AZ) for the generations to come.(BA) They will receive no inheritance(BB) among the Israelites.(BC) 24 Instead, I give to the Levites as their inheritance the tithes that the Israelites present as an offering to the Lord.(BD) That is why I said concerning them: ‘They will have no inheritance among the Israelites.’”

25 The Lord said to Moses, 26 “Speak to the Levites and say to them: ‘When you receive from the Israelites the tithe I give you(BE) as your inheritance, you must present a tenth of that tithe as the Lord’s offering.(BF) 27 Your offering will be reckoned(BG) to you as grain from the threshing floor(BH) or juice from the winepress.(BI) 28 In this way you also will present an offering to the Lord from all the tithes(BJ) you receive from the Israelites. From these tithes you must give the Lord’s portion to Aaron the priest. 29 You must present as the Lord’s portion the best and holiest part of everything given to you.’

30 “Say to the Levites: ‘When you present the best part, it will be reckoned to you as the product of the threshing floor or the winepress.(BK) 31 You and your households may eat the rest of it anywhere, for it is your wages for your work at the tent of meeting.(BL) 32 By presenting the best part(BM) of it you will not be guilty in this matter;(BN) then you will not defile the holy offerings(BO) of the Israelites, and you will not die.’”

Footnotes

  1. Numbers 18:9 Or purification
  2. Numbers 18:14 The Hebrew term refers to the irrevocable giving over of things or persons to the Lord.
  3. Numbers 18:16 That is, about 2 ounces or about 58 grams