Add parallel Print Page Options

Nyimbo za Mayamiko

12 Tsiku limenelo aliyense wa inu adzati:

“Ndikukuyamikani, Inu Yehova;
    chifukwa ngakhale munandipsera mtima,
mkwiyo wanu wachoka,
    ndipo mwanditonthoza.
Zoonadi, Mulungu ndiye Mpulumutsi wanga;
    ndidzamudalira ndipo sindidzachita mantha.
Yehova ndiye mphamvu yanga ndi nyimbo yanga;
    Iye wakhala chipulumutso changa.”
Mudzakondwera popeza Yehova
    ali ngati chitsime cha chipulumutso chanu.

Tsiku limenelo mudzati:

“Yamikani Yehova, tamandani dzina lake;
    mulengeze ntchito zake pakati pa mitundu ya anthu,
    ndipo mulalike kuti dzina lake ndi lopambana.
Imbirani Yehova, pakuti wachita ntchito zazikulu;
    zimenezi zidziwike pa dziko lonse lapansi.
Fuwulani ndi kuyimba mwachimwemwe, inu anthu a ku Ziyoni;
    pakuti Woyerayo wa Israeli ndi wamkulu pakati panu.”