Yesaya 13
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
Kulangidwa Kwa Babuloni
13 Uthenga onena za Babuloni umene Yesaya mwana wa Amozi anawulandira:
2 Kwezani mbendera yankhondo pa phiri loti see,
muwafuwulire ankhondo;
muwakodole kuti adzalowe pa zipata
za anthu olemekezeka.
3 Ine Yehova, ndalamulira ankhondo anga;
ndasonkhanitsa ankhondo anga kuti akhale zida zanga zolangira
amene amadzikuza ndi chipambano changa.
4 Tamvani phokoso ku mapiri,
likumveka ngati phokoso la gulu lalikulu la anthu!
Tamvani phokoso pakati pa maufumu,
ngati kuti mitundu ya anthu ikusonkhana pamodzi!
Yehova Wamphamvuzonse akukhazika asilikali ake mokonzekera
kuchita nkhondo.
5 Iwo akuchokera ku mayiko akutali,
kuchokera kumalekezero a dziko
Yehova ali ndi zida zake za nkhondo
kuti adzawononge dziko la Babuloni.
6 Lirani mofuwula, pakuti tsiku la Yehova layandikira;
lidzabwera ngati chiwonongeko chochokera kwa Wamphamvuzonse.
7 Zimenezi zinafowoketsa manja onse,
mtima wa munthu aliyense udzachokamo.
8 Anthu adzagwidwa ndi mantha aakulu,
zowawa ndi masautso zidzawagwera;
adzamva zowawa zonga amamva mayi pobereka.
Adzayangʼanana mwamantha,
nkhope zawo zikufiira ngati malawi amoto.
9 Taonani, tsiku la Yehova likubwera,
tsiku lopanda chisoni, lawukali ndi lamkwiyo;
kudzasandutsa dziko kuti likhale chipululu
ndi kuwononga anthu ochimwa a mʼmenemo.
10 Nyenyezi zakumwamba ndiponso zonse zamlengalenga
sizidzaonetsa kuwala kwawo.
Dzuwa lidzada potuluka,
ndipo mwezi sudzawala konse.
11 Ndidzalanga dziko lonse chifukwa cha zolakwa zake,
anthu oyipa ndidzawalanga chifukwa cha machimo awo.
Ndidzathetsa kunyada kwa odzikuza,
ndipo ndidzatsitsa kudzitukumula kwa anthu ankhanza.
12 Ndidzasandutsa anthu kukhala ovuta kupeza kuposa mmene amasowera golide wabwino.
Iwo sazidzapezekapezeka kuposa mmene amasowera golide wa ku Ofiri.
13 Tsono ndidzagwedeza miyamba
ndipo dziko lapansi lidzachoka pa maziko ake.
Izi zidzachitika chifukwa cha ukali wa Wamphamvuzonse
pa tsiku la mkwiyo wake woopsa.
14 Ngati mbawala zosakidwa,
ngati nkhosa zopanda wozikusa,
munthu aliyense adzabwerera kwa anthu akwawo,
aliyense adzathawira ku dziko lake.
15 Aliyense amene atadzapezeke ndi kugwidwa
adzaphedwa momubaya ndi lupanga.
16 Ana awo akhanda adzaphwanyidwa iwo akuona;
nyumba zawo zidzafunkhidwa ndipo akazi awo adzagwiriridwa.
17 Taona, Ine ndidzadzutsa Amedi amene safuna siliva
ndipo sasangalatsidwa ndi golide,
kuti amenyane ndi Ababuloni.
18 Adzapha anyamata ndi mauta awo;
sadzachitira chifundo ana
ngakhale kumvera chisoni ana akhanda.
19 Babuloni, ufumu wake ndi waulemerero kuposa mafumu onse.
Anthu ake amawunyadira.
Koma Yehova adzawuwononga
ngati mmene anawonongera Sodomu ndi Gomora.
20 Anthu sadzakhalamonso
kapena kukhazikikamo pa mibado yonse;
palibe Mwarabu amene adzayimike tenti yake,
palibe mʼbusa amene adzawetamo ziweto zake.
21 Koma nyama zakuthengo ndizo zidzakhale kumeneko,
nyumba zake zidzadzaza ndi nkhandwe;
mu mzindamo muzidzakhala akadzidzi,
ndipo atonde akuthengo azidzalumphalumphamo.
22 Mu nsanja zake muzidzalira afisi,
mʼnyumba zake zokongola muzidzalira nkhandwe.
Nthawi yake yayandikira
ndipo masiku ake ali pafupi kutha.
Isaiah 13
New International Version
A Prophecy Against Babylon
13 A prophecy(A) against Babylon(B) that Isaiah son of Amoz(C) saw:(D)
2 Raise a banner(E) on a bare hilltop,
shout to them;
beckon to them
to enter the gates(F) of the nobles.
3 I have commanded those I prepared for battle;
I have summoned my warriors(G) to carry out my wrath(H)—
those who rejoice(I) in my triumph.
4 Listen, a noise on the mountains,
like that of a great multitude!(J)
Listen, an uproar(K) among the kingdoms,
like nations massing together!
The Lord Almighty(L) is mustering(M)
an army for war.
5 They come from faraway lands,
from the ends of the heavens(N)—
the Lord and the weapons(O) of his wrath(P)—
to destroy(Q) the whole country.
6 Wail,(R) for the day(S) of the Lord is near;
it will come like destruction(T) from the Almighty.[a](U)
7 Because of this, all hands will go limp,(V)
every heart will melt with fear.(W)
8 Terror(X) will seize them,
pain and anguish will grip(Y) them;
they will writhe like a woman in labor.(Z)
They will look aghast at each other,
their faces aflame.(AA)
9 See, the day(AB) of the Lord is coming
—a cruel(AC) day, with wrath(AD) and fierce anger(AE)—
to make the land desolate
and destroy the sinners within it.
10 The stars of heaven and their constellations
will not show their light.(AF)
The rising sun(AG) will be darkened(AH)
and the moon will not give its light.(AI)
11 I will punish(AJ) the world for its evil,
the wicked(AK) for their sins.
I will put an end to the arrogance of the haughty(AL)
and will humble(AM) the pride of the ruthless.(AN)
12 I will make people(AO) scarcer than pure gold,
more rare than the gold of Ophir.(AP)
13 Therefore I will make the heavens tremble;(AQ)
and the earth will shake(AR) from its place
at the wrath(AS) of the Lord Almighty,
in the day of his burning anger.(AT)
14 Like a hunted(AU) gazelle,
like sheep without a shepherd,(AV)
they will all return to their own people,
they will flee(AW) to their native land.(AX)
15 Whoever is captured will be thrust through;
all who are caught will fall(AY) by the sword.(AZ)
16 Their infants(BA) will be dashed to pieces before their eyes;
their houses will be looted and their wives violated.(BB)
17 See, I will stir up(BC) against them the Medes,(BD)
who do not care for silver
and have no delight in gold.(BE)
18 Their bows(BF) will strike down the young men;(BG)
they will have no mercy(BH) on infants,
nor will they look with compassion on children.(BI)
19 Babylon,(BJ) the jewel of kingdoms,(BK)
the pride and glory(BL) of the Babylonians,[b]
will be overthrown(BM) by God
like Sodom and Gomorrah.(BN)
20 She will never be inhabited(BO)
or lived in through all generations;
there no nomads(BP) will pitch their tents,
there no shepherds will rest their flocks.
21 But desert creatures(BQ) will lie there,
jackals(BR) will fill her houses;
there the owls(BS) will dwell,
and there the wild goats(BT) will leap about.
22 Hyenas(BU) will inhabit her strongholds,(BV)
jackals(BW) her luxurious palaces.
Her time is at hand,(BX)
and her days will not be prolonged.(BY)
Footnotes
- Isaiah 13:6 Hebrew Shaddai
- Isaiah 13:19 Or Chaldeans
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.
Holy Bible, New International Version®, NIV® Copyright ©1973, 1978, 1984, 2011 by Biblica, Inc.® Used by permission. All rights reserved worldwide.
NIV Reverse Interlinear Bible: English to Hebrew and English to Greek. Copyright © 2019 by Zondervan.