Add parallel Print Page Options

Yehova Adzasamalira Yuda

10 Pemphani mvula kwa Yehova pa nthawi yamphukira;
    ndi Yehova amene amapanga mitambo ya mvula.
Iye amagwetsa mivumbi ya mvula kwa anthu,
    ndi kumeretsa mbewu za mʼmunda kwa aliyense.
Mafano amayankhula zachinyengo,
    owombeza mawula amaona masomphenya abodza;
amafotokoza maloto onama,
    amapereka chitonthozo chopandapake.
Choncho anthu amangoyendayenda ngati nkhosa zozunzika
    chifukwa chosowa mʼbusa.

“Ine ndawakwiyira kwambiri abusa,
    ndipo ndidzalanga atsogoleri;
pakuti Yehova Wamphamvuzonse adzasamalira
    nkhosa zake, nyumba ya Yuda,
    ndi kuwasandutsa ngati akavalo aulemerero ankhondo.
Mu Yuda mudzachokera mwala wapangodya,
    mudzachokera chikhomo cha tenti,
    mudzachokera uta wankhondo,
    mudzachokera mtsogoleri aliyense.
Onse pamodzi adzakhala ngati ngwazi zankhondo
    zoponda mʼmatope a mʼmisewu nthawi yankhondo.
Chifukwa Yehova adzakhala nawo,
    adzachita nkhondo ndi kugonjetsa okwera pa akavalo.

“Ndidzalimbitsa nyumba ya Yuda
    ndi kupulumutsa nyumba ya Yosefe.
Ndidzawabwezeretsa
    chifukwa ndawamvera chisoni.
Adzakhala ngati kuti
    sindinawakane,
chifukwa ndine Yehova Mulungu wawo
    ndipo ndidzawayankha.
Aefereimu adzakhala ngati ankhondo amphamvu
    adzasangalala ngati anthu amene amwa vinyo.
Ana awo adzaziona zimenezi ndipo adzasangalala;
    mʼmitima mwawo adzakondwa mwa Ambuye.
Ndidzaliza mluzu
    ndi kuwasonkhanitsa pamodzi.
Ndithu ndawawombola;
    adzachulukana ngati poyamba paja.
Ndinawamwaza pakati pa mitundu ina ya anthu,
    koma ku mayiko akutaliwo adzandikumbukira.
Iwo pamodzi ndi ana awo adzapulumuka,
    ndipo adzabwerera.
10 Ndidzawabweretsa kuchokera ku Igupto
    ndipo ndidzawasonkhanitsa kuchokera ku Asiriya.
Ndidzawabwezera ku Giliyadi ndi ku Lebanoni,
    mpaka malo woti nʼkukhalamo adzatheratu.
11 Adzawoloka nyanja ya masautso;
    nyanja yokokoma idzagonja
    ndipo madzi onse a mu Nailo adzaphwa.
Kudzikuza kwa Asiriya kudzatha
    ndipo ndodo yaufumu ya Igupto idzathyoka.
12 Ndidzalimbitsa iwo mwa Yehova
    ndipo adzayenda mʼdzina lake,”
            akutero Yehova.