Add parallel Print Page Options

Israeli Wosankhidwa wa Yehova

44 Yehova akuti, “Mvera tsopano, iwe Yakobo, mtumiki wanga,
    Israeli, amene ndinakusankha.
Yehova
    amene anakupanga iwe, anakuwumba iwe mʼmimba ya amayi ako,
    ndi amene adzakuthandiza iwe. Iye akuti,
Usachite mantha, iwe Yakobo, mtumiki wanga,
    Yesuruni, amene ndinakusankha.
Pakuti ndidzathira madzi pa nthaka yowuma,
    ndi kuyendetsa mitsinje mʼdziko lowuma;
ndidzatumiza Mzimu wanga pa ana anu,
    ndi kutsitsa madalitso anga pa zidzukulu zanu.
Iwo adzakula ngati udzu wothirira bwino
    ndi ngati bango lomera mʼmbali mwa mitsinje ya madzi oyenda.
Wina adzanena kuti, ‘Ine ndine wa Yehova;’
    wina adzadzitcha yekha wa banja la Yakobo;
winanso adzalemba pa dzanja lake, ‘Wa Yehova’
    ndipo adzadzitcha wa banja la Israeli.

Yehova, Osati Mafano

“Yehova Mfumu
    ndi Mpulumutsi wa Israeli, Yehova Wamphamvuzonse akuti:
Ine ndine woyamba ndi wotsiriza;
    palibenso Mulungu wina koma Ine ndekha.
Ndani nanga angafanane ndi Ine? Muloleni kuti ayankhule.
    Muloleni andifotokozere ndi kundiyalira bwino lomwe
zimene zinachitika kuyambira pamene ndinkakhazikitsa anthu anga akalekale,
    ndi ziti zimene zidzachitike;
    inde, muloleni alosere zimene zikubwera.
Musanjenjemere, musachite mantha.
    Kodi sindinakuwuzeni zimenezi ndi kuzilosera kalekale lomwe?
Inu ndinu mboni zanga. Kodi aliponso Mulungu wina kupatula Ine?
    Ayi, palibe Thanthwe linanso limene sindikulidziwa.”

Onse amene amapanga mafano ngachabe,
    ndipo milungu imene amayilemekeza ndi yopanda phindu.
Iwo amene amapembedza mafano ndi wosaona;
    ndipo sazindikira kanthu. Choncho adzawachititsa manyazi.
10 Ndani amasema mulungu ndi kuwumba fano,
    limene silingamupindulire?
11 Iye pamodzi ndi anzake onse adzawachititsa manyazi;
    amisiri a mafano ndi anthu chabe.
Aloleni onse asonkhane ndi kuyima pabwalo la milandu;
    onse adzaopsedwa ndipo adzachita manyazi.

12 Mmisiri wa zitsulo amatenga chitsulo
    ndipo amachiyika pa makala amoto;
ndi dzanja lake lamphamvu
    amachisula pochimenya ndi nyundo.
Pambuyo pake mʼmisiri uja amamva njala natha mphamvu;
    iye samwa madzi, ndipo amalefuka.
13 Mmisiri wa matabwa nayenso amayeza mtengo ndi chingwe
    ndipo amajambula chithunzi ndi cholembera;
amasema bwinobwino ndi chipangizo chake
    ndipo amachiwongola bwino ndi chida chake.
Amachipanga ngati munthu,
    munthu wake wokongola
    kuti aliyike mʼnyumba yake yachipembedzo.
14 Amagwetsa mitengo ya mkungudza,
    mwinanso amatenga mtengo wa payini kapena wa thundu
nʼkudzisankhira mtengo wabwino pakati pa mitengo ya mʼnkhalango,
    ndipo amadzala mtengo wa payini ndi kuwuleka kuti ukule ndi mvula.
15 Mitengoyo munthu amachitako nkhuni;
    nthambi zina amasonkhera moto wowotha,
    amakolezera moto wophikira buledi
ndi mbali ina ya mtengowo amapangira mulungu ndipo amapembedza;
    iye amapanga fano ndi kumaligwadira.
16 Chigawo china cha mtengowo amasonkhera moto
    wowotcherapo nyama imene
    amadya, nakhuta.
Iye amawotha motowo ndipo amanena kuti,
    “Aa! Ndikumva kutentha; pano pali moto.”
17 Chigawo chotsala amapanga kamulungu, fano lake limenelo;
    amaligwadira ndi kulipembedza.
Amapemphera kwa fanolo ndipo amanena kuti,
    “Iwe ndiwe mulungu wanga, ndipulumutse.”
18 Anthu otere sadziwa kanthu, samvetsa kanthu kalikonse;
    maso awo ndi omatirira ndipo sangathe kuona,
    ndipo mitu yawo ndi yogontha kotero sangathe kumvetsa.
19 Palibe amene amayima nʼkulingalira.
    Palibe wanzeru kapena womvetsa zinthu bwino woti nʼkunena kuti,
chigawo china cha mtengowo ndinasonkhera moto;
    pa makala ake ndinaphikira buledi,
    ndinawotchapo nyama ndipo ndinadya.
Chigawo chotsalachi ndipangire chinthu chonyansachi.
    Kodi ndidzagwadira mtengo?
20 Munthu wotere ali ngati wodya phulusa, maganizo ake opusa amusocheretsa;
    motero kuti sangathe kudzipulumutsa yekha kapena kudzifunsa kuti,
    “Kodi chinthu chili mʼmanja mwangachi si chabodza?”

21 Yehova akuti, “Iwe Yakobo, kumbukira zinthu izi
    popeza kuti ndiwe mtumiki wanga, iwe Israeli.
Ine ndinakupanga iwe, ndiwe mtumiki wanga;
    iwe Israeli, sindidzakuyiwala.
22 Ndachotsa zolakwa zako ngati mitambo,
    ndi machimo ako ngati nkhungu ya mmawa.
Bwerera kwa Ine,
    popeza ndakupulumutsa.”

23 Imbani mwachimwemwe, inu zolengedwa zamlengalenga, pakuti Yehova wachita zimenezi;
    fuwula, iwe dziko lapansi.
Imbani nyimbo, inu mapiri,
    inu nkhalango ndi mitengo yonse,
chifukwa Yehova wawombola Yakobo,
    waonetsa ulemerero wake mwa Israeli.

Anthu Adzakhalanso mu Yerusalemu

24 Yehova Mpulumutsi wanu, amene
    anakuwumbani mʼmimba ya amayi anu akuti:

“Ine ndine Yehova,
amene anapanga zinthu zonse,
ndinatambasula ndekha zinthu zakuthambo,
ndinayala ndekha dziko lapansi.
25 Ndine amene ndinalepheretsa mipingo ya anthu onyenga,
    ndipo ndimapusitsa owombeza mawula.
Ndimasokoneza anthu a nzeru,
    ndi kuonetsa kuti nzeru zawo nʼzopusa.
26 Ndine amene ndimatsimikiza mawu a atumiki ake
    ndi kukwaniritsa zimene analosera amithenga ake.

“Ndine amene ndinanena za Yerusalemu kuti mudzakhalanso anthu.
    Ndinanenanso za mizinda ya Yuda kuti idzamangidwanso.
    Za mabwinja awo ndinanena kuti ndidzawawutsanso.
27 Ndine amene ndinawuza nyanga yayikulu kuti, ‘Uma’
    ndipo ndidzawumitsa mitsinje yako.
28 Ndine amene ndinanena kwa Koresi kuti, ‘Iye ndiye mʼbusa wanga,’
    ndipo adzachita zonse zimene ndikufuna;
    iye adzalamula kuti, ‘Yerusalemu amangidwenso’
    ndi kuti, ‘Maziko a Nyumba ya Mulungu ayikidwenso.’ ”

Israel the Chosen

44 “But now listen, Jacob, my servant,(A)
    Israel, whom I have chosen.(B)
This is what the Lord says—
    he who made(C) you, who formed you in the womb,(D)
    and who will help(E) you:
Do not be afraid,(F) Jacob, my servant,(G)
    Jeshurun,[a](H) whom I have chosen.
For I will pour water(I) on the thirsty land,
    and streams on the dry ground;(J)
I will pour out my Spirit(K) on your offspring,
    and my blessing(L) on your descendants.(M)
They will spring up like grass(N) in a meadow,
    like poplar trees(O) by flowing streams.(P)
Some will say, ‘I belong(Q) to the Lord’;
    others will call themselves by the name of Jacob;
still others will write on their hand,(R) ‘The Lord’s,’(S)
    and will take the name Israel.

The Lord, Not Idols

“This is what the Lord says—
    Israel’s King(T) and Redeemer,(U) the Lord Almighty:
I am the first and I am the last;(V)
    apart from me there is no God.(W)
Who then is like me?(X) Let him proclaim it.
    Let him declare and lay out before me
what has happened since I established my ancient people,
    and what is yet to come—
    yes, let them foretell(Y) what will come.
Do not tremble, do not be afraid.
    Did I not proclaim(Z) this and foretell it long ago?
You are my witnesses. Is there any God(AA) besides me?
    No, there is no other Rock;(AB) I know not one.”

All who make idols(AC) are nothing,
    and the things they treasure are worthless.(AD)
Those who would speak up for them are blind;(AE)
    they are ignorant, to their own shame.(AF)
10 Who shapes a god and casts an idol,(AG)
    which can profit nothing?(AH)
11 People who do that will be put to shame;(AI)
    such craftsmen are only human beings.
Let them all come together and take their stand;
    they will be brought down to terror and shame.(AJ)

12 The blacksmith(AK) takes a tool
    and works with it in the coals;
he shapes an idol with hammers,
    he forges it with the might of his arm.(AL)
He gets hungry and loses his strength;
    he drinks no water and grows faint.(AM)
13 The carpenter(AN) measures with a line
    and makes an outline with a marker;
he roughs it out with chisels
    and marks it with compasses.
He shapes it in human form,(AO)
    human form in all its glory,
    that it may dwell in a shrine.(AP)
14 He cut down cedars,
    or perhaps took a cypress or oak.
He let it grow among the trees of the forest,
    or planted a pine,(AQ) and the rain made it grow.
15 It is used as fuel(AR) for burning;
    some of it he takes and warms himself,
    he kindles a fire and bakes bread.
But he also fashions a god and worships(AS) it;
    he makes an idol and bows(AT) down to it.
16 Half of the wood he burns in the fire;
    over it he prepares his meal,
    he roasts his meat and eats his fill.
He also warms himself and says,
    “Ah! I am warm; I see the fire.(AU)
17 From the rest he makes a god, his idol;
    he bows down to it and worships.(AV)
He prays(AW) to it and says,
    “Save(AX) me! You are my god!”
18 They know nothing, they understand(AY) nothing;
    their eyes(AZ) are plastered over so they cannot see,
    and their minds closed so they cannot understand.
19 No one stops to think,
    no one has the knowledge or understanding(BA) to say,
“Half of it I used for fuel;(BB)
    I even baked bread over its coals,
    I roasted meat and I ate.
Shall I make a detestable(BC) thing from what is left?
    Shall I bow down to a block of wood?”(BD)
20 Such a person feeds on ashes;(BE) a deluded(BF) heart misleads him;
    he cannot save himself, or say,
    “Is not this thing in my right hand a lie?(BG)

21 “Remember(BH) these things, Jacob,
    for you, Israel, are my servant.(BI)
I have made you, you are my servant;(BJ)
    Israel, I will not forget you.(BK)
22 I have swept away(BL) your offenses like a cloud,
    your sins like the morning mist.
Return(BM) to me,
    for I have redeemed(BN) you.”

23 Sing for joy,(BO) you heavens, for the Lord has done this;
    shout aloud, you earth(BP) beneath.
Burst into song, you mountains,(BQ)
    you forests and all your trees,(BR)
for the Lord has redeemed(BS) Jacob,
    he displays his glory(BT) in Israel.

Jerusalem to Be Inhabited

24 “This is what the Lord says—
    your Redeemer,(BU) who formed(BV) you in the womb:(BW)

I am the Lord,
    the Maker of all things,
    who stretches out the heavens,(BX)
    who spreads out the earth(BY) by myself,
25 who foils(BZ) the signs of false prophets
    and makes fools of diviners,(CA)
who overthrows the learning of the wise(CB)
    and turns it into nonsense,(CC)
26 who carries out the words(CD) of his servants
    and fulfills(CE) the predictions of his messengers,

who says of Jerusalem,(CF) ‘It shall be inhabited,’
    of the towns of Judah, ‘They shall be rebuilt,’
    and of their ruins,(CG) ‘I will restore them,’(CH)
27 who says to the watery deep, ‘Be dry,
    and I will dry up(CI) your streams,’
28 who says of Cyrus,(CJ) ‘He is my shepherd
    and will accomplish all that I please;
he will say of Jerusalem,(CK) “Let it be rebuilt,”
    and of the temple,(CL) “Let its foundations(CM) be laid.”’

Footnotes

  1. Isaiah 44:2 Jeshurun means the upright one, that is, Israel.