Add parallel Print Page Options

Chilango cha Mulungu

Lizani lipenga mu Ziyoni.
    Chenjezani pa phiri langa loyera.
Onse okhala mʼdziko anjenjemere,
    pakuti tsiku la Yehova likubwera,
layandikira;
    tsiku la mdima ndi chisoni,
    tsiku la mitambo ndi la mdima wandiweyani.
Ngati mʼbandakucha umene wakuta mapiri,
    gulu lalikulu ndi la ankhondo amphamvu likubwera,
gulu limene nʼkale lomwe silinaonekepo
    ngakhale kutsogolo kuno silidzaonekanso.
Patsogolo pawo moto ukupsereza,
    kumbuyo kwawo malawi amoto akutentha zinthu.
Patsogolo pawo dziko lili ngati munda wa Edeni,
    kumbuyo kwawo kuli ngati chipululu,
    kulibe kanthu kotsalapo.
Maonekedwe awo ali ngati akavalo;
    akuthamanga ngati akavalo ankhondo.
Akulumpha pamwamba pa mapiri
    ndi phokoso ngati la magaleta,
ngati moto wothetheka wonyeketsa ziputu,
    ngati gulu lalikulu la ankhondo lokonzekera nkhondo.

Akangowaona, anthu a mitundu ina amazunzika mu mtima;
    nkhope iliyonse imagwa.
Amathamanga ngati ankhondo;
    amakwera makoma ngati asilikali.
Onse amayenda pa mizere,
    osaphonya njira yawo.
Iwo sakankhanakankhana,
    aliyense amayenda molunjika.
Amadutsa malo otchingidwa
    popanda kumwazikana.
Amakhamukira mu mzinda,
    amathamanga mʼmbali mwa khoma.
Amakwera nyumba ndi kulowamo;
    amalowera pa zenera ngati mbala.

10 Patsogolo pawo dziko limagwedezeka,
    thambo limanjenjemera,
dzuwa ndi mwezi zimachita mdima,
    ndipo nyenyezi zimaleka kuwala.
11 Yehova amabangula
    patsogolo pawo,
gulu lake lankhondo ndi losawerengeka,
    ndipo amphamvu ndi amene amamvera kulamula kwake.
Tsiku la Yehova ndi lalikulu;
    ndi loopsa.
    Ndani adzapirira pa tsikulo?

Ngʼambani Mtima Wanu

12 “Ngakhale tsopano,
    bwererani kwa Ine ndi mtima wanu wonse
    posala zakudya ndi kukhetsa misozi,” akutero Yehova.

13 Ngʼambani mtima wanu
    osati zovala zanu.
Bwererani kwa Yehova Mulungu wanu,
    pakuti Iye ndi wokoma mtima ndi wachifundo,
wosakwiya msanga ndi wachikondi chochuluka,
    ndipo amaleka kubweretsa mavuto.
14 Akudziwa ndani? Mwina adzasintha maganizo nʼkutimvera chisoni,
    nʼkutisiyira madalitso,
a chopereka cha chakudya ndi cha chakumwa
    kwa Yehova Mulungu wanu.

15 Lizani lipenga mu Ziyoni,
    lengezani tsiku losala zakudya,
    itanitsani msonkhano wopatulika.
16 Sonkhanitsani anthu pamodzi,
    muwawuze kuti adziyeretse;
sonkhanitsani akuluakulu,
    sonkhanitsani ana,
    sonkhanitsani ndi oyamwa omwe.
Mkwati atuluke mʼchipinda chake,
    mkwatibwi atuluke mokhala mwake.
17 Ansembe amene amatumikira pamaso pa Yehova,
    alire pakati pa guwa lansembe ndi khonde la Nyumba ya Yehova.
Azinena kuti, “Inu Yehova, achitireni chifundo anthu anu.
    Musalole kuti cholowa chanu chikhale chinthu chonyozeka,
    kuti anthu a mitundu ina awalamulire.
Kodi nʼchifukwa chiyani anthu a mitundu ina amanena kuti,
    ‘Ali kuti Mulungu wawo?’ ”

Yankho la Yehova

18 Pamenepo Yehova adzachitira nsanje dziko lake
    ndi kuchitira chisoni anthu ake.

19 Yehova adzawayankha kuti,

“Ine ndikukutumizirani tirigu, vinyo watsopano ndi mafuta
    ndipo mudzakhuta ndithu;
sindidzakuperekaninso kuti mukhale chitonzo
    kwa anthu a mitundu ina.

20 “Ine ndidzachotsa ankhondo akumpoto kuti apite kutali ndi inu,
    kuwapirikitsira ku dziko lowuma ndi lachipululu,
gulu lawo lakutsogolo ndidzalipirikitsira ku nyanja ya kummawa
    ndi gulu lawo lakumbuyo, ku nyanja ya kumadzulo.
Ndipo mitembo yawo idzawola,
    fungo lake lidzamveka.”

Zoonadi Yehova wachita zinthu zazikulu.
21     Iwe dziko usachite mantha;
    sangalala ndipo kondwera.
Zoonadi Yehova wachita zinthu zazikulu.
22     Inu nyama zakuthengo, musachite mantha,
    pakuti msipu wa ku chipululu ukuphukira.
Mitengo ikubala zipatso zake;
    mitengo ya mkuyu ndi mpesa ikubereka kwambiri.
23 Inu anthu a ku Ziyoni sangalalani,
    kondwerani mwa Yehova Mulungu wanu,
pakuti wakupatsani
    mvula yoyambirira mwachilungamo chake.
Iye wakutumizirani mivumbi yochuluka,
    mvula yoyambirira ndi mvula ya nthawi ya mphukira, monga poyamba paja.
24 Pa malo opunthira padzaza tirigu;
    mʼmitsuko mudzasefukira vinyo watsopano ndi mafuta.

25 “Ine ndidzakubwezerani zonse zimene zinawonongedwa ndi dzombe,
    dzombe lalikulu ndi dzombe lalingʼono,
    dzombe lopanda mapiko ndi dzombe lowuluka;
gulu langa lalikulu la nkhondo limene ndinalitumiza pakati panu.
26 Mudzakhala ndi chakudya chambiri, mpaka mudzakhuta,
    ndipo mudzatamanda dzina la Yehova Mulungu wanu,
    amene wakuchitirani zodabwitsa;
ndipo anthu anga sadzachitanso manyazi.
27 Pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine ndili mu Israeli,
    kuti Ine ndine Yehova Mulungu wanu,
    ndi kuti palibenso wina;
ndipo anthu anga sadzachitanso manyazi.

Tsiku la Yehova

28 “Ndipo patapita nthawi,
    ndidzakhuthulira Mzimu wanga pa anthu onse.
Ana anu aamuna ndi ana anu aakazi adzanenera,
    nkhalamba zanu zidzalota maloto,
    anyamata anu adzaona masomphenya.
29 Ngakhalenso pa antchito anga aamuna ndi aakazi
    ndidzakhuthulira Mzimu wanga masiku amenewo.
30 Ndidzaonetsa zodabwitsa mlengalenga
    ndi pa dziko lapansi,
    ndizo magazi, moto ndi utsi watolotolo.
31 Dzuwa lidzadetsedwa
    ndipo mwezi udzaoneka ngati magazi
    lisanafike tsiku lalikulu ndi loopsa la Ambuye.
32 Ndipo aliyense amene adzayitana
    pa dzina la Ambuye adzapulumuka;
pakuti chipulumutso chidzakhala pa Phiri la Ziyoni
    ndi mu Yerusalemu,
    monga Yehova wanenera,
pakati pa otsala
    amene Yehova wawayitana.

An Army of Locusts

Blow the trumpet(A) in Zion;(B)
    sound the alarm on my holy hill.(C)

Let all who live in the land tremble,
    for the day of the Lord(D) is coming.
It is close at hand(E)
    a day of darkness(F) and gloom,(G)
    a day of clouds(H) and blackness.(I)
Like dawn spreading across the mountains
    a large and mighty army(J) comes,
such as never was in ancient times(K)
    nor ever will be in ages to come.

Before them fire(L) devours,
    behind them a flame blazes.
Before them the land is like the garden of Eden,(M)
    behind them, a desert waste(N)
    nothing escapes them.
They have the appearance of horses;(O)
    they gallop along like cavalry.
With a noise like that of chariots(P)
    they leap over the mountaintops,
like a crackling fire(Q) consuming stubble,
    like a mighty army drawn up for battle.

At the sight of them, nations are in anguish;(R)
    every face turns pale.(S)
They charge like warriors;(T)
    they scale walls like soldiers.
They all march in line,(U)
    not swerving(V) from their course.
They do not jostle each other;
    each marches straight ahead.
They plunge through defenses
    without breaking ranks.
They rush upon the city;
    they run along the wall.
They climb into the houses;(W)
    like thieves they enter through the windows.(X)

10 Before them the earth shakes,(Y)
    the heavens tremble,(Z)
the sun and moon are darkened,(AA)
    and the stars no longer shine.(AB)
11 The Lord(AC) thunders(AD)
    at the head of his army;(AE)
his forces are beyond number,
    and mighty is the army that obeys his command.
The day of the Lord is great;(AF)
    it is dreadful.
    Who can endure it?(AG)

Rend Your Heart

12 “Even now,” declares the Lord,
    “return(AH) to me with all your heart,(AI)
    with fasting and weeping and mourning.”

13 Rend your heart(AJ)
    and not your garments.(AK)
Return(AL) to the Lord your God,
    for he is gracious and compassionate,(AM)
slow to anger and abounding in love,(AN)
    and he relents from sending calamity.(AO)
14 Who knows? He may turn(AP) and relent(AQ)
    and leave behind a blessing(AR)
grain offerings and drink offerings(AS)
    for the Lord your God.

15 Blow the trumpet(AT) in Zion,(AU)
    declare a holy fast,(AV)
    call a sacred assembly.(AW)
16 Gather the people,
    consecrate(AX) the assembly;
bring together the elders,(AY)
    gather the children,
    those nursing at the breast.
Let the bridegroom(AZ) leave his room
    and the bride her chamber.
17 Let the priests, who minister(BA) before the Lord,
    weep(BB) between the portico and the altar.(BC)
Let them say, “Spare your people, Lord.
    Do not make your inheritance an object of scorn,(BD)
    a byword(BE) among the nations.
Why should they say among the peoples,
    ‘Where is their God?(BF)’”

The Lord’s Answer

18 Then the Lord was jealous(BG) for his land
    and took pity(BH) on his people.

19 The Lord replied[a] to them:

“I am sending you grain, new wine(BI) and olive oil,(BJ)
    enough to satisfy you fully;(BK)
never again will I make you
    an object of scorn(BL) to the nations.

20 “I will drive the northern horde(BM) far from you,
    pushing it into a parched and barren land;
its eastern ranks will drown in the Dead Sea
    and its western ranks in the Mediterranean Sea.
And its stench(BN) will go up;
    its smell will rise.”

Surely he has done great things!
21     Do not be afraid,(BO) land of Judah;
    be glad and rejoice.(BP)
Surely the Lord has done great things!(BQ)
22     Do not be afraid, you wild animals,
    for the pastures in the wilderness are becoming green.(BR)
The trees are bearing their fruit;
    the fig tree(BS) and the vine(BT) yield their riches.(BU)
23 Be glad, people of Zion,
    rejoice(BV) in the Lord your God,
for he has given you the autumn rains
    because he is faithful.(BW)
He sends you abundant showers,(BX)
    both autumn(BY) and spring rains,(BZ) as before.
24 The threshing floors will be filled with grain;
    the vats will overflow(CA) with new wine(CB) and oil.

25 “I will repay you for the years the locusts(CC) have eaten(CD)
    the great locust and the young locust,
    the other locusts and the locust swarm[b]
my great army(CE) that I sent among you.
26 You will have plenty to eat, until you are full,(CF)
    and you will praise(CG) the name of the Lord your God,
    who has worked wonders(CH) for you;
never again will my people be shamed.(CI)
27 Then you will know(CJ) that I am in Israel,
    that I am the Lord(CK) your God,
    and that there is no other;
never again will my people be shamed.(CL)

The Day of the Lord

28 “And afterward,
    I will pour out my Spirit(CM) on all people.(CN)
Your sons and daughters will prophesy,(CO)
    your old men will dream dreams,(CP)
    your young men will see visions.
29 Even on my servants,(CQ) both men and women,
    I will pour out my Spirit in those days.(CR)
30 I will show wonders in the heavens(CS)
    and on the earth,(CT)
    blood and fire and billows of smoke.
31 The sun will be turned to darkness(CU)
    and the moon to blood
    before the coming of the great and dreadful day of the Lord.(CV)
32 And everyone who calls
    on the name of the Lord(CW) will be saved;(CX)
for on Mount Zion(CY) and in Jerusalem
    there will be deliverance,(CZ)
    as the Lord has said,
even among the survivors(DA)
    whom the Lord calls.[c](DB)

Footnotes

  1. Joel 2:19 Or Lord will be jealous … / and take pity … / 19 The Lord will reply
  2. Joel 2:25 The precise meaning of the four Hebrew words used here for locusts is uncertain.
  3. Joel 2:32 In Hebrew texts 2:28-32 is numbered 3:1-5.